阿摩司书 2 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

阿摩司书 2:1-16

对摩押的审判

1耶和华说:

摩押人三番四次地犯罪,

我必不收回对他们的惩罚,

因为他们把以东王的骸骨焚烧成灰。

2所以我要降火在摩押

烧毁加略的城堡。

摩押要在战争的喧嚣、吶喊和号角声中灭亡。

3我要铲除摩押的君王,

杀死那里所有的首领。

这是耶和华说的。”

对犹大的审判

4耶和华说:

犹大人三番四次地犯罪,

我必不收回对他们的惩罚,

因为他们厌弃耶和华的训诲,

不遵守我的律例。

他们祖先祭拜的偶像使他们走入歧途。

5所以我要降火在犹大

烧毁耶路撒冷的城堡。”

对以色列的审判

6耶和华说:

以色列人三番四次地犯罪,

我必不收回对他们的惩罚,

因为他们为了银子卖掉义人,

为了一双鞋子卖掉穷人。

7他们践踏穷人如同践踏地上的尘土,

使卑微的人无处申冤;

父子同淫一女,亵渎我的圣名。

8在每座祭坛旁边,

他们把穷人典当的衣服铺开,躺在上面,

又在上帝的殿里喝剥削来的酒。

9以色列人啊,

我在你们面前消灭了亚摩利人。

虽然他们像香柏树那样高大,

如橡树那样强壮,

但我灭尽了他们的果子,

砍断了他们的根。

10我带领你们离开埃及

在旷野引导你们四十年,

使你们得到亚摩利人的土地。

11我从你们的子孙中拣选先知,

从你们的青年中拣选拿细耳2:11 拿细耳人的详情参见民数记6:1-8

以色列人啊,难道不是这样吗?

这是耶和华说的。

12可是,你们迫使拿细耳人喝酒,

禁止先知传达我的话。

13看啊,我要压碎你们,

如满载谷物的车轧过一样。

14快捷的无法逃遁,

强壮的无力可施,

勇猛的救不了自己,

15拉弓的站立不住,

腿快的无法逃脱,

骑马的救不了自己。

16到那日,

最勇猛的战士也要丢盔弃甲,仓皇逃命。

这是耶和华说的。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 2:1-16

1Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu,

mpaka kuwasandutsa phulusa,

2Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu,

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti.

Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa,

mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.

3Ndidzawononga wolamulira wake

ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,”

akutero Yehova.

4Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza iwo akana lamulo la Yehova

ndipo sanasunge malangizo ake,

popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza,

milungu imene makolo awo ankayitsatira,

5Ine ndidzatumiza moto pa Yuda,

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”

Chilango cha Anthu a ku Israeli

6Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva,

ndi osauka ndi nsapato.

7Amapondereza anthu osauka

ngati akuponda fumbi,

ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa.

Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo,

ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.

8Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe

pa zovala zimene anatenga ngati chikole.

Mʼnyumba ya mulungu wawo

amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.

9“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo,

ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza

ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu.

Ndinawononga zipatso zawo

ndiponso mizu yawo.

10“Ine ndinakutulutsani ku Igupto,

ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi,

kudzakupatsani dziko la Aamori.

11Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri,

ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri.

Kodi si choncho, inu Aisraeli?”

akutero Yehova.

12“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja,

ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.

13“Tsono Ine ndidzakupsinjani

monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.

14Munthu waliwiro sadzatha kuthawa,

munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga,

wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.

15Munthu wa uta sadzalimbika,

msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka,

ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.

16Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri

adzathawa ali maliseche pa tsikulo,”

akutero Yehova.