阿摩司书 1 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

阿摩司书 1:1-15

1犹大乌西雅约阿施的儿子以色列耶罗波安执政期间,大地震前两年,提哥亚的牧人阿摩司看到了关于以色列的异象。以下是阿摩司的话。

2他说:

“耶和华在锡安1:2 锡安”位于耶路撒冷北部,即大卫城,有时用来指耶路撒冷。怒吼,

在耶路撒冷呼喊。

牧人的草场枯干,

迦密山顶枯黄。”

对亚兰的审判

3耶和华说:

大马士革人三番四次地犯罪,

我必不收回对他们的惩罚,

因为他们用打粮食的铁器蹂躏基列

4所以我要降火在哈薛王家,

烧毁便·哈达王的城堡。

5我要折断大马士革城的门闩,

铲除亚文平原1:5 亚文平原”希伯来文是“邪恶谷”。亚文平原和伯·伊甸皆属于亚兰人。的居民和伯·伊甸的掌权者,

使亚兰人被掳到吉珥1:5 吉珥的位置不详,亚兰人原来自吉珥。

这是耶和华说的。”

对非利士的审判

6耶和华说:

迦萨人三番四次地犯罪,

我必不收回对他们的惩罚,

因为他们把被掳之人全都带走,

卖到以东做奴隶。

7所以,我要降火在迦萨的城墙上,

烧毁它的城堡。

8我要铲除亚实突的居民和亚实基伦的掌权者,

伸手攻击以革伦

剩下的非利士人都要灭亡。

这是主耶和华说的。”

对泰尔的审判

9耶和华说:

泰尔人三番四次地犯罪,

我必不收回对他们的惩罚,

因为他们背弃弟兄之盟,

把被掳之人都卖到以东

10所以,我要降火在泰尔的城墙上,

烧毁它的城堡。”

对以东的审判

11耶和华说:

以东人三番四次地犯罪,

我必不收回对他们的惩罚,

因为他们拔刀追赶自己的弟兄,

没有半点怜悯之心;

他们怒气不息,永怀愤怒。

12所以,我要降火在提幔

烧毁波斯拉的城堡。”

对亚扪的审判

13耶和华说:

亚扪人三番四次地犯罪,

我必不收回对他们的惩罚,

因为他们为了扩张领土,

竟剖开基列孕妇的肚腹。

14所以,我要在战争的吶喊声中,

在暴风雨吹袭的时候,

降火在拉巴的城墙上,

烧毁它的城堡。

15他们的君王和首领都要被掳。

这是耶和华说的。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 1:1-15

1Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.

2Amosi anati:

“Yehova akubangula mu Ziyoni

ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu;

msipu wa abusa ukulira,

ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”

Chiweruzo pa Anthu Oyandikana ndi Israeli

3Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anapuntha Giliyadi

ndi zopunthira za mano achitsulo,

4Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.

5Ndidzathyola chipata cha Damasiko;

ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni,

ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni.

Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,”

akutero Yehova.

6Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu

ndi kuwugulitsa ku Edomu,

7ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

8Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi

komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni.

Ndidzalanga Ekroni,

mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,”

akutero Ambuye Yehova.

9Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu,

osasunga pangano laubale lija,

10Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”

11Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,

popanda nʼchifundo chomwe.

Popeza mkwiyo wake unakulabe

ndipo ukali wake sunatonthozeke,

12Ine ndidzatumiza moto pa Temani

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”

13Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi

nʼcholinga choti akuze malire awo,

14Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo,

kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.

15Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo,

iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,”

akutero Yehova.