俄巴底亚书 1 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

俄巴底亚书 1:1-21

1俄巴底亚看到的异象。

耶和华惩罚以东

论到以东

主耶和华这样说:

“我们从耶和华那里听到消息,

有位使者被派到各国,说,

‘来!我们去攻打以东吧!’”

2耶和华对以东说:

“我要让你成为列国中最弱小的国家,

使你饱受藐视。

3你住在悬崖峭壁间,

住在高山上,

自以为谁也不能把你拉下来,

但你的骄傲欺骗了你。

4即使你如鹰高飞,

在星辰间筑巢,

我也必把你拉下来。

这是耶和华说的。

5“盗贼深夜洗劫你的家,

不会洗劫一空;

人们摘葡萄,不会摘光;

但你会被彻底毁灭!

6以扫1:6 以扫”又名“以东”。要被洗劫一空,

他藏的珍宝要被搜去。

7你的盟友将你逐出家园;

你的朋友欺骗你,战胜你;

你的知己设陷阱害你,

你却懵然不知。”

8耶和华说:“到那天,

我要毁灭以东的智者,

除掉以扫山上的明哲。

9提幔的勇士必惊慌失措,

以扫山上的人尽遭杀戮。

惩罚以东的原因

10“因你曾残暴地对待同胞兄弟雅各

你必蒙羞,永遭毁灭。

11外族人掠夺雅各的财物,

攻入耶路撒冷抽签分赃时,

你竟然袖手旁观,

就像他们的同伙一样。

12你的亲族遭难之日,

你不该幸灾乐祸;

犹大人被灭的日子,

你不该兴高采烈;

他们遭难的日子,

你不该口出狂言;

13我子民遭难的日子,

你不该闯进他们的城;

他们遭难的日子,

你不该幸灾乐祸;

他们遭难的日子,

你不该趁火打劫;

14你不该站在路口截杀那些逃亡者;

他们遭难的日子,

你不该把幸存者交给仇敌。

15“耶和华惩罚万国的日子近了。

必按你的所作所为报应你,

你的恶行必落到自己头上。

16你们犹大人在我的圣山上怎样饱饮愤怒,

万国也要照样饮,

且要大口吞下,

直到他们完全消逝。

以色列的复兴

17“然而,锡安山必成为避难所,

成为圣地。

雅各家必得到自己的产业。

18雅各家将成为火,

约瑟家将成为烈焰,

以扫家将成为碎秸,

被火焚烧、吞噬,无一人逃脱。

这是耶和华说的。

19“南地的人将占领以扫山;

丘陵的人将占领非利士

夺取以法莲撒玛利亚

便雅悯人将占领基列

20被掳的以色列人将返回家园,

占领远至撒勒法一带的土地;

耶路撒冷被掳到西法拉的人将占领南地各城。

21拯救者必登上锡安山,

统治以扫山,

耶和华必做王掌权。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Obadiya 1:1-21

Masomphenya a Obadiya

1Masomphenya a Obadiya.

Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,

Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:

Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,

“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”

2“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;

udzanyozedwa kwambiri.

3Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,

iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe

ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,

iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,

‘Ndani anganditsitse pansi?’

4Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga

ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,

ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”

akutero Yehova.

5“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,

kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,

aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!

Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?

Ngati anthu othyola mphesa akanafika,

kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?

6Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,

chuma chake chobisika chidzabedwa!

7Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;

abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;

amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,

koma iwe sudzazindikira zimenezi.”

8Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,

kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,

anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?

9Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,

ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau

adzaphedwa pa nkhondo.

10Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,

udzakhala wamanyazi;

adzakuwononga mpaka muyaya.

11Pamene adani

ankamulanda chuma chake

pamene alendo analowa pa zipata zake

ndi kuchita maere pa Yerusalemu,

pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.

12Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako

pa nthawi ya tsoka lake,

kapena kunyogodola Ayuda

chifukwa cha chiwonongeko chawo,

kapena kuwaseka pa nthawi ya

mavuto awo.

13Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga

pa nthawi ya masautso awo,

kapena kuwanyogodola

pa tsiku la tsoka lawo,

kapena kulanda chuma chawo

pa nthawi ya masautso awo.

14Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu

kuti uphe Ayuda othawa,

kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka

pa nthawi ya mavuto awo.”

15“Tsiku la Yehova layandikira

limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.

Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;

zochita zako zidzakubwerera wekha.

16Iwe unamwa pa phiri langa loyera,

koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;

iwo adzamwa ndi kudzandira

ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.

17Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;

phirilo lidzakhala lopatulika,

ndipo nyumba ya Yakobo

idzalandira cholowa chake.

18Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto

ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;

nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,

ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.

Sipadzakhala anthu opulumuka

kuchokera mʼnyumba ya Esau.”

Yehova wayankhula.

19Anthu ochokera ku Negevi adzakhala

ku mapiri a Esau,

ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri

adzatenga dziko la Afilisti.

Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,

ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.

20Aisraeli amene ali ku ukapolo

adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;

a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi

adzalandira mizinda ya ku Negevi.

21Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni

ndipo adzalamulira mapiri a Esau.

Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.