以赛亚书 42 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 42:1-25

主的仆人

1“看啊,我所扶持、所拣选、所喜悦的仆人,

我已将我的灵赐给祂,

祂必将正义带给万邦。

2祂不喧嚷,不呼喊,

不在街上高声说话。

3压伤的芦苇,祂不折断;

将残的灯火,祂不吹灭。

祂必信实地带来正义。

4祂不灰心也不沮丧,

直到祂在地上设立正义。

四海都渴望祂的训诲。”

5创造诸天、铺展穹苍、

设立大地和地上的一切、

赐给世人生命气息和灵性的耶和华上帝说:

6“我耶和华凭公义呼召你,

我必扶持你,保护你,

使你做我与众民立约的中保、

成为列国的光,

7使你开瞎子的眼睛、

从监牢中释放囚犯、

领出陷在黑暗中的人。

8我是耶和华,这就是我的名字。

我不会把我的荣耀给假神,

也不会把我当受的赞美给雕刻的偶像。

9看啊,以前的预言都已应验,

我现在要宣告新的预言,

把还未发生的事告诉你们。”

赞美主的歌

10航海的和海中的一切、

众海岛和岛上的居民啊,

你们要向耶和华高唱新歌,

从地极赞美祂。

11旷野和其中的城邑以及基达人居住的村庄,

要一同扬声颂赞。

西拉的居民要歌唱,

在山顶欢呼。

12愿他们把荣耀归给耶和华,

在众海岛上颂赞祂。

13耶和华像出征的勇士,

像斗志激昂的战士。

祂必高呼吶喊,战胜仇敌。

上帝应许帮助以色列人

14“我已沉默多时,我克制不语,

现在我要发出急促的呐喊,

像分娩的妇人。

15我要使大山小丘一片荒凉,

上面的草木都枯萎。

我要使河川变成岛屿,

池塘干涸。

16我要带领瞎子走他们不认识的路,

引导他们走陌生的道。

我要把他们面前的黑暗变为光明,

坎坷之地变得平坦。

我必行这些事,我必不离弃他们。

17但那些信靠雕刻的偶像、

供奉金属铸像的必遭唾弃,

羞愧难当。

以色列眼瞎耳聋

18“耳聋的人啊,听吧!

眼瞎的人啊,看吧!

19有谁比我的仆人更瞎,

比我差遣的使者更聋呢?

有谁像那些与我立约的人那样瞎呢?

有谁像耶和华的仆人那样瞎呢?

20你们看见许多事却不领会,

耳朵开着却听不见。”

21耶和华乐意使祂的律法尊大而荣耀,

因为祂行事公义。

22但这些百姓饱受劫掠,

都被困在坑中,囚在监内。

他们沦为俘虏,无人搭救;

被当作战利品掳走,无人追回。

23你们当中谁肯专心听呢?

以后谁肯留心倾听呢?

24谁把雅各交给了掳掠者,

使以色列任人劫掠?

难道不是被我们得罪的耶和华吗?

他们不肯遵行祂的道,

也不听从祂的训诲。

25所以,祂把烈怒和战火倾倒在他们身上。

他们被火包围,却不明白;

被烈火焚身,却不在乎。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 42:1-25

Mtumiki wa Yehova

1“Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza,

amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye.

Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo,

ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.

2Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu,

kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.

3Bango lophwanyika sadzalithyola,

ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa.

Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;

4sadzafowoka kapena kukhumudwa

mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi,

ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”

5Yehova Mulungu

amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika,

amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka,

amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo,

ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,

6“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama;

ndikugwira dzanja ndipo

ndidzakuteteza.

Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu

ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.

7Udzatsekula maso a anthu osaona,

udzamasula anthu a mʼndende

ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.

8“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo!

Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense

kapena matamando anga kwa mafano.

9Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi,

ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano;

zinthuzo zisanaonekere

Ine ndakudziwitsani.”

Nyimbo Yotamanda Yehova

10Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi,

inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo.

Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.

11Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo;

midzi ya Akedara ikondwere.

Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe;

afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.

12Atamande Yehova

ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.

13Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu,

adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo;

akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo

ndipo adzagonjetsa adani ake.

14Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali,

ndakhala ndili phee osachita kanthu.

Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira,

ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.

15Ndidzawononga mapiri ndi zitunda

ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse;

ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba

ndipo ndidzawumitsa maiwe.

16Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe,

ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo;

ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala

ndipo ndidzasalaza malo osalala.

Zimenezi ndizo ndidzachite;

sindidzawataya.

17Koma onse amene amadalira mafano

amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’

ndidzawachititsa manyazi kotheratu.

Aisraeli Alephera Kuphunzira

18“Imvani, agonthi inu;

yangʼanani osaona inu, kuti muone! 19Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi?

Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma?

Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano,

kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?

20Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale;

makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”

21Chinamukomera Yehova

chifukwa cha chilungamo chake,

kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.

22Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo,

onsewa anawakola mʼmaenje

kapena akuwabisa mʼndende.

Tsono asanduka chofunkha

popanda wina wowapulumutsa

kapena kunena kuti,

“Abwezeni kwawo.”

23Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi

kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?

24Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha,

ndi Israeli kwa anthu akuba?

Kodi si Yehova,

amene ife tamuchimwirayu?

Pakuti sanathe kutsatira njira zake;

ndipo sanamvere malangizo ake.

25Motero anawakwiyira kwambiri,

nawavutitsa ndi nkhondo.

Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse;

motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.