雅歌 1 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

雅歌 1:1-17

1这是所罗门的歌,是歌中最美妙的歌。

女子:

2深深地吻我吧!

因为你的爱情比美酒更香甜。

3你的美名如此芬芳,

如同倒出来的香膏,

难怪少女们都爱慕你。

4你带我走,让我们一起奔跑吧!

王啊,把我带进你的寝宫吧!

耶路撒冷的少女:

我们为你欢喜快乐,

我们要颂扬你那胜似美酒的爱情。

女子:

难怪少女们都爱慕你!

5耶路撒冷的少女啊!

我虽然黑似基达的帐篷,

却美如所罗门的锦帐。

6不要因为我被太阳晒黑就看不起我。

这是因为我的兄弟恼恨我,

要我在烈日之下看守葡萄园,

使我无暇照顾自己1:6 我无暇照顾自己”希伯来文是“我却无法照料自己的葡萄园。”

7我心爱的人啊,告诉我吧,

你在哪里牧羊?

中午带羊去哪里歇息?

我何必在你同伴的羊群旁流浪,

像风尘女子一样呢?

耶路撒冷的少女:

8绝色佳人啊!

要是你不知道,

就跟着羊群的足迹,

到牧人的帐篷边喂养你的山羊羔吧。

男子:

9我的爱人啊,

你好比法老战车上套的牝马,

引人注目。

10耳环辉映你的脸颊,

珠链轻衬你的颈项。

11我们要为你打造镶有银珠的金饰。

女子:

12王坐席的时候,

我身上的哪哒香膏芬芳四溢。

13我的良人靠在我怀中,

如同一袋没药。

14我的良人在我眼中,

好像隐·基底葡萄园中的凤仙花。

男子:

15我的爱人啊!

你真是美极了!美极了!

你的眼神纯情专一,好像鸽子的眼睛。

女子:

16我的良人啊!

你真英俊!真可爱!

我们以青草作床榻,

17以香柏树作屋梁,

以松树作椽子。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 1:1-17

1Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.

Mkazi

2Undipsompsone ndi milomo yako

chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.

3Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;

dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.

Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!

4Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!

Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.

Abwenzi

Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,

tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.

Mkazi

Amachita bwinotu potamanda iwe!

5Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,

inu akazi a ku Yerusalemu,

ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,

ngati makatani a tenti ya Solomoni.

6Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,

ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.

Alongo anga anandikwiyira

ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;

munda wangawanga sindinawusamalire.

7Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako

ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.

Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere

pambali pa ziweto za abwenzi ako?

Abwenzi

8Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,

ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa

ndipo udyetse ana ambuzi

pambali pa matenti a abusa.

Mwamuna

9Iwe bwenzi langa,

uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.

10Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,

khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.

11Tidzakupangira ndolo zagolide

zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.

Mkazi

12Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,

mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.

13Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,

kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.

14Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,

ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.

Mwamuna

15Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!

Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,

maso ako ali ngati nkhunda.

Mkazi

16Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!

Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!

Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.

Mwamuna

17Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,

phaso lake ndi la mtengo wa payini.