耶利米书 1 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 1:1-19

1希勒迦的儿子耶利米便雅悯境内亚拿突城的一位祭司,以下是他的话。 2犹大亚们的儿子约西亚执政第十三年,耶和华的话传给了耶利米3犹大约西亚的儿子约雅敬开始执政,一直到约西亚的另一个儿子西底迦犹大王的第十一年五月,就是耶路撒冷的居民被掳之日,耶和华的话常常传给耶利米

耶利米蒙召

4耶和华对我说:

5“我还没有使你在母腹中成形,就认识你;

你还未出生,我已使你圣洁,

立你做万国的先知。”

6我回答说:“主耶和华啊,我太年轻,不懂得怎样说话。” 7耶和华却说:

“不要说你太年轻,

我派你去谁那里,

你就去谁那里;

我吩咐你说什么,

你就说什么。

8谁也不要怕,

因为我与你同在,

我必拯救你。

这是耶和华说的。”

9然后,耶和华伸手摸我的口,对我说:“看啊,我已把我的话放在你口中。 10今日,我派你到列邦列国去拔掉、拆除、毁灭、推翻、建造和栽植。”

两个异象

11耶和华又对我说:“耶利米,你看见什么?”我说:“我看见一根杏树枝。” 12耶和华说:“不错。我必实现我说过的话。”

13耶和华又对我说:“你看见什么?”我回答说:“我看见一锅煮沸的水,从北方倾倒下来。” 14耶和华说:“不错。因为有灾祸要从北方降临到这地方的一切居民。 15我要召来北方各国,他们要在耶路撒冷的城门自立王位,攻打耶路撒冷周围的城墙和犹大各城邑。这是耶和华说的。 16我要审判他们,因为他们犯罪作恶,背弃我,给别的神明烧香,又跪拜自己制造的神像。 17现在,你要做好准备,去把我吩咐你的话告诉他们。不要惧怕他们,不然我将使你在他们面前充满恐惧。 18看啊,今天我已使你成为坚城、铁柱、铜墙,来对抗整个犹大,对抗犹大的君王、首领、祭司和境内的众民。 19他们必攻击你,但绝不能胜过你,因为我与你同在,我必拯救你。这是耶和华说的。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 1:1-19

1Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini. 2Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda. 3Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.

Kuyitanidwa kwa Yeremiya

4Yehova anayankhula nane kuti,

5“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale,

iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale;

ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”

6Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”

7Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira. 8Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

9Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako. 10Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”

11Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”

12Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”

13Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”

14Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto. 15Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova.

“Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu

polowera pa zipata za Yerusalemu;

iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake

ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.

16Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo

chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine.

Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina,

ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.

17“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona. 18Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo. 19Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.