以赛亚书 27 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 27:1-13

以色列必蒙拯救

1到那日,耶和华必用祂无坚不摧的利剑惩罚巨龙——那飞快、曲行的蛇。祂必杀死那海中的怪物。

2到那日,耶和华说:

“你们要歌颂那佳美的葡萄园。

3我耶和华是看守它的,

我勤加浇灌,

昼夜守护,

不让人毁坏。

4我不再向它发怒。

若是发现荆棘和蒺藜,

我就对付它们,

把它们烧光。

5除非它们寻求我的庇护,

与我和好,

与我和好。”

6有一天,雅各必扎根生长,

以色列必发芽开花,

果实遍地。

7耶和华不像击打以色列的敌人那样击打以色列人。

祂不像击杀以色列的敌人那样击杀以色列人。

8祂与以色列人为敌,

使他们被掳,

驱逐他们离开本地,

用从东方刮来的暴风吹散他们。

9借此,雅各家的罪恶必得到赦免,

他们罪恶被除掉后所结的果实是:

打碎假神祭坛的石头,

推倒亚舍拉神像和香坛。

10坚城荒凉,被人遗弃,

如同旷野。

牛犊在那里吃草、躺卧,

吃光树枝上的叶子。

11树枝枯干断落,

妇女拿去作柴烧。

因为以色列人愚昧无知,

所以他们的创造主不怜悯他们,

也不向他们施恩。

12到那日,耶和华必把以色列人从幼发拉底河到埃及小河一个一个地召集起来,像人打树拾果子一样。 13到那日,号角吹响后,亚述地将要灭亡的以色列人和流散到埃及以色列人,都必来到耶路撒冷的圣山敬拜耶和华。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 27:1-13

Za Munda Wamphesa wa Yehova

1Tsiku limenelo,

Yehova ndi lupanga lake

lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu,

adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija,

Leviyatani chinjoka chodzikulunga;

adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.

2Tsiku limenelo Yehova adzati,

“Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:

3Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira;

ndimawuthirira nthawi zonse.

Ndimawulondera usana ndi usiku

kuti wina angawononge.

4Ine sindinakwiye.

Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo!

Ndikachita nazo nkhondo;

ndikanazitentha zonse ndi moto.

5Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze;

apangane nane za mtendere,

ndithu, apangane nane za mtendere.”

6Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu,

Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa,

ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.

7Kodi Yehova anakantha Israeli

ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli?

Kapena kodi Yehova anapha Israeli

ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?

8Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo,

mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa,

monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.

9Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo.

Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja,

ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza

mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha.

Sipadzapezekanso mafano a Asera

kapena maguwa ofukiza lubani.

10Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja,

wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu;

kumeneko amadyetselako ana angʼombe

kumeneko zimapumulako ziweto

ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.

11Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka

ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni.

Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru;

kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni,

ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.

12Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto. 13Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.