Псалми 82 – NSP & CCL

New Serbian Translation

Псалми 82:1-8

Псалам 82

Псалам Асафов.

1Бог је стао у Божијем збору,

па сад суди међу боговима:

2„Докле ћете судити нечасно

и држати страну злотворима? Села

3Заступајте право убогога и сиротога,

оправдајте сиромаха и невољника.

4Спасавајте слабог и тлаченог,

избавите их из руке зликоваца.

5Али нису знали, нису разумели;

у тами су посртали

и темеље земљи задрмали.

6Ја рекох: ’Богови сте,

сви сте деца Свевишњега!’

7Ипак ћете помрети ко људи,

пропашћете ко и главар сваки.“

8Устани, Боже, и суди земљи,

јер сви су народи наследство твоје!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 82:1-8

Salimo 82

Salimo la Asafu.

1Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;

Iye akuweruza pakati pa “milungu.”

2“Mudzateteza osalungama mpaka liti,

ndi kukondera anthu oyipa?

3Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;

mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.

4Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;

apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.

5“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.

Amayendayenda mu mdima;

maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,

nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’

7Koma mudzafa ngati anthu wamba;

mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”

8Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,

pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.