Zaburi 89 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 89:1-52

Zaburi 89

Wimbo Wakati Wa Taabu Ya Kitaifa

Utenzi wa Ethani Mwezrahi.

189:1 Za 59:16; 36:5; 40:10Nitaimba juu ya upendo mkuu wa Bwana milele;

kwa kinywa changu nitajulisha uaminifu wako

ujulikane kwa vizazi vyote.

289:2 Za 36:5Nitatangaza kuwa upendo wako unasimama imara milele

na uaminifu wako umeuthibitisha mbinguni.

389:3 Eze 34:23; Hes 3:5; Ebr 7:21; Mdo 2:30Ulisema, “Nimefanya agano na mteule wangu,

nimemwapia mtumishi wangu Daudi,

489:4 2Sam 7:12-16; Lk 1:32, 33; Mt 1:1; Isa 9:6, 7; Rum 1:3; 1Fal 9:5; 8:16; Eze 37:24, 25; Za 132:11, 12‘Nitaimarisha uzao wako milele

na kudumisha ufalme wako kwa vizazi vyote.’ ”

589:5 Za 19:1; 1:5Ee Bwana, mbingu zinayasifu maajabu yako,

uaminifu wako pia katika kusanyiko la watakatifu.

689:6 Mwa 1:26; Kut 9:14; Za 18:31; 113:5Kwa kuwa ni nani katika mbingu

anayeweza kulinganishwa na Bwana?

Ni nani miongoni mwa viumbe vya mbinguni

aliye kama Bwana?

789:7 Ay 5:1; Za 11:1; 47:2Katika kusanyiko la watakatifu, Mungu huogopwa sana,

anahofiwa kuliko wote wanaomzunguka.

889:8 Isa 6:3; Za 71:19Ee Bwana Mwenye Nguvu Zote,

ni nani aliye kama wewe?

Ee Bwana, wewe ni mwenye nguvu,

na uaminifu wako unakuzunguka.

989:9 Za 65:7; Ay 38:11; Nah 1:4; Mt 8:26Wewe unatawala bahari yenye msukosuko;

wakati mawimbi yake yanapoinuka, wewe unayatuliza.

1089:10 Ay 9:13; Za 59:11; 68:1; 92:9; Isa 30:9Wewe ulimponda Rahabu89:10 Rahabu hapa ina maana jina la Misri kwa fumbo, yaani mwenye majivuno (lakini sio Rahabu wa Yos 2).

kama mmojawapo wa waliochinjwa;

kwa mkono wako wenye nguvu,

uliwatawanya adui zako.

1189:11 Kum 10:14; Za 24:1; 115:6; 1Nya 29:11; Mwa 1:1Mbingu ni zako, nayo nchi pia ni yako,

uliuwekea ulimwengu msingi

pamoja na vyote vilivyomo.

1289:12 Yos 19:22; Kum 3:8; 4:48; Za 98:8; Yos 12:1; Amu 4:6Uliumba kaskazini na kusini;

Tabori na Hermoni wanaliimbia jina lako kwa furaha.

1389:13 Yos 4:24Mkono wako umejaa uwezo;

mkono wako una nguvu,

mkono wako wa kuume umetukuzwa.

1489:14 Za 97:2; 85:10, 11Haki na hukumu ndio msingi wa kiti chako cha enzi;

upendo na uaminifu vinakutangulia.

1589:15 Za 1:1; 44:3; Hes 10:10Heri ni wale ambao wamejifunza kukusifu kwa shangwe,

wanaotembea katika mwanga

wa uwepo wako, Ee Bwana.

1689:16 Za 30:4; 105:3Wanashangilia katika jina lako mchana kutwa,

wanafurahi katika haki yako.

1789:17 Za 18:1, 24; 75:10; 92:10; 112:9; 148:14Kwa kuwa wewe ni utukufu na nguvu yao,

kwa wema wako unatukuza pembe89:17 Pembe inawakilisha nguvu. yetu.

1889:18 Hos 13:10; Za 18:2; 47:9; Isa 16:5; 33:17, 22Naam, ngao yetu ni mali ya Bwana,

na mfalme wetu mali ya Aliye Mtakatifu wa Israeli.

19Ulizungumza wakati fulani katika maono,

kwa watu wako waaminifu, ukasema:

“Nimeweka nguvu kwa shujaa,

nimemwinua kijana miongoni mwa watu.

2089:20 Mdo 13:22; Za 78:70; Kut 29:7; 1Fal 1:39; 1Sam 2:35; 2Sam 22:51Nimemwona Daudi, mtumishi wangu,

na nimemtia mafuta yangu matakatifu.

2189:21 Za 89:13; 18:35Kitanga changu kitamtegemeza,

hakika mkono wangu utamtia nguvu.

2289:22 Amu 3:15; 2Sam 7:10Hakuna adui atakayemtoza ushuru,

hakuna mtu mwovu atakayemwonea.

2389:23 Za 18:40; 2Sam 7:9Nitawaponda adui zake mbele zake

na kuwaangamiza watesi wake.

2489:24 2Sam 7:15; Za 61:7Upendo wangu mkamilifu utakuwa pamoja naye,

kwa Jina langu pembe yake itatukuzwa.

2589:25 Za 72:8Nitauweka mkono wake juu ya bahari,

mkono wake wa kuume juu ya mito.

2689:26 Za 62:2; Yer 3:4; 2Sam 7:14; 22:47; 1Nya 22:10; Yn 5:17; Ebr 1:5Naye ataniita kwa sauti, ‘Wewe ni Baba yangu,

Mungu wangu, Mwamba na Mwokozi wangu.’

2789:27 Kol 1:18; Hes 24:7; Za 2:6, 7; Ufu 1:5; 19:16Nitamteua pia awe mzaliwa wangu wa kwanza,

aliyetukuka kuliko wafalme wote wa dunia.

2889:28 Za 89:33-34; Isa 55:3Nitadumisha upendo wangu kwake milele,

na agano langu naye litakuwa imara.

2989:29 Isa 9:7; Yer 33:17; Dan 7:14; Kum 11:21; Za 89:4, 36Nitaudumisha uzao wake milele,

kiti chake cha enzi kama mbingu zinavyodumu.

3089:30 2Sam 7:14; Yer 9:13“Kama wanae wataacha amri yangu

na wasifuate sheria zangu,

31kama wakihalifu maagizo yangu

na kutoshika amri zangu,

3289:32 2Sam 7:14nitaadhibu dhambi yao kwa fimbo,

uovu wao kwa kuwapiga,

3389:33 2Sam 7:15lakini sitauondoa upendo wangu kwake,

wala sitausaliti uaminifu wangu kamwe.

3489:34 Hes 23:19Mimi sitavunja agano langu

wala sitabadili lile ambalo midomo yangu imelitamka.

3589:35 Za 110:4; Ebr 6:13, 17; Amo 4:2; 8:7Mara moja na kwa milele, nimeapa kwa utakatifu wangu,

nami sitamdanganya Daudi:

3689:36 Za 89:4; 2Sam 7:18; Lk 1:33; Yn 12:34kwamba uzao wake utaendelea milele,

na kiti chake cha enzi kitadumu mbele zangu kama jua;

3789:37 Yer 31:35; 33:20, 21kitaimarishwa milele kama mwezi,

shahidi mwaminifu angani.”

3889:38 1Nya 28:9; Isa 22:5; Mao 2:2Lakini wewe umemkataa, umemdharau,

umemkasirikia sana mpakwa mafuta wako.

3989:39 Mao 5:16Umelikana agano lako na mtumishi wako,

na umeinajisi taji yake mavumbini.

4089:40 Za 80:12; Isa 22:5; Mao 2:2Umebomoa kuta zake zote,

na ngome zake zote umezifanya kuwa magofu.

4189:41 Amu 2:14; Za 44:13Wote wapitao karibu wamemnyangʼanya mali zake;

amekuwa dharau kwa jirani zake.

4289:42 Za 13:2; 80:6Umeutukuza mkono wa kuume wa adui zake,

umewafanya watesi wake wote washangilie.

4389:43 Za 44:10Umegeuza makali ya upanga wake,

na hukumpa msaada katika vita.

44Umeikomesha fahari yake,

na kukiangusha kiti chake cha enzi.

4589:45 Za 39:5; 44:15; 109:29Umezifupisha siku za ujana wake,

umemfunika kwa vazi la aibu.

4689:46 Za 79:5Hata lini, Ee Bwana? Utajificha milele?

Ghadhabu yako itawaka kama moto hata lini?

4789:47 Mwa 47:9; Ay 7:7; Za 39:5; 1Pet 1:24Kumbuka jinsi maisha yangu yanavyopita haraka.

Ni kwa ubatili kiasi gani umemuumba mwanadamu!

4889:48 Mwa 5:24; Za 22:29; Ebr 11:5Ni mtu gani awezaye kuishi na asione kifo,

au kujiokoa mwenyewe kutoka nguvu za kaburi?89:48 Kaburi hapa maana yake ni Kuzimu, kwa Kiebrania ni Sheol.

4989:49 2Sam 7:12; Isa 55:13Ee Bwana, uko wapi upendo wako mkuu wa mwanzoni,

ambao katika uaminifu wako ulimwapia Daudi?

5089:50 Za 69:19Bwana kumbuka jinsi mtumishi wako amesimangwa,

jinsi ninavyovumilia moyoni mwangu dhihaka za mataifa yote,

5189:51 Za 74:10dhihaka ambazo kwazo adui zako

wamenisimanga, Ee Bwana,

ambazo kwazo wamesimanga

kila hatua ya mpakwa mafuta wako.

5289:52 Za 41:13; 72:19Msifuni Bwana milele!

Amen na Amen.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 89:1-52

Salimo 89

Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara.

1Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya;

ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.

2Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya,

kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.

3Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga,

ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,

4‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya.

Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’ ”

Sela.

5Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,

kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.

6Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?

Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?

7Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;

Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.

8Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?

Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.

9Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;

pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.

10Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;

ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.

11Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;

munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.

12Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;

Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.

13Mkono wanu ndi wamphamvu;

dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.

14Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;

chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.

15Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,

amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.

16Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;

amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.

17Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo

ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.

18Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,

Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.

19Kale munayankhula mʼmasomphenya,

kwa anthu anu okhulupirika munati,

“Ndapatsa mphamvu wankhondo;

ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.

20Ndamupeza mtumiki wanga Davide;

ndamudzoza ndi mafuta opatulika.

21Dzanja langa lidzamuchirikiza;

zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.

22Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;

anthu oyipa sadzamusautsa.

23Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake

ndi kukantha otsutsana naye.

24Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,

ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.

25Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,

dzanja lake lamanja pa mitsinje.

26Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,

Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’

27Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;

wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.

28Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,

ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.

29Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,

mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.

30“Ngati ana ake adzataya lamulo langa

ndi kusatsatira malangizo anga,

31ngati adzaswa malamulo anga

ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,

32Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,

mphulupulu zawo powakwapula.

33Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,

kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.

34Sindidzaswa pangano langa

kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.

35Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga

ndipo sindidzanama kwa Davide,

36kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya

ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;

37udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,

mboni yokhulupirika mʼmitambo.

Sela

38“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya,

mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.

39Mwakana pangano ndi mtumiki wanu

ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.

40Inu mwagumula makoma ake onse

ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.

41Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake;

iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.

42Mwakweza dzanja lamanja la adani ake;

mwachititsa kuti adani ake akondwere.

43Mwabunthitsa lupanga lake,

simunamuthandize pa nkhondo.

44Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake

ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.

45Mwachepetsa masiku a unyamata wake;

mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi.

Sela

46“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale?

Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?

47Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa

pakuti munalenga kwachabe anthu onse!

48Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa?

Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda?

Sela

49Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija,

chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?

50Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera,

momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,

51mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova,

ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.

52“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”

Ameni ndi Ameni.