Zaburi 90 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 90:1-17

KITABU CHA NNE

(Zaburi 90–106)

Zaburi 90

Umilele Wa Mungu Na Udhaifu Wa Mwanadamu

Maombi ya Mose, mtu wa Mungu.

190:1 Kum 33:27; Efe 2:22; Ufu 21:3Bwana, wewe umekuwa makao yetu

katika vizazi vyote.

290:2 Ay 38:4, 5; 10:5; 15:7; Mwa 21:33; Isa 9:6; 57:15; Za 102:24-27; Mit 8:23-26Kabla ya kuzaliwa milima

au hujaumba dunia na ulimwengu,

wewe ni Mungu tangu milele hata milele.

390:3 Mwa 2:7; 3:9; Ay 7:21; 34:15; 1Kor 15:47; Mhu 12:7Huwarudisha watu mavumbini,

ukisema, “Rudini mavumbini, enyi wanadamu.”

490:4 Ebr 13:8; 2Pet 3:8; Ay 10:5Kwa maana kwako miaka elfu

ni kama siku moja iliyokwisha pita,

au kama kesha la usiku.

590:5 Mwa 19:15; Isa 40:6Unawatowesha wanadamu katika usingizi wa kifo,

nao ni kama majani machanga ya asubuhi:

690:6 Isa 40:6-8; Ay 14:2; Za 92:7ingawa asubuhi yanachipua,

ifikapo jioni huwa yamenyauka na kukauka.

7Tumeangamizwa kwa hasira yako

na tumetishwa kwa ghadhabu yako.

890:8 2Kor 4:2; Efe 5:12; Ebr 4:13; 4:12, 13; Za 19:12; 50:21; Yer 16:17; Mit 5:21; Mhu 12:14; Rum 2:16; 1Kor 4:5Umeyaweka maovu yetu mbele yako,

dhambi zetu za siri katika nuru ya uwepo wako.

990:9 Za 78:33Tumeishi siku zetu zote chini ya ghadhabu yako,

tunamaliza miaka yetu kwa kuomboleza.

1090:10 Isa 23:15, 17; 2Sam 19:35; Ay 5:7; 20:8; 34:15; Yer 25:11Siku zetu za kuishi ni miaka sabini,

au miaka themanini ikiwa tuna nguvu,

lakini yote ni ya shida na taabu,

nazo zapita haraka, nasi twatoweka.

1190:11 Za 7:11; 76:7Ni nani ajuaye nguvu za hasira yako?

Kwa maana ghadhabu yako ni kubwa

kama hofu tunayopaswa kuwa nayo kwako.

1290:12 Za 39:4; 139:16; Mit 16:9; 20:24; Kum 32:29Tufundishe kuzihesabu siku zetu vizuri,

ili tujipatie moyo wa hekima.

1390:13 Za 6:3; Kum 32:36Ee Bwana, uwe na huruma! Utakawia hata lini?

Wahurumie watumishi wako.

1490:14 Za 103:5; 107:9; 145:16, 19; 31:7; 77:8; 143:8Tushibishe asubuhi kwa upendo wako usiokoma,

ili tuweze kuimba kwa shangwe na kufurahi siku zetu zote.

15Utufurahishe kulingana na siku ulizotuadhibu,

kulingana na miaka tuliyotaabika.

1690:16 Za 44:1; Hab 3:2Matendo yako na yaonekane kwa watumishi wako,

utukufu wako kwa watoto wao.

1790:17 Isa 26:12; 2The 2:16, 17Wema wa Bwana Mungu wetu uwe juu yetu;

uzithibitishe kazi za mikono yetu:

naam, uzithibitishe kazi za mikono yetu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 90:1-17

BUKU LACHINAYI

Masalimo 90–106

Salimo 90

Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.

1Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo

pa mibado yonse.

2Mapiri asanabadwe,

musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse,

kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.

3Inu mumabwezera anthu ku fumbi,

mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”

4Pakuti zaka 1,000 pamaso panu

zili ngati tsiku limene lapita

kapena ngati kamphindi ka usiku.

5Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa,

iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,

6ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano,

pofika madzulo wauma ndi kufota.

7Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu;

ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.

8Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu,

machimo athu obisika poonekera pamaso panu.

9Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu;

timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.

10Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70,

kapena 80 ngati tili ndi mphamvu;

komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa,

zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.

11Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu?

Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.

12Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola,

kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

13Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?

Achitireni chifundo atumiki anu.

14Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha,

kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.

15Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa,

kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.

16Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu,

kukongola kwanu kwa ana awo.

17Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife;

tikhazikitsireni ntchito ya manja athu;

inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.