Zaburi 135 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 135:1-21

Zaburi 135

Wimbo Wa Sifa Kwa Mungu

1135:1 Neh 7:73Msifuni Bwana.

Lisifuni jina la Bwana,

msifuni, enyi watumishi wa Bwana,

2135:2 1Nya 15:2; Lk 2:37; Za 116:19ninyi ambao mnatumika ndani ya nyumba ya Bwana,

katika nyua za nyumba ya Mungu wetu.

3135:3 1Nya 16:34; Za 119:68; 68:4; 92:1; 147:1Msifuni Bwana, kwa kuwa Bwana ni mwema,

liimbieni sifa jina lake, kwa maana hilo lapendeza.

4135:4 Kut 19:5; Kum 7:6, 7; 10:15; Mal 3:17; Tit 2:14Kwa maana Bwana amemchagua Yakobo kuwa wake mwenyewe,

Israeli kuwa mali yake ya thamani.

5135:5 Za 48:1; 145:3; Kut 12:12; 1Nya 16:25; Ay 21:22Ninajua ya kuwa Bwana ni mkuu,

kwamba Bwana wetu ni mkuu kuliko miungu yote.

6135:6 Za 115:3; Dan 4:35; Mt 6:10Bwana hufanya lolote apendalo,

mbinguni na duniani,

katika bahari na vilindi vyake vyote.

7135:7 Ay 5:10; Za 68:6; Isa 30:23; Amo 4:13; Yer 10:13; 51:16; Yoe 2:23; Zek 10:1; Kum 28:12; Mwa 2:6; Ay 28:25; 38:22Hufanya mawingu kupanda kutoka miisho ya dunia;

hupeleka umeme wa radi pamoja na mvua

na huleta upepo kutoka ghala zake.

8135:8 Kut 4:23; 12:12Alimuua mzaliwa wa kwanza wa Misri,

mzaliwa wa kwanza wa wanadamu na wanyama.

9135:9 Kut 7:9; Za 136:10-15Alipeleka ishara zake na maajabu katikati yako, ee Misri,

dhidi ya Farao na watumishi wake wote.

10135:10 Hes 21:21-25; Yos 24:8-11; Za 44:2; 78:55; 136:17-21Aliyapiga mataifa mengi,

na akaua wafalme wenye nguvu:

11135:11 Hes 21:21, 26, 33; Yos 12:7-24Mfalme Sihoni na Waamori,

Ogu mfalme wa Bashani

na wafalme wote wa Kanaani:

12135:12 Kum 29:8akatoa nchi yao kuwa urithi,

urithi kwa watu wake Israeli.

13135:13 Kut 3:15; Za 102:12Ee Bwana, jina lako ladumu milele,

kumbukumbu za fahari zako, Ee Bwana, kwa vizazi vyote.

14135:14 1Sam 24:15; Ebr 10:30; Kum 32:36Maana Bwana atawathibitisha watu wake,

na kuwahurumia watumishi wake.

15135:15 Ufu 9:20; Isa 2:8; 31:7; 37:19; 40:19; Yer 1:16; 10:5; Za 96:5Sanamu za mataifa ni fedha na dhahabu,

zilizotengenezwa kwa mikono ya wanadamu.

16135:16 1Fal 18:26Zina vinywa, lakini haziwezi kusema,

zina macho, lakini haziwezi kuona;

17135:17 Yer 10:14; Hab 2:19zina masikio, lakini haziwezi kusikia,

wala hakuna pumzi katika vinywa vyao.

18Wale wanaozitengeneza watafanana nazo,

vivyo hivyo wale wote wanaozitumainia.

19135:19 Za 22:23Ee nyumba ya Israeli, msifuni Bwana;

ee nyumba ya Aroni, msifuni Bwana;

20ee nyumba ya Lawi, msifuni Bwana;

ninyi mnaomcha, msifuni Bwana.

21135:21 Za 128:5; 134:3; 1Fal 8:13; 2Nya 6:2Msifuni Bwana kutoka Sayuni,

msifuni yeye aishiye Yerusalemu.

Msifuni Bwana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 135:1-21

Salimo 135

1Tamandani Yehova.

Tamandani dzina la Yehova;

mutamandeni, inu atumiki a Yehova,

2amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova,

mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

3Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino;

imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,

4Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake,

Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.

5Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu,

kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.

6Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera,

kumwamba ndi dziko lapansi,

ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.

7Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi,

amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula

ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.

8Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,

ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.

9Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto,

kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.

10Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu

ndi kupha mafumu amphamvu:

11Sihoni mfumu ya Aamori,

Ogi mfumu ya Basani,

ndi maufumu onse a ku Kanaani;

12ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa,

cholowa cha anthu ake Aisraeli.

13Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya,

mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.

14Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa,

ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.

15Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide,

opangidwa ndi manja a anthu.

16Pakamwa ali napo koma sayankhula

maso ali nawo, koma sapenya;

17makutu ali nawo, koma sakumva

ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.

18Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo,

chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.

19Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova;

inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;

20Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova;

Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.

21Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni,

amene amakhala mu Yerusalemu.

Tamandani Yehova.