Nahumu 1 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Nahumu 1:1-15

11:1 Isa 13:1; 19:1; Yer 23:33-34; 50:18; Mwa 10:11; Nah 2:8; 3:7Neno alilosema Mungu kuhusu Ninawi. Kitabu cha maono cha Nahumu, Mwelkoshi.

Hasira Ya Mungu Dhidi Ya Ninawi

21:2 Kut 20:5; Mwa 4:24; Kum 32:41; 7:10; Za 94:1Bwana ni mwenye wivu na Mungu mlipiza kisasi;

Bwana hulipiza kisasi na amejaa ghadhabu.

Bwana hulipiza kisasi juu ya watesi wake,

naye anadumisha ghadhabu yake dhidi ya adui zake.

31:3 Neh 9:17; Kut 34:7; 19:16; Za 103:8; Mik 7:18; 2Sam 22:10; Za 50:3; 104:3Bwana si mwepesi wa hasira naye ni mwenye nguvu,

Bwana hataacha kuadhibu wenye hatia.

Njia yake ipo katika kisulisuli na tufani,

na mawingu ni vumbi la miguu yake.

41:4 2Sam 22:16; Kut 14:22; Isa 33:9; Yos 3:15, 16Anakemea bahari na kuikausha,

anafanya mito yote kukauka.

Bashani na Karmeli zinanyauka

na maua ya Lebanoni hukauka.

51:5 Kut 19:18; Ay 9:6; 2Sam 22:8; Yoe 2:10; Eze 38:20; Mik 1:4Milima hutikisika mbele yake

na vilima huyeyuka.

Nchi hutetemeka mbele yake,

dunia na wote waishio ndani yake.

61:6 Za 130:3; Eze 22:14; Isa 5:24-25; 42:25; Yer 10:10; 1Fal 19:11Ni nani awezaye kuzuia hasira yake yenye uchungu?

Nani awezaye kuvumilia hasira yake kali?

Ghadhabu yake imemiminwa kama moto,

na miamba inapasuka mbele zake.

71:7 Yer 33:11; 17:17; Za 22:9; 1:6; 2Tim 2:19Bwana ni Mwema,

kimbilio wakati wa taabu.

Huwatunza wale wanaomtegemea,

81:8 Isa 8:7; Amo 8:8; Dan 9:26lakini kwa mafuriko makubwa,

ataangamiza Ninawi;

atafuatilia adui zake hadi gizani.

91:9 Hos 7:15Shauri baya lolote wapangalo dhidi ya Bwana

yeye atalikomesha;

taabu haitatokea mara ya pili.

101:10 2Sam 23:6; Isa 49:26; 5:24; Mal 4:1Watasongwa katikati ya miiba

na kulewa kwa mvinyo wao.

Watateketezwa kama mabua makavu.

11Ee Ninawi, kutoka kwako amejitokeza mmoja,

ambaye anapanga shauri baya

dhidi ya Bwana

na kushauri uovu.

121:12 Isa 10:34; 54:6-8; Mao 3:31-32Hili ndilo asemalo Bwana:

“Ingawa wana muungano nao ni wengi sana,

watakatiliwa mbali na kuangamia.

Ingawa nimekutesa wewe, ee Yuda,

sitakutesa tena.

131:13 Isa 9:4; Ay 12:18; Za 107:14Sasa nitavunja nira zao kutoka shingo yako,

nami nitazivunjilia mbali pingu zako.”

141:14 Isa 14:22; Mik 5:13; Yer 28:8; Eze 32:22-23Hii ndiyo amri Bwana aliyoitoa kukuhusu wewe, Ninawi:

“Hutakuwa na wazao

watakaoendeleza jina lako.

Nitaharibu sanamu za kuchonga na sanamu za kuyeyusha

ambazo zipo katika hekalu la miungu yenu.

Nitaandaa kaburi lako,

kwa maana wewe ni mwovu kabisa.”

151:15 Isa 40:9; Rum 10:15; Isa 52:7; Mdo 10:36; Law 23:2-4Tazama, huko juu milimani,

miguu ya huyo mmoja aletaye habari njema,

ambaye anatangaza amani!

Ee Yuda, sherehekea sikukuu zako,

nawe utimize nadhiri zako.

Waovu hawatakuvamia tena;

wataangamizwa kabisa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 1:1-15

1Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

Mkwiyo wa Yehova pa Ninive

2Yehova ndi Mulungu wansanje

ndiponso wobwezera;

Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.

Yehova amabwezera adani ake

ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.

3Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;

ndipo sadzalola kuti munthu

wolakwa asalangidwe.

Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,

ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.

4Amalamulira nyanja ndipo imawuma;

amawumitsa mitsinje yonse.

Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma

ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.

5Mapiri amagwedera pamaso pake

ndipo zitunda zimasungunuka.

Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,

dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.

6Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?

Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?

Ukali wake ukuyaka ngati moto;

matanthwe akunyeka pamaso pake.

7Yehova ndi wabwino,

ndiye kothawirako nthawi ya masautso.

Amasamalira amene amamudalira,

8koma ndi madzi achigumula choopsa

Iye adzawononga adani ake (Ninive);

adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.

9Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova

adzachiwononga kotheratu;

msautso sudzabweranso kachiwiri.

10Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga

ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;

adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.

11Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,

wofuna kuchitira Yehova chiwembu,

amene amapereka uphungu woyipa.

12Yehova akuti,

“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,

kaya iwowo ndi ambiri,

koma adzawonongedwa ndi kutheratu.

Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,

sindidzakuzunzanso.

13Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako

ndipo ndidzadula maunyolo ako.”

14Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,

“Sudzakhala ndi zidzukulu

zimene zidzadziwike ndi dzina lako.

Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba

amene ali mʼnyumba ya milungu yako.

Ine ndidzakukumbira manda

chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”

15Taonani, pa phiripo,

mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,

amene akulengeza za mtendere!

Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu

ndipo kwaniritsani malumbiro anu.

Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;

iwo adzawonongedwa kotheratu.