Isaya 53 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 53:1-12

153:1 Isa 28:9; Yn 12:38; Rum 10:16; Za 98:1; Isa 30:30Ni nani aliyeamini ujumbe wetu,

na mkono wa Bwana umefunuliwa kwa nani?

253:2 Mk 9:12; Isa 52:14; 2Fal 19:26; Ay 14:7; Isa 4:2; 11:10Alikua mbele yake kama mche mwororo

na kama mzizi katika nchi kavu.

Hakuwa na uzuri wala utukufu wa kutuvutia kwake,

hakuwa na chochote katika sura yake cha kutufanya tumtamani.

353:3 Ebr 4:15; Mt 16:21; 27:29; 1Sam 2:30; Za 69:29; Kut 1:10; Lk 18:31-33Alidharauliwa na kukataliwa na wanadamu,

mtu wa huzuni nyingi, ajuaye mateso.

Kama mtu ambaye watu humficha nyuso zao,

alidharauliwa, wala hatukumhesabu kuwa kitu.

453:4 Mt 8:17; Zek 13:7; Yn 19:7; Kum 5:24; Ay 4:5; Yer 23:5-6; Eze 34:23-24; Mik 5:2Hakika alichukua udhaifu wetu

na akajitwika huzuni zetu,

hata hivyo tulidhania kuwa amepigwa na Mungu,

akapigwa sana naye, na kuteswa.

553:5 Kum 32:39; Yn 3:17; 1Pet 2:24-25; 2Nya 7:14; Rum 4:25; 1Kor 15:3; Ebr 9:8; Kut 28:38Lakini alitobolewa kwa ajili ya makosa yetu,

alichubuliwa kwa ajili ya maovu yetu;

adhabu iliyotuletea sisi amani ilikuwa juu yake,

na kwa majeraha yake sisi tumepona.

653:6 Za 119:176; 1Pet 2:25Sisi sote, kama kondoo, tumepotea,

kila mmoja wetu amegeukia njia yake mwenyewe,

naye Bwana aliweka juu yake

maovu yetu sisi sote.

753:7 Mdo 8:32; Mk 14:61; 1Pet 2:23; Isa 49:26; Mt 27:31; Yn 1:29; Za 44:22Alionewa na kuteswa,

hata hivyo hakufungua kinywa chake;

aliongozwa kama mwana-kondoo

apelekwaye machinjoni,

kama vile kondoo anyamazavyo mbele ya wao wamkataye manyoya,

hivyo hakufungua kinywa chake.

853:8 Za 88:5; Dan 9:26; Mdo 8:32-33; Za 39:8; Mk 14:49Kwa kuonewa na kuhukumiwa aliondolewa.

Nani awezaye kueleza kuhusu kizazi chake?

Kwa maana alikatiliwa mbali na nchi ya walio hai,

alipigwa kwa ajili ya makosa ya watu wangu.

953:9 Mk 15:43-46; Lk 23:50-53; Isa 42:1-3; Ay 16:17; Ufu 14:5; Yn 19:19, 38-41Wakamfanyia kaburi pamoja na waovu,

pamoja na matajiri katika kifo chake,

ingawa hakutenda jeuri,

wala hapakuwa na hila kinywani mwake.

1053:10 2Kor 5:21; Mwa 12:17; Za 22:30; Mdo 2:23; Isa 46:10; Law 5:15; Yn 3:17Lakini yalikuwa ni mapenzi ya Bwana

kumchubua na kumsababisha ateseke.

Ingawa Bwana amefanya maisha yake

kuwa sadaka ya hatia,

ataona uzao wake na kuishi siku nyingi,

nayo mapenzi ya Bwana yatafanikiwa mkononi mwake.

1153:11 Yn 10:14-18; Rum 5:18-19; Ay 33:30; Isa 20:3; Mdo 7:52; Yn 1:29; Rum 4:24; Mdo 10:43Baada ya maumivu ya nafsi yake,

ataona nuru ya uzima na kuridhika;

kwa maarifa yake, mtumishi wangu mwenye haki

atawafanya wengi kuwa wenye haki,

naye atayachukua maovu yao.

1253:12 Flp 2:9; Mt 26:28, 38; 27:38; Lk 23:34; Kut 15:9; Za 119:162; Ebr 9:28; Isa 59:19; Rum 8:34; Mk 15:27; Lk 22:37Kwa hiyo nitamgawia sehemu miongoni mwa wakuu,

naye atagawana nyara pamoja na wenye nguvu,

kwa sababu aliyamimina maisha yake hadi mauti,

naye alihesabiwa pamoja na wakosaji.

Kwa kuwa alichukua dhambi za wengi,

na kuwaombea wakosaji.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 53:1-12

1Ndani wakhulupirira zimene tanenazi;

kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?

2Iye anakula ngati mphukira pamaso pake,

ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma.

Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira,

analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.

3Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu,

munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa,

ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona.

Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.

4Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife;

ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu.

Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga,

kumukantha ndi kumusautsa.

5Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu,

ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu;

iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere,

ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.

6Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera,

aliyense mwa ife akungodziyendera;

ndipo Yehova wamusenzetsa

zoyipa zathu zonse.

7Anthu anamuzunza ndi kumusautsa,

koma sanayankhule kanthu.

Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira,

kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta,

momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.

8Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha.

Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake,

poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo?

Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?

9Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa

ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma,

ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa,

kapena kuyankhula za chinyengo.

10Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa.

Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa.

Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali,

ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.

11Atatha mazunzo a moyo wake,

adzaona kuwala, ndipo adzakhutira.

Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri,

popeza adzasenza zolakwa zawo.

12Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu,

adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu,

popeza anapereka moyo wake mpaka kufa,

ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe.

Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri,

ndipo anawapempherera anthu olakwa.