Ayubu 7 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ayubu 7:1-21

Ayubu: Mateso Yangu Hayana Mwisho

17:1 Ay 14:6, 13-14; Isa 40:2; Law 25:50; Za 39:4; Mhu 3:1, 2; Ay 5:7“Je, mwanadamu hana kazi ngumu duniani?

Siku zake si kama zile za mtu aliyeajiriwa?

27:2 Law 19:13; Ay 14:1; Mhu 2:23; Ay 14:6Kama mtumwa anavyovionea shauku vivuli vya jioni,

au mtu aliyeajiriwa anavyoungojea mshahara wake,

37:3 Mhu 4:1; Mao 1:2, 16; Za 39:5; Mhu 1:14; Isa 16:9; Yer 9:1ndivyo nilivyogawiwa miezi ya ubatili,

nami nimeandikiwa huzuni usiku hata usiku.

47:4 Kum 28:67; Ay 7:13-14Wakati nilalapo ninawaza, ‘Itachukua muda gani kabla sijaamka?’

Usiku huwa mrefu, nami najigeuzageuza hadi mapambazuko.

57:5 Ay 17:14; Za 38:5-7; Isa 1:6Mwili wangu umevikwa mabuu na uchafu,

ngozi yangu imetumbuka na kutunga usaha.

Ayubu Anamlilia Mungu

67:6 Za 39:5; 52:9; Isa 38:15; Ay 9:25; 13:15“Siku zangu zinapita upesi kuliko mtande wa kufuma,

nazo zinafikia mwisho wake bila matumaini.

77:7 Mhu 7:15; Yak 4:14; Ay 9:25; Za 78:39Kumbuka, Ee Mungu, maisha yangu ni kama pumzi;

macho yangu kamwe hayataona tena raha.

87:8 Isa 41:12; Mdo 20:25; Ay 20:9Lile jicho linaloniona sasa halitaniona tena;

utanitafuta, wala sitakuwepo.

97:9 Ay 30:15; 38:17; 2Sam 12:23; Za 39:13Kama vile wingu liondokavyo na kutoweka,

vivyo hivyo yeye ashukaye kaburini7:9 Kaburini hapa maana yake ni Kuzimu, kwa Kiebrania ni Sheol. harudi tena.

107:10 Ay 18:21; 21:18; 27:21; Za 58:9; Yer 18:17; 19:8; Za 37:10; 104:35Kamwe harudi tena nyumbani mwake;

wala mahali pake hapatamjua tena.

117:11 Za 39:1, 9“Kwa hiyo sitanyamaza;

nitanena kutokana na maumivu makuu ya roho yangu,

nitalalama kwa uchungu wa nafsi yangu.

127:12 Mwa 1:21; Eze 32:2-3; Ay 38:8-11; Isa 1:14Je, mimi ni bahari, au mnyama mkubwa mno akaaye vilindini,

hata uniweke chini ya ulinzi?

137:13 Ay 7:11Ninapofikiri kwamba kitanda changu kitanifariji,

nacho kiti changu cha fahari kitapunguza malalamiko yangu,

147:14 Ay 9:34; 3:26; Mwa 41:8ndipo wanitisha kwa ndoto

na kunitia hofu kwa maono,

157:15 1Fal 19:4; Yn 4:3; Ay 6:9; Ufu 9:6hivyo ninachagua kujinyonga na kufa,

kuliko huu mwili wangu.

167:16 Mwa 27:46; Za 62:9; 1Fal 19:4; Ay 10:1; Mhu 6:11Ninayachukia maisha yangu; nisingetamani kuendelea kuishi.

Niache; siku zangu ni ubatili.

177:17 Za 144:3; 8:4; Ebr 2:6; Ay 4:19“Mwanadamu ni kitu gani hata umjali kiasi hiki,

kwamba unamtia sana maanani,

187:18 Ay 23:10; 14:3; Za 139:23; 17:3; 26:2; 66:10; 73:14kwamba unamwangalia kila asubuhi

na kumjaribu kila wakati?

197:19 Ay 7:16; 9:18; 13:26; 14:6; 27:2; Za 139:7Je, hutaacha kamwe kunitazama,

au kuniacha japo kwa kitambo kidogo tu?

207:20 Yer 7:19; Ay 6:4; 16:12; 35:6; Za 36:6Ikiwa nimetenda dhambi, nimekufanyia nini,

Ewe mlinzi wa wanadamu?

Kwa nini umeniweka niwe shabaha yako?

Je, nimekuwa mzigo kwako?

217:21 Yer 31:34; Mwa 3:19; Ay 9:28; Ebr 1:3; Za 119:120; 7:5; 22:15; 90:3; 104:29; Isa 43:25Kwa nini husamehi makosa yangu

na kuachilia dhambi zangu?

Kwa kuwa hivi karibuni nitalala mavumbini;

nawe utanitafuta, wala sitakuwepo.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 7:1-21

1“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi?

Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?

2Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo,

kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,

3choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe,

ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.

4Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’

Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.

5Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera,

khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.

6“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu,

ndipo amatha wopanda chiyembekezo.

7Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya;

sindidzaonanso masiku achisangalalo.

8Amene akundiona tsopano akundiona;

mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.

9Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka,

momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera.

10Iye sadzabweranso ku nyumba kwake

ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.

11“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete;

ndidzayankhula mopsinjika mtima,

ndidzadandaula mowawidwa mtima.

12Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja

kuti inu mundiyikire alonda?

13Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga

ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,

14ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto

ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,

15kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa,

kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.

16Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse.

Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.

17“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere,

kuti muzisamala zochita zake,

18kuti muzimusanthula mmawa uliwonse

ndi kumamuyesa nthawi yonse?

19Kodi simudzaleka kumandizonda

kuti ndipezeko mpata wopumula?

20Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu,

Inu wopenyetsetsa anthu?

Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu?

Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?

21Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga

ndi kundichotsera machimo anga?

Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda;

mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”