Ayubu 8 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ayubu 8:1-22

Bildadi Anasema: Yampasa Ayubu Atubu

18:1 Mwa 25:2; Ay 18:1; 25:1Kisha Bildadi Mshuhi akajibu:

28:2 Ay 6:26; 11:2; 2Nya 36:16“Hata lini wewe utasema mambo kama haya?

Maneno yako ni kama upepo mkuu.

38:3 Mwa 18:25; 2Nya 19:7; Kum 32:4; Ay 34:12; Dan 9:14Je, Mungu hupotosha hukumu?

Je, Mwenyezi hupotosha kile kilicho haki?

48:4 Ay 1:5, 18Watoto wako walipomtenda dhambi,

aliwapa adhabu ya dhambi yao.

58:5 Ay 5:8; 11:13; 22:23Lakini ukimtafuta Mungu,

nawe ukamsihi Mwenyezi,

68:6 Za 7:6; Isa 58:9; Ay 5:24; 5:15; 22:27; Isa 65:24ikiwa wewe ni safi na mnyofu,

hata sasa atainuka mwenyewe kwa niaba yako,

na kukurudisha katika mahali pako pa haki.

78:7 Ay 21:13; 22:21; 36:11; Za 25:13; Yer 29:11; 31:17Ijapokuwa mwanzo wako ulikuwa mdogo,

lakini mwisho wako utakuwa wa mafanikio.

88:8 Kum 4:32; 32:7; Za 71:18; Ay 15:18“Ukaulize vizazi vilivyotangulia

na uone baba zao walijifunza nini,

98:9 Mwa 47:9; 2Nya 10:6; Za 39:5-6; 1Nya 29:15; Ay 7:6kwa kuwa sisi tumezaliwa jana tu na hatujui lolote,

nazo siku zetu duniani ni kama kivuli tu.

108:10 Mt 1:8; 2:1-2; 4:1Je, hawatakufundisha na kukueleza?

Je, hawataleta maneno kutoka kwenye kufahamu kwao?

118:11 Ay 40:21; Kut 2:3; Isa 19:6; 35:7Je, mafunjo yaweza kumea mahali pasipo na matope?

Matete yaweza kustawi bila maji?

128:12 Isa 34:4; Yer 17:6; Za 129:6; Yak 1:10, 11; 1Pet 1:24Wakati bado yanaendelea kukua kabla ya kukatwa,

hunyauka haraka kuliko majani mengine.

138:13 Za 50:13; 112:10; Mit 10:28; Yer 15:9; Ay 11:20; 18:14; Isa 33:14; Mt 24:51; Lk 12:1Huu ndio mwisho wa watu wote wanaomsahau Mungu;

vivyo hivyo matumaini ya wasiomjali Mungu huangamia.

148:14 Ay 8:15; 27:18; Isa 59:5Lile analolitumainia huvunjika upesi;

lile analolitegemea ni utando wa buibui.

158:15 Ay 27:18; 8:12; Za 49:11; Mt 7:26-27Huutegemea utando wake, lakini hausimami;

huungʼangʼania, lakini haudumu.

168:16 Za 80:11; 37:35; Isa 16:5; Yer 11:16Yeye ni kama mti ulionyeshewa vizuri wakati wa jua,

ukieneza machipukizi yake bustanini;

17huifunganisha mizizi yake kwenye lundo la mawe,

na kutafuta nafasi katikati ya mawe.

188:18 Ay 14:20; 7:10; Za 37:36; 103:16Unapongʼolewa kutoka mahali pake,

ndipo mahali pale huukana na kusema,

‘Mimi kamwe sikukuona.’

198:19 Za 113:7Hakika uhai wake hunyauka,

na kutoka udongoni mimea mingine huota.

208:20 Mwa 18:25; Ay 21:30; 1The 5:23-24; Za 37:24“Hakika Mungu hamkatai mtu asiye na hatia,

wala kuitia nguvu mikono ya mtenda mabaya.

218:21 Ay 5:22; Ezr 3:13; Isa 35:6; Za 47:5; 107:22Bado atakijaza kinywa chako na kicheko,

na midomo yako na kelele za shangwe.

228:22 Za 6:10; Eze 7:27; 1Sam 8:3; Mit 14:11; Ay 18:6Adui zako watavikwa aibu,

nazo hema za waovu hazitakuwepo tena.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 8:1-22

Mawu a Bilidadi

1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

2“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti?

Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.

3Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama?

Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?

4Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu,

Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.

5Koma utayangʼana kwa Mulungu,

ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,

6ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima

ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako

ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.

7Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa

koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.

8“Funsa kwa anthu amvulazakale

ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira

9pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse,

ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.

10Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera?

Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?

11Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho?

Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?

12Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula;

zimawuma msangamsanga kuposa bango.

13Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu;

ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.

14Kulimba mtima kwake kumafowoka;

zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.

15Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka;

amawugwiritsitsa koma sulimba.

16Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa,

nthambi zake zimatambalala pa munda wake;

17mizu yake imayanga pa mulu wa miyala

ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.

18Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo,

pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’

19Ndithudi chomeracho chimafota,

ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.

20“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa

kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.

21Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete

ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.

22Adani ako adzachita manyazi,

ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”