Mashahidi Waitwa Dhidi Ya Israeli
13:1 Amo 2:10; Sef 2:5Sikilizeni neno hili alilosema Bwana dhidi yenu, enyi watu wa Israeli, dhidi ya jamaa nzima niliowapandisha toka Misri:
23:2 Kut 19:6; 1Pet 4:17; Lk 12:47; Mik 2:3; Eze 9:6; Dan 9:12; Mt 11:22; Rum 2:9; Kum 7:6; Yer 14:10“Ni ninyi tu niliowachagua
kati ya jamaa zote za dunia;
kwa hiyo nitawaadhibu
kwa ajili ya dhambi zenu zote.”
3Je, watu wawili hutembea pamoja
wasipokubaliana kufanya hivyo?
43:4 Za 104:21; Hos 5:14; Isa 42:13Je, simba hunguruma katika kichaka
wakati hana mawindo?
Aweza kuvuma katika pango
wakati ambao hajakamata chochote?
5Je, ndege aweza kuanguka kwenye mtego ulio ardhini
ambapo hajategewa chambo?
Je, mtego unaweza kufyatuka toka ardhini
wakati ambapo hakuna chochote cha kunasa?
63:6 Isa 14:24-27; 31:2; 45:7; Hes 10:2; Eze 33:3; Ay 39:24; Yer 4:21Je, tarumbeta inapopigwa mjini kujulisha hatari,
watu hawatetemeki?
Mji upatwapo na maafa,
je, si Bwana amesababisha?
73:7 1Sam 3:7; Mwa 6:13; 18:17; Mit 3:32; Yn 15:15; Yer 23:22; Mit 3:32; Dan 9:22-27; Ufu 1:1, 19Hakika Bwana Mwenyezi hatafanya neno lolote
bila kuwafunulia watumishi wake manabii siri yake.
83:8 1Kor 9:16; Yn 3:1-3; Mdo 4:20; Isa 31:4; 42:13; Yer 20:9Simba amenguruma:
je, ni nani ambaye hataogopa?
Bwana Mwenyezi ametamka:
je, ni nani awezaye kukosa kutoa unabii?
93:9 Yos 13:3; 2Nya 26:6Tangazeni katika ngome za Ashdodi
na katika ngome za Misri:
“Kusanyikeni juu ya milima ya Samaria;
angalieni wingi wa wasiwasi ulio ndani yake,
na uonevu ulio miongoni mwa watu wake.”
103:10 Yer 4:22; Amo 6:12; 5:7; Mik 6:10; Hab 2:8Bwana asema: “Hawajui kutenda lililo jema,
wale ambao hujilundikia nyara
na vitu vilivyotekwa katika ngome zao.”
113:11 Amo 2:5; 6:14; 2Fal 17:6Kwa hiyo hili ndilo asemalo Bwana Mwenyezi:
“Adui ataizingira nchi;
ataangusha chini ngome zenu
na kuteka nyara maboma yenu.”
123:12 1Sam 17:34; Es 1:6; Amo 6:4Hili ndilo asemalo Bwana:
“Kama vile mchungaji aokoavyo kinywani mwa simba
vipande viwili tu vya mfupa wa mguu
au kipande cha sikio,
hivyo ndivyo Waisraeli watakavyookolewa,
wale wakaao Samaria
kwenye kingo za vitanda vyao,
na katika Dameski
kwenye viti vyao vya fahari.”
13“Sikia hili na ushuhudie dhidi ya nyumba ya Yakobo,” asema Bwana, Bwana Mungu Mwenye Nguvu Zote.
143:14 Mwa 12:8; Amo 5:5-6; Kut 27:2; Law 26:18“Siku nitakapomwadhibu Israeli kwa sababu ya dhambi zake,
nitaharibu madhabahu za Betheli;
pembe za madhabahu zitakatiliwa mbali
na kuanguka chini.
153:15 Yer 36:22; Amu 3:20; 1Fal 22:39; Hos 10:5-8; Isa 34:5; Amo 5:11; 6:11Nitabomoa nyumba ya wakati wa masika,
pamoja na nyumba ya wakati wa kiangazi;
nyumba zilizonakshiwa kwa pembe za ndovu
na majumba makubwa ya fahari yatabomolewa,”
asema Bwana.
Mboni Zotsutsa Israeli
1Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
2“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani
pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;
nʼchifukwa chake ndidzakulangani
chifukwa cha machimo anu onse.”
3Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi
asanapangane?
4Kodi mkango umabangula mʼnkhalango
usanagwire nyama?
Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake
pamene sunagwire kanthu?
5Kodi mbalame nʼkutera pa msampha
pamene palibe nyambo yake?
Kodi msampha umafwamphuka
usanakole kanthu?
6Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,
anthu sanjenjemera?
Pamene tsoka lafika mu mzinda,
kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
7Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu
asanawulule zimene akufuna kuchita
kwa atumiki ake, aneneri.
8Mkango wabangula,
ndani amene sachita mantha?
Ambuye Yehova wayankhula,
ndani amene sanganenere?
9Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi
ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:
“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;
onani chisokonezo pakati pake
ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
10“Iwo sadziwa kuchita zolungama,
ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
11Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:
“Mdani adzalizungulira dzikoli;
iye adzagwetsa malinga ako,
ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
12Yehova akuti,
“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango
miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,
moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli
amene amakhala mu Samariya
pa msonga za mabedi awo,
ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
13“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
14“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,
ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;
nyanga za guwa zidzathyoka
ndipo zidzagwa pansi.
15Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira
pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;
nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa
ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”
akutero Yehova.