ኤርምያስ 5 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኤርምያስ 5:1-31

ቅን ሰው አለመገኘቱ

1“በኢየሩሳሌም መንገዶች እስቲ ውጡ፤ ወደ ላይ ወደ ታችም ውረዱ፤

ዙሪያውን ተመልከቱ ቃኙ፤

በአደባባይዋም ፈልጉ፤

እውነትን የሚሻና በቅንነት የሚሄድ፣

አንድ ሰው እንኳ ብታገኙ፣

እኔ ይህችን ከተማ እምራታለሁ።

2‘ሕያው እግዚአብሔርን!’ ቢሉም፣

የሚምሉት በሐሰት ነው።”

3እግዚአብሔር ሆይ፤ ዐይኖችህ እውነትን አይመለከቱምን?

አንተ መታሃቸው፤ እነርሱ ግን አልተሰማቸውም፤

አደቀቅሃቸው፤ እነርሱ ግን አልታረሙም፤

ፊታቸውን ከድንጋይ ይልቅ አጠነከሩ

በንስሓ ለመመለስም አልፈለጉም።

4እኔም በልቤ እንዲህ አልሁ፤ “እነዚህ ድኾች ናቸው፤

ሞኞች ናቸው፤

የእግዚአብሔርን መንገድ፣

የአምላካቸውን ሕግ አላወቁምና።

5ስለዚህ ወደ ታላላቆቹ እሄዳለሁ፤

ለእነርሱም እናገራለሁ፤

በርግጥ እነርሱ የእግዚአብሔርን መንገድ፣

የአምላካቸውንም ሕግ ያውቃሉና።”

ነገር ግን እነርሱም ቢሆኑ ያው እንደዚያው ቀንበሩን ሰብረዋል፤

እስራቱንም በጥሰዋል።

6ስለዚህ አንበሳ ከዱር ወጥቶ ይሰባብራቸዋል፣

የበረሓ ተኵላም ይቦጫጭቃቸዋል፤

ብቅ የሚለውን ሰው ሁሉ ለመገነጣጠል፣

ነብር በከተሞቻቸው ዙሪያ ያደባል፤

ዐመፃቸው ታላቅ፣

ክሕደታቸው ብዙ ነውና።

7“ታዲያ፣ እንዴት ይቅር ልልሽ እችላለሁ?

ልጆችሽ ትተውኛል፤

እውነተኛውን አምላክ ትተው አማልክት ባልሆኑት ምለዋል፤

እስኪጠግቡ ድረስ መገብኋቸው፤

እነርሱ ግን አመነዘሩ፤

ወደ ጋለሞቶችም ቤት ተንጋጉ።

8እንደ ተቀለበ ብርቱ ድንጉላ ፈረስ ሆኑ፤

እያንዳንዱም የሌላውን ሚስት ተከትሎ አሽካካ።

9ስለ እነዚህ ነገሮች አልቀጣቸውምን?”

ይላል እግዚአብሔር

“እኔ ራሴ እንደዚህ ዐይነቱን ሕዝብ

አልበቀልምን?

10“ወደ ወይን አትክልቷ ስፍራ ገብታችሁ አበላሹት፤

ነገር ግን ፈጽማችሁ አታጥፉት፤

ቅርንጫፎቿን ገነጣጥሉ፤

የእግዚአብሔር አይደሉምና፤

11የእስራኤል ቤትና የይሁዳ ቤት፣

ፈጽመው ከድተውኛል፤”

ይላል እግዚአብሔር

12በእግዚአብሔር ላይ ሐሰትን ተናገሩ፤

እንዲህም አሉ፤ “እሱ ምንም አያደርግም!

ክፉ ነገር አይደርስብንም፤

ሰይፍም ራብም አናይም፤

13ነቢያቱ ነፋስ እንጂ ሌላ ነገር አይደሉም፤

ቃሉም በውስጣቸው የለም፤

ያሉት ሁሉ በእነርሱ ላይ ይመለስ።”

14ስለዚህ የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“ሕዝቡ ይህን ቃል ስለ ተናገረ፣

ቃሌን በአፍህ ውስጥ የሚፋጅ እሳት፣

ይህንም ሕዝብ ማገዶ አደርጋለሁ፤

እሳቱም ይበላቸዋል፤

15የእስራኤል ቤት ሆይ፤” ይላል እግዚአብሔር

“ከሩቅ ሕዝብን አመጣባችኋለሁ፤

ጥንታዊና ብርቱ፣

ቋንቋውን የማታውቁት፣ ንግግሩንም

የማትረዱት ሕዝብ ነው።

16የፍላጻቸው ሰገባ እንደ ተከፈተ መቃብር ነው፤

ሁሉም ብርቱ ተዋጊዎች ናቸው።

17ሰብልህንና ምግብህን ጠራርገው ይበሉብሃል፤

ወንዶችና ሴቶች ልጆችህን ይውጣሉ፤

በጎችህንና ከብቶችህን ይፈጃሉ፤

የወይን ተክሎችህንና የበለስ ዛፎችህን ያወድማሉ፤

የታመንህባቸውንም የተመሸጉ ከተሞች

በሰይፍ ያጠፏቸዋል።

18“ይሁን እንጂ፣ በዚያን ዘመን እንኳ” ይላል እግዚአብሔር፤ “ፈጽሜ አላጠፋችሁም። 19ሕዝቡ፣ ‘እግዚአብሔር አምላካችን ይህን ሁሉ ነገር ለምን አደረገብን?’ ብለው ቢጠይቁ፣ ‘እኔን፣ እንደ ተዋችሁኝና በራሳችሁ ምድር ባዕዳን አማልክትን እንዳገለገላችሁ፣ እንደዚሁ የእናንተ ባልሆነ ምድር ባዕዳንን ታገለግላላችሁ’ ትላቸዋለህ።

20“በያዕቆብ ቤት ይህን አሰሙ፤

በይሁዳም እንዲህ ብላችሁ ዐውጁ፤

21እናንት ዐይን እያላችሁ የማታዩ፣

ጆሮ እያላችሁ የማትሰሙ፣

ሞኞችና የማታስተውሉ ሰዎች ይህን ስሙ፤

22ልትፈሩኝ አይገባችሁምን?” ይላል እግዚአብሔር

“በእኔ ፊት ልትንቀጠቀጡስ አይገባምን?

ለዘላለም ዐልፎት መሄድ እንዳይችል፣

አሸዋን ለባሕር ድንበር አደረግሁ፤

ማዕበሉ እየጋለበ ቢመጣ ከዚያ አያልፍም፤

ሞገዱ ቢጮኽም ሊያቋርጠው አይችልም።

23ይህ ሕዝብ ግን የሸፈተና እልኸኛ ልብ አለው፤

መንገድ ለቆ ሄዷል፤

24በልባቸውም፣

‘የፊተኛውንና የኋለኛውን ዝናብ በጊዜው የሚያዘንበውን፣

መከርን በወቅቱ የሚያመጣልንን፣

አምላካችንን እግዚአብሔርን እንፍራ’ አላሉም።

25በደላችሁ እነዚህን አስቀርቶባችኋል።

ኀጢአታችሁ መልካሙን ነገር ከልክሏችኋል።

26“በሕዝቤ መካከል ክፉ ሰዎች አሉና፤

ወፍ እንደሚያጠምዱ ሰዎች፣

ወጥመድ ዘርግተው ሰው እንደሚይዙ ሰዎችም ያደባሉ።

27ወፎች እንደ ሞሉት ጐጆ፣

ቤታቸው በማጭበርበር የተሞላ ነው፤

ባለጠጎችና ኀያላን ሆነዋል፤

28ወፍረዋል፤ ሠብተዋልም።

ክፋታቸው ገደብ የለውም፤

ወላጅ የሌላቸው ፍትሕ እንዲያገኙ

አልቆሙላቸውም፤

ለድኾችም መብት አልተከራከሩም።

29ስለ እነዚህ ነገሮች ልቀጣቸው አይገባኝምን?”

ይላል እግዚአብሔር

እንዲህ ዐይነቶቹን ሕዝብ፣

እኔ ራሴ ልበቀላቸው አይገባኝምን?

30“የሚያስፈራና የሚያስደነግጥ ነገር

በምድሪቱ ላይ ሆኗል፤

31ነቢያት በሐሰት ትንቢት ይናገራሉ፤

ካህናት በነቢያቱ ምክር ያስተዳድራሉ፤

ሕዝቤም እንዲህ ያለውን ይወድዳሉ፤

ፍጻሜው ሲደርስ ግን ምን ታደርጉ ይሆን?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 5:1-31

Palibe Munthu Wolungama

1“Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu,

mudzionere nokha,

funafunani mʼmabwalo ake.

Ngati mungapeze munthu mmodzi

amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi,

ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.

2Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’

komabe akungolumbira mwachinyengo.”

3Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona?

Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka;

munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro.

Anawumitsa mitima yawo ngati mwala

ndipo anakaniratu kulapa.

4Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe;

anthu ochita zopusa.

Sadziwa njira ya Yehova,

sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.

5Tsono ndidzapita kwa atsogoleri

ndi kukayankhula nawo;

ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova,

amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.”

Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova

ndipo anadula msinga zawo.

6Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha,

mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga,

kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo

kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo

pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu

ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.

7Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita?

Ana anu andisiya Ine

ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse.

Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa,

komabe iwo anachita chigololo

namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.

8Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa,

aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.

9Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?”

akutero Yehova.

“Kodi nʼkuleka kuwulipsira

mtundu woterewu?

10“Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga,

koma musakayiwononge kotheratu.

Sadzani nthambi zake

pakuti anthu amenewa si a Yehova.

11Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda

onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”

12Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti,

“Yehova sangachite zimenezi!

Choyipa sichidzatigwera;

sitidzaona nkhondo kapena njala.

13Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo;

ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova.

Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”

14Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti,

“Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa,

tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako

ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.

15Inu Aisraeli,” Yehova akuti,

“Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali,

ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo,

mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa,

zimene akunena inu simungazimvetse.

16Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri;

onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.

17Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu,

adzapha ana anu aamuna ndi aakazi;

adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu,

adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu.

Ndi malupanga awo adzagwetsa

mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.

18“Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova. 19Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”

20“Lengeza izi kwa ana a Yakobo

ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,

21Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru,

inu amene maso muli nawo koma simupenya,

amene makutu muli nawo koma simumva.

22Kodi simuyenera kuchita nane mantha?”

Akutero Yehova.

“Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga?

Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja,

malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo.

Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo;

mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.

23Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira;

andifulatira ndipo andisiyiratu.

24Sananenepo mʼmitima mwawo kuti,

‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu.

Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika.

Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’

25Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi;

ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.

26“Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa

amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame

ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.

27Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo

ngati zikwere zodzaza ndi mbalame.

Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.

28Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala.

Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire;

saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino,

sateteza ufulu wa anthu osauka.

29Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?

Kodi ndisawulipsire

mtundu woterewu?

Akutero Yehova.

30“Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri

chachitika mʼdzikomo:

31Aneneri akunenera zabodza,

ndipo ansembe akuvomerezana nawo,

ndipo anthu anga akukonda zimenezi.

Koma mudzatani potsiriza?