ኤርምያስ 4 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኤርምያስ 4:1-31

1“እስራኤል ሆይ፤ ብትመለስ፣

ወደ እኔ ብትመለስ”

ይላል እግዚአብሔር

“አስጸያፊ ነገሮችህን ከፊቴ ብታስወግድ፣

ባትናወጥ ብትቆምም፣

2በእውነት፣ በቅንነትና በጽድቅ፣

‘ሕያው እግዚአብሔርን!’ ብለህ ብትምል፣

አሕዛብ በእርሱ ይባረካሉ፤

በእርሱም ይከበራሉ።”

3እግዚአብሔር ለይሁዳና ለኢየሩሳሌም ሰዎች እንዲህ ይላል፤

“ዕዳሪውን መሬት ዕረሱ፤

በእሾኽም መካከል አትዝሩ።

4እናንተ የይሁዳ ሰዎች፣ የኢየሩሳሌምም ነዋሪዎች፤

ለእግዚአብሔር ተገረዙ፤

የልባችሁንም ሸለፈት አስወግዱ፤

አለዚያ ስለ ሠራችሁት ክፋት፣

ቍጣዬ እንደ እሳት ይንበለበላል፤

ሊገታውም የሚችል የለም።

ጥፋት ከሰሜን መምጣቱ

5“ ‘በምድሪቱ ሁሉ መለከትን ንፉ’ ብላችሁ፤

በይሁዳ ተናገሩ፣ በኢየሩሳሌም ዐውጁ፤

ጩኹ፤ እንዲህም በሉ፤

‘በአንድነት ተሰብሰቡ፤

ወደ ተመሸጉት ከተሞች እንሽሽ!’

6ወደ ጽዮን ለመግባት ሰንደቅ ዐላማ አንሡ፤

ቶሎ ሸሽታችሁ አምልጡ፤

ከሰሜን መቅሠፍትን፣

ታላቅ ጥፋትን አመጣለሁና።”

7አንበሳ ከደኑ ወጥቷል፤

ሕዝብንም የሚያጠፋ ተሰማርቷል፤

ምድርሽን ባዶ ሊያደርግ፣

ከስፍራው ወጥቷል።

ከተሞችሽ ፈራርሰው ይወድቃሉ፤

ያለ ነዋሪም ይቀራሉ።

8ስለዚህ ማቅ ልበሱ፤

ዕዘኑ፤ ዋይ በሉ፤

የእግዚአብሔር አስፈሪ ቍጣ፣

ከእኛ አልተመለሰምና።

9“በዚያ ቀን” ይላል እግዚአብሔር

“ንጉሡና ሹማምቱ ወኔ ይከዳቸዋል፤

ካህናቱ ድንጋጤ ይውጣቸዋል፤

ነቢያቱም ብርክ ይይዛቸዋል።”

10እኔም፣ “ጌታ እግዚአብሔር ሆይ፤ ሰይፍ ዐንገታቸው ላይ ተቃጥቶ ሳለ፣ ‘ሰላም ይሆንላችኋል’ ብለህ ይህን ሕዝብና ኢየሩሳሌምን ለምን እጅግ አታለልህ?” አልሁ።

11በዚያን ጊዜ፣ ለእዚህ ሕዝብና ለኢየሩሳሌም እንዲህ ተብሎ ይነገራል፤ “ለማበጠር ወይም ለማጥራት ሳይሆን፣ ከዚያ የበረታ የሚጠብስ ደረቅ ነፋስ በምድረ በዳ ካሉት ባድማ ኰረብቶች ወደ ወገኔ ሴት ልጅ 12በእኔ ትእዛዝ ይነፍሳል፤4፥12 ወይም በእኔ ትእዛዝ የሚመጣው እንግዲህ ፍርዴን በእነርሱ ላይ እናገራለሁ።”

13እነሆ፤ እንደ ደመና ይንሰራፋል፤

ሠረገሎቹ እንደ ዐውሎ ነፋስ ይመጣሉ፤

ፈረሶቹም ከንስር ይፈጥናሉ፤

መጥፋታችን ነውና ወዮልን!

14ኢየሩሳሌም ሆይ፤ እንድትድኚ ከልብሽ ክፋት ታጠቢ፤

እስከ መቼ ክፉ ሐሳብ በውስጥሽ ይኖራል?

15ድምፅ ከዳን ይሰማልና፤

ከኤፍሬም ተራሮችም ጥፋትን ያውጃል።

16“ይህን ለሕዝቦች አሳውቁ፤

ለኢየሩሳሌምም እንዲህ ብላችሁ በይፋ ንገሩ፤

‘ከብበው የሚያስጨንቁ ከሩቅ አገር ይመጣሉ፤

በይሁዳ ከተሞችም ላይ ይደነፋሉ፤

17ሰብል እንደሚጠብቁ ሰዎች ይከቧታል፤

በእኔ ላይ ዐምፃለችና፤’ ”

ይላል እግዚአብሔር

18“የገዛ መንገድሽና ተግባርሽ፣

ይህን አምጥቶብሻል፤

ይህም ቅጣትሽ ነው፤

ምንኛ ይመርራል!

እንዴትስ ልብ ይሰብራል!”

19ወይ አበሳዬ! ወይ አበሳዬ!

ሥቃይ በሥቃይ ላይ ሆነብኝ፤

አወይ፣ የልቤ ጭንቀት!

ልቤ ክፉኛ ይመታል፤

ዝም ማለት አልችልም፤

የመለከትን ድምፅ፣

የጦርነትንም ውካታ ሰምቻለሁና።

20ጥፋት በጥፋት ላይ ይመጣል፤

ምድሪቱም በሞላ ባድማ ትሆናለች፤

ድንኳኔ በድንገት፣

መጠለያዬም በቅጽበት ጠፋ።

21እስከ መቼ የጦርነት ዐርማ እመለከታለሁ?

እስከ መቼስ የመለከት ድምፅ እሰማለሁ?

22“ሕዝቤ ተላሎች ናቸው፤

እኔን አያውቁኝም።

ማስተዋል የጐደላቸው፣

መረዳትም የማይችሉ ልጆች ናቸው።

ክፋትን ለማድረግ ጥበበኞች፣

መልካም መሥራት ግን የማያውቁ።”

23ምድርን ተመለከትሁ፤

እነሆ ቅርጽ የለሽና ባዶ ነበረች፤

ሰማያትንም አየሁ፣

ብርሃናቸው ጠፍቷል።

24ተራሮችን ተመለከትሁ፣

እነሆ ይንቀጠቀጡ ነበር፤

ኰረብቶችም ሁሉ ተናጡ።

25አየሁ፤ ሰው አልነበረም፤

የሰማይ ወፎች ሁሉ በረው ጠፍተዋል።

26ተመለከትሁ፤ እነሆም፣ ፍሬያማው ምድር በረሓ ሆነ፤

ከተሞቹ ሁሉ በእግዚአብሔር ፊት፣

ከብርቱ ቍጣው የተነሣ ፈራረሱ።

27እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“ምድር ሁሉ ባድማ ትሆናለች፤

ነገር ግን ፈጽሜ አላጠፋትም።

28ስለዚህ ምድር ታለቅሳለች፤

ሰማያትም በላይ ይጨልማሉ፤

ተናግሬአለሁ፤ ሐሳቤን አልለውጥም፤

ወስኛለሁ፤ ወደ ኋላም አልልም።”

29ከፈረሰኞችና ከቀስተኞች ጩኸት የተነሣ፣

ከተማ ሁሉ ይሸሻል፤

አንዳንዶች ደን ውስጥ ይገባሉ፤

ሌሎችም ቋጥኝ ላይ ይወጣሉ፤

ከተሞች ሁሉ ባዶ ቀርተዋል፤

የሚኖርባቸውም የለም።

30አንቺ ለጥፋት የተዳረግሽ ሆይ፤ ምን መሆንሽ ነው?

ቀይ ቀሚስ የለበስሽው ለምንድን ነው?

ለምን በወርቅ አጌጥሽ?

ዐይኖችሽንስ ለምን ተኳልሽ?

እንዲያው በከንቱ ተሽሞንሙነሻል፤

የተወዳጀሻቸው ንቀውሻልና፤

ነፍስሽንም ሊያጠፉ ይፈልጋሉ።

31የበኵር ልጇን ለመውለድ እንደምታምጥ፣

በወሊድ እንደምትጨነቅ ሴት ድምፅ ሰማሁ፤

የጽዮን ሴት ልጅ ትንፋሽ ዐጥሯት ስትጮኽ፣

እጇን ዘርግታ፣

“ወዮልኝ! ተዝለፈለፍሁ፣

በነፍሰ ገዳዮች እጅ ወደቅሁ!” ስትል ሰማሁ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 4:1-31

1“Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli,

bwererani kwa Ine,”

akutero Yehova.

“Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga

ndipo musasocherenso.

2Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo

kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’

Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse

ndipo adzanditamanda.”

3Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi:

“Limani masala anu

musadzale pakati pa minga.

4Dziperekeni nokha kwa Ine

kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse,

inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu.

Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani,

chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo

popanda wina wowuzimitsa.

Adani Ochokera Kumpoto kwa Yuda

5“Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti,

‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’

Ndipo fuwulani kuti,

‘Sonkhanani!

Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’

6Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni!

Musachedwe, thawani kuti mupulumuke!

Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto,

kudzakhala chiwonongeko choopsa.”

7Monga mkango umatulukira mʼngaka yake

momwemonso wowononga mayiko

wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake.

Watero kuti awononge dziko lanu.

Mizinda yanu idzakhala mabwinja

popanda wokhalamo.

8Choncho valani ziguduli,

lirani ndi kubuwula,

pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova

sunatichokere.

9“Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima,

ansembe adzachita mantha kwambiri,

ndipo aneneri adzathedwa nzeru,”

akutero Yehova.

10Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”

11Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa; 12koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”

13Taonani, adani akubwera ngati mitambo,

magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu,

akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga.

Tsoka ilo! Tawonongeka!

14Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke.

Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?

15Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani;

akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.

16Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina,

lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti,

‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali,

akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.

17Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda,

chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’ ”

akutero Yehova.

18“Makhalidwe anu ndi zochita zanu

zakubweretserani zimenezi.

Chimenechi ndiye chilango chanu.

Nʼchowawa kwambiri!

Nʼcholasa mpaka mu mtima!”

19Mayo, mayo,

ndikumva kupweteka!

Aa, mtima wanga ukupweteka,

ukugunda kuti thi, thi, thi.

Sindingathe kukhala chete.

Pakuti ndamva kulira kwa lipenga;

ndamva mfuwu wankhondo.

20Tsoka limatsata tsoka linzake;

dziko lonse lasanduka bwinja.

Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa,

mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.

21Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo,

ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?

22Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru;

iwo sandidziwa.

Iwo ndi ana opanda nzeru;

samvetsa chilichonse.

Ali ndi luso lochita zoyipa,

koma sadziwa kuchita zabwino.”

23Ndinayangʼana dziko lapansi,

ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu;

ndinayangʼana thambo,

koma linalibe kuwala kulikonse.

24Ndinayangʼana mapiri,

ndipo ankagwedezeka;

magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.

25Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu;

mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.

26Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu;

mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja

pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.

27Yehova akuti,

“Dziko lonse lidzasanduka chipululu

komabe sindidzaliwononga kotheratu.

28Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira

ndipo thambo lidzachita mdima,

pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima,

ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”

29Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi,

anthu a mʼmizinda adzathawa.

Ena adzabisala ku nkhalango;

ena adzakwera mʼmatanthwe

mizinda yonse nʼkuyisiya;

popanda munthu wokhalamo.

30Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja!

Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira

ndi kuvalanso zokometsera zagolide?

Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera,

ukungodzivuta chabe.

Zibwenzi zako zikukunyoza;

zikufuna kuchotsa moyo wako.

31Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka,

kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba.

Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu.

Atambalitsa manja awo nʼkumati,

“Kalanga ife! Tikukomoka.

Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”