ኢዮብ 19 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢዮብ 19:1-29

ኢዮብ

1ኢዮብም እንዲህ ሲል መለሰ፤

2“ነፍሴን የምታስጨንቋት፣

በቃልስ የምትደቍሱኝ እስከ መቼ ነው?

3እነሆ፤ ዐሥር ጊዜ ዘለፋችሁኝ፤

ያለ ዕፍረትም በደላችሁኝ።

4በእውነት ተሳስቼ ከሆነ፣

ስሕተቱ የራሴ ጕዳይ ነው።

5ነገር ግን ራሳችሁን በእኔ ላይ ከፍ ብታደርጉ፣

መዋረዴንም እኔን ለመሞገት ብትጠቀሙበት፣

6እግዚአብሔር እንደ በደለኝ፣

በመረቡም እንደ ከበበኝ ዕወቁ።

7“ ‘ተበደልሁ’ ብዬ ብጮኽ ማንም አይመልስልኝም፤

ድምፄን ከፍ አድርጌ ባሰማም፣ ፍትሕ አላገኝም።

8እንዳላልፍ መንገዴን ዘግቷል፤

መሄጃዬንም በጨለማ ጋርዷል።

9ክብሬን ገፍፎኛል፤

ዘውዴንም ከራሴ ላይ ወስዷል።

10እስክወገድ ድረስ በሁሉ አቅጣጫ አፈራርሶኛል፤

ተስፋዬንም እንደ ዛፍ ነቅሎታል።

11ቍጣው በላዬ ነድዷል፤

እንደ ጠላቱም ቈጥሮኛል።

12ሰራዊቱ ገፍተው መጡ፤

በዙሪያዬ ምሽግ ሠሩ፤ ድንኳኔንም ከብበው ሰፈሩ።

13“ወንድሞቼን ከእኔ አርቋል፤

ከሚያውቁኝም ተገለልሁ።

14ዘመዶቼ ትተውኛል፤

ወዳጆቼም ረስተውኛል።

15የቤቴ እንግዶችና ሴት አገልጋዮቼ እንደ መጻተኛ ቈጠሩኝ፤

እንደ ባዕድም ተመለከቱኝ፤

16አገልጋዬን ብጣራ፣

በአንደበቴም ብለምነው፣ አይመልስልኝም።

17እስትንፋሴ ለሚስቴ እንኳ የሚያስጠላት ሆነ፤

የገዛ ወንድሞቼም ተጸየፉኝ።

18ሕፃናት እንኳ ይንቁኛል፤

ባዩኝም ቍጥር ያላግጡብኛል።

19የቅርብ ወዳጆቼ ሁሉ ተጸየፉኝ፤

የምወድዳቸውም በላዬ ተነሡ፤

20ቈዳና ዐጥንት ብቻ ሆኜ ቀረሁ፤

ድድ ብቻ ቀርቶልኝ አመለጥሁ።

21“ወዳጆቼ ሆይ፤ ራሩልኝ፤

የእግዚአብሔር እጅ መትታኛለችና ዕዘኑልኝ።

22እግዚአብሔር እንዳሳደደኝ ለምን ታሳድዱኛላችሁ?

አሁንም ሥጋዬ አልበቃችሁምን?

23“ምነው ቃሌ በተጻፈ ኖሮ!

በመጽሐፍም በታተመ!

24ምነው በብረትና በእርሳስ በተጻፈ ኖሮ!

በዐለትም ላይ በተቀረጸ!

25የሚቤዠኝ ሕያው እንደ ሆነ፣

በመጨረሻም በምድር ላይ እንደሚቆም ዐውቃለሁ።

26ቈዳዬ ቢጠፋም፣

ከሥጋዬ ብለይም፣ እግዚአብሔርን አየዋለሁ፤

27ሌላ ሳይሆን እኔው በገዛ ዐይኔ፣

እኔ ራሴ አየዋለሁ፤

ልቤ በውስጤ ምንኛ በጉጉት ዛለ!

28“ ‘የችግሩ መንሥኤ በውስጡ19፥28 አብዛኞቹ የዕብራይስጥ ቅጆች፣ የሰብዓ ሊቃናት ትርጕምና ቩልጌት፣ በእኔ ይላሉ። አለ፤

እኛ እንዴት እናሳድደዋለን?’ ብትሉ፣

29ቍጣ በሰይፍ መቀጣትን ያስከትላልና፣

ራሳችሁ ሰይፍን ፍሩ፤

በዚያን ጊዜ ፍርድ19፥29 ወይም ሁሉን ቻዩን ታውቃላችሁ ማለት ነው። እንዳለ ታውቃላችሁ።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 19:1-29

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti,

ndi kundilasa ndi mawu anuwo?

3Inuyo mwandinyoza kwambiri;

mwanditsutsa mopanda manyazi.

4Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera,

cholakwachotu nʼchanga.

5Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga,

ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,

6pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira

ndipo wandizinga ukonde wake.

7“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha;

ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.

8Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa;

waphimba njira zanga ndi mdima.

9Iye wandilanda ulemu wanga

ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.

10Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu;

Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.

11Wandikwiyira ndipo

akundiyesa mmodzi mwa adani ake.

12Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu,

akonzekera zodzalimbana nane

ndipo azungulira nyumba yanga.

13“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga;

wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.

14Abale anga andithawa;

abwenzi anga andiyiwala.

15Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo;

ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.

16Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha,

ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.

17Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga;

ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.

18Inde, ngakhale ana amandinyoza;

akandiona amandinyodola.

19Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane;

iwo amene ndinkawakonda andiwukira.

20Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha;

ndapulumuka lokumbakumba.

21“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni,

pakuti dzanja la Mulungu landikantha.

22Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu?

Kodi simunatope nalo thupi langa?

23“Aa, achikhala mawu anga analembedwa,

achikhala analembedwa mʼbuku,

24akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo,

akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!

25Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo,

ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.

26Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka,

mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.

27Ine ndemwe ndidzamuona Iye

ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi.

Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!

28“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji,

popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’

29Inu muyenera kuopa lupanga;

pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga;

zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”