ኢዮብ 20 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢዮብ 20:1-29

ሶፋር

1ናዕማታዊውም ሶፋር እንዲህ ሲል መለሰ፤

2“እጅግ ታውኬአለሁና፣

ሐሳቤ መልስ እንድሰጥ ይጐተጕተኛል።

3የሚያቃልለኝን ንግግር ሰምቼአለሁ፤

መልስም እሰጥ ዘንድ መንፈሴ ገፋፋኝ።

4“ሰው20፥4 ወይም አዳም ማለት ነው። በምድር ላይ ከተቀመጠ ጊዜ ጀምሮ፣

ከጥንቱ እንዴት እንደ ነበረ ታውቃለህን?

5የኀጢአተኞች መፈንጨት ለዐጭር ጊዜ፣

የክፉዎችም ደስታ ለቅጽበት መሆኑን አታውቅምን?

6እስከ ሰማይ ከፍ ከፍ ቢልም፣

ዐናቱም ደመናትን ቢነካ፣

7እንደ ኵበት ለዘላለም ይጠፋል፤

ቀድሞ ያዩትም፣ ‘የት ገባ?’ ይላሉ።

8እንደ ሕልም በርሮ ይጠፋል፤ አይገኝምም፤

እንደ ሌሊትም ራእይ በቅጽበት ያልፋል።

9ቀድሞ ያየው ዐይን ዳግመኛ አያየውም፤

የነበረበትም ቦታ ከእንግዲህ አይመለከተውም።

10ልጆቹ ለድኾች ካሳ መክፈል አለባቸው፤

እጆቹም ሀብቱን መልሰው መስጠት ይገባቸዋል።

11ዐጥንቱን የሞላው የወጣትነት ብርታት፣

ከእርሱ ጋር በዐፈር ውስጥ ይተኛል።

12“ክፋት በአፉ ውስጥ ቢጣፍጥ፣

ከምላሱም በታች ቢደብቀው፣

13አውጥቶ ለመጣል እየሳሳ፣

በአፉ ውስጥ ቢያቈየው፣

14ምግቡ በሆዱ ውስጥ ይመርራል፤

በውስጡም እንደ እባብ መርዝ ይሆናል።

15የዋጠውን ሀብት ይተፋል፤

እግዚአብሔርም መልሶ ከሆዱ ያወጣዋል።

16የእባብ መርዝ ይጠባል፤

የእፉኝትም ምላስ ይገድለዋል።

17ማርና ቅቤ በሚያፈስሱ ጅረቶች፣

በወንዞችም አይደሰትም።

18የለፋበትን ሳይበላው ይመልሳል፤

ከንግዱም ባገኘው ትርፍ አይደሰትም፤

19ድኾችን በመጨቈን ባዶ

አስቀርቷቸዋልና፣ ያልሠራውንም ቤት ነጥቋል።

20“ክፉ ምኞቱ ዕረፍት አይሰጠውም

ሀብቱም ሊያድነው አይችልም።

21ያለውን አሟጥጦ ስለሚበላ፣

ዘላቂ ብልጽግና አይኖረውም።

22በተድላ መካከል እያለ ጕስቍልና ይመጣበታል፤

በከባድ መከራም ይዋጣል።

23ሆዱን በሞላ ጊዜ፣

እግዚአብሔር የሚነድድ ቍጣውን ይሰድበታል፤

መዓቱንም ያወርድበታል።

24ከብረት መሣሪያ ቢሸሽም፣

የናስ ቀስት ይወጋዋል።

25ቀስቱን ከጀርባው፣

የሚያብለጨልጨውንም ጫፍ ከጕበቱ ይመዝዛል፤

ፍርሀትም ይይዘዋል፤

26ሀብቱ ለድቅድቅ ጨለማ ተዳርጓል፤

ሰው ባላራገበው እሳት ይበላል፤

በድንኳኑም ውስጥ የተረፈውን ይልሳል።

27ሰማያት ኀጢአቱን ይገልጡበታል፤

ምድርም ትነሣበታለች፤

28በእግዚአብሔር የቍጣ ቀን ቤቱን ጐርፍ፣

መኖሪያውንም ወራጅ ውሃ20፥28 ወይም በቤቱ ውስጥ ያለውን ንብረት ወራጅ ውሃ ይወስድበታል ማለት ነው። ይወስድበታል።

29እግዚአብሔር ለኀጢአተኞች የወሰነው ዕድል ፈንታ፣

ከአምላክም ዘንድ የተመደበላቸው ቋሚ ቅርስ ይህ ነው።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 20:1-29

Mawu a Zofari

1Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti

2“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe

chifukwa ndasautsidwa kwambiri.

3Ndikumva kudzudzula kondinyoza,

ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.

4“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale,

kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,

5kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha,

chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.

6Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba

ndipo mutu wake uli nengʼaa,

7iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe;

iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’

8Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso,

adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.

9Diso limene linamuona silidzamuonanso;

sadzapezekanso pamalo pake.

10Ana ake adzabwezera zonse

zimene iyeyo analanda anthu osauka;

11Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake

zidzagona naye limodzi mʼfumbi.

12“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake

ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,

13ngakhale salola kuzilavula,

ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,

14koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake;

chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.

15Adzachisanza chuma chimene anachimeza;

Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.

16Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo

ululu wa mphiri udzamupha.

17Sadzasangalala ndi timitsinje,

mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.

18Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya;

sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.

19Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo;

iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.

20“Chifukwa choti umbombo wake sutha,

sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.

21Palibe chatsala kuti iye adye;

chuma chake sichidzachedwa kutha.

22Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera;

mavuto aakulu adzamugwera.

23Akadya nʼkukhuta,

Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto

ngati mvula yosalekeza.

24Ngakhale athawe mkondo wachitsulo,

muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.

25Muviwo adzawutulutsira ku msana,

songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake.

Adzagwidwa ndi mantha aakulu;

26mdima wandiweyani ukudikira chuma chake.

Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza

ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.

27Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake;

dziko lapansi lidzamuwukira.

28Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake,

katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.

29Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa,

mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”