መዝሙር 97 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 97:1-12

መዝሙር 97

የእግዚአብሔር ድል አድራጊነት

1እግዚአብሔር ነገሠ፤ ምድር ደስ ይበላት፤

በሩቅ ያሉ የባሕር ጠረፎች ሐሤት ያድርጉ።

2ደመናና ጥቅጥቅ ያለ ጭጋግ በዙሪያው አለ፤

ጽድቅና ፍትሕ የዙፋኑ መሠረት ናቸው።

3እሳት በፊቱ ይሄዳል፤

በዙሪያው ያሉትንም ጠላቶቹን ይፈጃል።

4መብረቁ ዓለምን አበራ፤

ምድርም አይታ ተንቀጠቀጠች።

5ተራሮች በእግዚአብሔር ፊት፣

በምድርም ሁሉ ጌታ ፊት እንደ ሰም ቀለጡ።

6ሰማያት ጽድቁን ያውጃሉ፤

ሕዝቦችም ሁሉ ክብሩን ያያሉ።

7ለተቀረጸ ምስል የሚሰግዱ፣

በጣዖታትም የሚመኩ ሁሉ ይፈሩ፤

እናንተ አማልክት ሁሉ፤ ለእርሱ ስገዱ።

8እግዚአብሔር ሆይ፤ ስለ ፍርድህ፣

ጽዮን ሰምታ ደስ አላት፤

የይሁዳም ሴት ልጆች ሐሤት አደረጉ።

9እግዚአብሔር ሆይ፤ አንተ በምድር ሁሉ ላይ ልዑል ነህና፤

ከአማልክትም ሁሉ በላይ እጅግ ከፍ ያልህ ነህ።

10እግዚአብሔርን የምትወድዱ ክፋትን ጥሉ፤

እርሱ የታማኞቹን ነፍስ ይጠብቃልና፤

ከዐመፀኞችም እጅ ይታደጋቸዋል።

11ብርሃን ለጻድቃን፣

ሐሤትም ልባቸው ለቀና ወጣ።

12እናንት ጻድቃን በእግዚአብሔር ደስ ይበላችሁ፤

ቅዱስ ስሙንም አመስግኑ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 97:1-12

Salimo 97

1Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale;

magombe akutali akondwere.

2Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira;

chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.

3Moto umapita patsogolo pake

ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.

4Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse;

dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.

5Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova,

pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.

6Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake,

ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.

7Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi,

iwo amene amanyadira mafano;

mulambireni, inu milungu yonse!

8Ziyoni akumva ndipo akukondwera,

midzi ya Yuda ikusangalala

chifukwa cha maweruzo anu Yehova.

9Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi;

ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.

10Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa

pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira

ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa

11Kuwala kumafika pa anthu olungama,

ndi chimwemwe kwa olungama mtima.

12Kondwerani mwa Yehova Inu olungama

ndipo tamandani dzina lake loyera.