መዝሙር 96 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 96:1-13

መዝሙር 96

እግዚአብሔር፤ ንጉሥም ዳኛም

96፥1-13 ተጓ ምብ – 1ዜና 16፥23-33

1ለእግዚአብሔር አዲስ ዝማሬ ዘምሩ፤

ምድር ሁሉ፤ ለእግዚአብሔር ዘምሩ።

2ለእግዚአብሔር ዘምሩ፤ ስሙንም ባርኩ፤

ማዳኑንም ነጋ ጠባ አውሩ።

3ክብሩን በሕዝቦች መካከል፣

ድንቅ ሥራውንም በሰዎች ሁሉ ፊት ተናገሩ።

4እግዚአብሔር ታላቅ ነውና፤ ውዳሴም የሚገባው ነው፤

ከአማልክትም ሁሉ በላይ ሊፈራ ይገባዋል።

5የሕዝብ አማልክት ሁሉ ጣዖታት ናቸው፤

እግዚአብሔር ግን ሰማያትን ሠራ።

6ክብርና ግርማ በፊቱ ናቸው፤

ብርታትና ውበትም በመቅደሱ ውስጥ አሉ።

7የሕዝቦች ወገኖች ሆይ፤ ለእግዚአብሔር ስጡ፤

ክብርንና ብርታትን ለእግዚአብሔር ስጡ።

8ለስሙ የሚገባ ክብርን ለእግዚአብሔር ስጡ፤

ቍርባንን ይዛችሁ ወደ አደባባዩ ግቡ።

9በተቀደሰ ውበት ለእግዚአብሔር ስገዱ፤

ምድር ሁሉ፤ በፊቱ ተንቀጥቀጡ።

10በሕዝቦች መካከል፣ “እግዚአብሔር ነገሠ” በሉ፤

ዓለም በጽኑ ተመሥርታለች፤ አትናወጥም፤

እርሱ ለሕዝቦች በእኩልነት ይፈርዳል።

11ሰማያት ደስ ይበላቸው፤ ምድርም ሐሤት ታድርግ፤

ባሕርና በውስጧ ያለው ሁሉ ያስተጋባ፤

12መስኩና በላዩ ያለው ሁሉ ይፈንጥዝ፤

ያን ጊዜ የዱር ዛፎች ሁሉ በደስታ ይዘምራሉ፤

13እርሱ ይመጣልና በእግዚአብሔር ፊት ይዘምራሉ፤

በምድር ላይ ሊፈርድ ይመጣል፤

በዓለም ላይ በጽድቅ፣

በሕዝቦችም ላይ በእውነት ይበይናል።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 96:1-13

Salimo 96

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;

Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.

2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,

ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.

5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,

koma Yehova analenga mayiko akumwamba.

6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,

mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;

bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.

9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;

njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”

Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;

Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.

11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;

nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.

Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;

13idzayimba pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lonse mwachilungamo

ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.