መዝሙር 128 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 128:1-6

መዝሙር 128

የጻድቃን በረከት

መዝሙረ መዓርግ።

1እግዚአብሔርን የሚፈሩ ሁሉ፣

በመንገዱም የሚሄዱ የተባረኩ ናቸው።

2የድካምህን ፍሬ ትበላለህ፤

ትባረካለህ፤ ይሳካልሃልም።

3ሚስትህ በቤትህ፣

እንደሚያፈራ ወይን ናት፤

ወንዶች ልጆችህ በማእድህ ዙሪያ፣

እንደ ወይራ ተክል ናቸው።

4እነሆ፤ እግዚአብሔርን የሚፈራ ሰው፣

እንዲህ ይባረካል።

5እግዚአብሔር ከጽዮን ይባርክህ፤

በሕይወትህ ዘመን ሁሉ፣ የኢየሩሳሌምን ብልጽግና ያሳይህ፤

6የልጅ ልጅ ለማየትም ያብቃህ።

በእስራኤል ላይ ሰላም ይውረድ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 128:1-6

Salimo 128

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Odala ndi onse amene amaopa Yehova,

amene amayenda mʼnjira zake.

2Udzadya chipatso cha ntchito yako;

madalitso ndi chuma zidzakhala zako.

3Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka

mʼkati mwa nyumba yako;

ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi

kuzungulira tebulo lako.

4Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa

amene amaopa Yehova.

5Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni

masiku onse a moyo wako;

uwone zokoma za Yerusalemu,

6ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israeli.