Yobu 19 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Yobu 19:1-29

Yobu Amuddamu

1Awo Yobu n’addamu nti:

2“Mulikomya ddi okunnyigiriza

ne mummenya n’ebigambo?

3Emirundi kkumi nga munvuma;

temukwatiddwa nsonyi kunnumba.

419:4 Yob 6:24Bwe kiba nga kituufu nti nawaba,

obukyamu bwange, bwange nzekka.

519:5 Zab 35:26; 38:16; 55:12Bwe muba munneegulumiririzaako

ne mukozesa obulumi bwange okunfeebya,

619:6 a Yob 27:2 b Yob 18:8mumanye nga Katonda ankoze bubi

era anzingizza mu kitimba kye.

719:7 a Yob 30:20 b Yob 9:24; Kbk 1:2-4“Wadde nga nkaaba nti, ‘Mpisiddwa bubi,’ siddibwamu;

ne bwe nkuba enduulu, tewali antaasa.

819:8 a Yob 3:23; Kgb 3:7 b Yob 30:26Azibye ekkubo lyange sisobola kuyita;

amakubo gange agalese mu kizikiza.

919:9 a Yob 12:17 b Zab 89:39, 44; Kgb 5:16Anziggyeeko ekitiibwa kyange

n’anziggyako n’engule ku mutwe gwange.

1019:10 a Yob 12:14 b Yob 7:6 c Yob 24:20Anjuzaayuza ku buli ludda okutuusa lwe watasigalawo kantu,

asigula essuubi lyange ng’omuti.

1119:11 a Yob 16:9 b Yob 13:24Obusungu bwe bumbubuukirako;

ambala ng’omu ku balabe be.

1219:12 a Yob 16:13 b Yob 30:12Amaggye ge galumba n’amaanyi;

ganzimbako enkomera

ne gagumba okwetooloola weema yange.

1319:13 a Zab 69:8 b Yob 16:7; Zab 88:8“Anziggyeeko baganda bange;

abo bwe twali tumanyiganye banviiriddeko ddala.

14Ab’ekika kyange banviiriddeko ddala,

mikwano gyange ginneerabidde.

15Abagenyi bange n’abaweereza bange abawala, bampisa nga gwe batamanyi,

ne bandaba nga munnagwanga.

16Mpita omuddu wange naye tawulira,

wadde nga mwegayirira n’akamwa kange.

17Omukka gwange gwe nzisa, guwunyira bubi mukyala wange;

nakyayibwa baganda bange bennyini.

1819:18 2Bk 2:23N’obulenzi obuto bunsekerera;

buli lwe bundaba bunvuma.

1919:19 a Zab 55:12-13 b Zab 38:11Mikwano gyange gyonna enfirabulago gya nkyawa;

abo be nnayagalanga banneefuukira.

2019:20 Yob 33:21; Zab 102:5Siriiko bwe ndi wabula ndi ddiba na magumba:

nsigazzaawo bibuno byokka.

21“Munkwatirwe ekisa mikwano gyange, munkwatirwe ekisa,

kubanga omukono gwa Katonda gunkubye.

2219:22 a Yob 13:25; 16:11 b Zab 69:26Lwaki munjigga nga Katonda bw’anjigga?

Omubiri gwe mufunye tegumala?

2319:23 Is 30:8“Singa nno ebigambo byange byawandiikibwa,

Singa byawandiikibwa ku muzingo, bandiguwadde ani?

24Singa byawandiikibwa n’ekyuma ku lubaati,

oba okuwandiikibwa ku lwazi ne bibeerawo emirembe n’emirembe!

2519:25 a Zab 78:35; Nge 23:11; Is 43:14; Yer 50:34 b Yob 16:19Mmanyi nga Omununuzi wange mulamu,

era nga ku nkomerero aliyimirira ku nsi.

2619:26 Zab 17:15; Mat 5:8; 1Ko 13:12; 1Yk 3:2Era ng’olususu lwange bwe luweddewo,

kyokka mu mubiri gwange ndiraba Katonda;

2719:27 Zab 73:26nze mwene ndimulaba,

n’amaaso gange, Nze, so si mulala.

Emmeeme yange ng’eyaayaana munda mu nze!

28“Bwe mugamba nti, ‘Tujja kumuyigganya,

kubanga ensibuko y’emitawaana eri mu ye;’

2919:29 a Yob 15:22 b Yob 22:4; Zab 1:5; 9:7nammwe bennyini musaana mutye ekitala.

Kubanga obusungu buleeta okubonereza okw’ekitala,

olwo mulyoke mumanye ng’eriyo okusalirwa omusango.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 19:1-29

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti,

ndi kundilasa ndi mawu anuwo?

3Inuyo mwandinyoza kwambiri;

mwanditsutsa mopanda manyazi.

4Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera,

cholakwachotu nʼchanga.

5Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga,

ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,

6pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira

ndipo wandizinga ukonde wake.

7“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha;

ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.

8Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa;

waphimba njira zanga ndi mdima.

9Iye wandilanda ulemu wanga

ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.

10Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu;

Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.

11Wandikwiyira ndipo

akundiyesa mmodzi mwa adani ake.

12Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu,

akonzekera zodzalimbana nane

ndipo azungulira nyumba yanga.

13“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga;

wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.

14Abale anga andithawa;

abwenzi anga andiyiwala.

15Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo;

ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.

16Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha,

ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.

17Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga;

ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.

18Inde, ngakhale ana amandinyoza;

akandiona amandinyodola.

19Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane;

iwo amene ndinkawakonda andiwukira.

20Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha;

ndapulumuka lokumbakumba.

21“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni,

pakuti dzanja la Mulungu landikantha.

22Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu?

Kodi simunatope nalo thupi langa?

23“Aa, achikhala mawu anga analembedwa,

achikhala analembedwa mʼbuku,

24akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo,

akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!

25Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo,

ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.

26Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka,

mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.

27Ine ndemwe ndidzamuona Iye

ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi.

Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!

28“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji,

popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’

29Inu muyenera kuopa lupanga;

pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga;

zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”