Yobu 17 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Yobu 17:1-16

117:1 Zab 88:3-4Omutima gwange gwennyise,

ennaku zange zisalibbwaako,

entaana enninze.

217:2 1Sa 1:6-7Ddala abansekerera bannetoolodde;

amaaso gange gabeekengera.

317:3 a Zab 119:122 b Nge 6:1 c Is 38:14“Ompe, Ayi Katonda akakalu k’onsaba.

Ani omulala ayinza okunneeyimirira?

4Ozibye emitima gyabwe obutategeera;

noolwekyo toobakkirize kuwangula.

517:5 Yob 11:20Omusajja avumirira mikwano gye olw’empeera

alireetera amaaso g’abaana be okuziba.

617:6 Yob 30:9“Katonda anfudde ekisekererwa eri buli omu,

anfudde buli omu gw’afujjira amalusu mu maaso.

717:7 Yob 16:8Amaaso gange gayimbadde olw’okunakuwala;

omubiri gwange gwonna kaakano guli nga kisiikirize.

817:8 Yob 22:19Abantu ab’amazima beesisiwala olwa kino;

atalina musango agolokokedde ku oyo atatya Katonda.

917:9 a Nge 4:18 b Yob 22:30Naye era abatuukirivu banaakwatanga amakubo gaabwe,

n’abo ab’emikono emirongoofu baneeyongeranga amaanyi.

1017:10 Yob 12:2“Naye mukomeewo mwenna kaakano, mujje,

naye siraba muntu mugezi mu mmwe!

1117:11 Yob 7:6Ennaku zange ziyise entegeka zange zoonoonese,

era bwe kityo n’okwegomba kw’omutima gwange.

12Abantu bano ekiro bakifuula emisana;

mu kizikiza mwennyini mwe bagambira nti, Ekitangaala kinaatera okujja.

1317:13 Yob 3:13Amagombe bwe gaba nga ge maka mwe nnina essuubi,

bwe njala obuliri bwange mu kizikiza,

1417:14 a Yob 13:28; 30:28, 30; Zab 16:10 b Yob 21:26ne ŋŋamba amagombe nti, ‘Ggwe kitange,’

era n’eri envunyu nti, ‘Ggwe mmange,’ oba nti, ‘Ggwe mwannyinaze,’

1517:15 Yob 7:6kale essuubi lyange liba ludda wa?

Ani ayinza okuliraba?

1617:16 Yob 3:17-19; Yon 2:6Nalyo lirigenda eri enzigi z’emagombe

Oba tuligenda ffenna mu nfuufu?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 17:1-16

1“Mtima wanga wasweka,

masiku anga atha,

manda akundidikira.

2Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira;

maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.

3“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna.

Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?

4Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu;

choncho simudzawalola kuti apambane.

5Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma,

ana ake sadzaona mwayi.

6“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense,

munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.

7Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni;

ndawonda ndi mutu womwe.

8Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi;

anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.

9Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo,

ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.

10“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo,

sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.

11Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka,

pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.

12Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana,

nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’

13Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda,

ngati ndiyala bedi langa mu mdima,

14ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’

ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’

15tsono chiyembekezo changa chili kuti?

Ndani angaone populumukira panga?

16Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse,

polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.”