詩篇 54 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

詩篇 54:1-7

54

ジフの人々によって、あわやサウル王に売り渡されそうになった時のダビデの詩。

1ああ神よ。

大いなる力をふるって私をお救いください。

力強い腕で守ってください。

2どうか、この祈りを聞き届けてくださいますように。

3暴虐を働く者どもが、いどみかかってきます。

神のことなど気にもかけない冷酷な者たちが、

このいのちをつけねらっています。

4しかし、神は助けてくださいます。

私の友なのですから。

5敵の悪らつな仕打ちは、その頭上に戻って来ます。

ああ神よ。お約束どおりに事を運び、

悪人どもの息の根を止めてください。

6主よ。私はあなたに心からのいけにえをささげ、

御名をほめたたえます。

それこそ道理にかなったことです。

7神はすべての苦しみから私を救い出し、

敵を蹴散らしてくださいます。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 54:1-7

Salimo 54

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

1Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;

onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.

2Imvani pemphero langa, Inu Mulungu

mvetserani mawu a pakamwa panga.

3Alendo akundithira nkhondo;

anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,

anthu amene salabadira za Mulungu.

4Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;

Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

5Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;

mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

6Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;

ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,

pakuti ndi labwino.

7Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,

ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.