詩篇 52 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

詩篇 52:1-9

52

ダビデが、その敵ドエグ(Ⅰサムエル22章参照)に抗議して書いたもの。ドエグは、のちに八十五人の祭司とその家族を虐殺した。

1おまえは英雄のつもりでいるのか。

神の民に加えたこの暴虐を誇っているのか。

2おまえは策略を謀ることにかけては天才だ。

3どうしてそれほど、善より悪が、

真実よりうそが好きなのか。

4相手を中傷するのに目がなく、

でたらめを並べ立てては、平気で人を傷つける者よ。

5神はおまえを激しく打ち倒し、

死人の国へ引きずって行かれる。

6それを見て、神に従う人々は恐れを感じるが、

まもなく笑ってこう言うだろう。

7「あれが、神をあなどり、富に望みを置き、

ますます大胆に悪事を働いた者の末路だ。」

8一方、この私は、主に守られている

囲いの中のオリーブのようで、

いつまでも主のあわれみにすがる。

9ああ主よ。

あなたの懲らしめがどんなものかを知った私は、

永久にあなたをほめたたえて、

そのあわれみを待ち望みます。

あなたがどんなにいつくしみ深い神であるか、

知らない者などいないのですから。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 52:1-9

Salimo 52

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”

1Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?

Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,

iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?

2Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;

lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,

ntchito yako nʼkunyenga.

3Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.

Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.

Sela

4Umakonda mawu onse opweteka,

iwe lilime lachinyengo!

5Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:

iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;

iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.

6Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;

adzamuseka nʼkumanena kuti,

7“Pano tsopano pali munthu

amene sanayese Mulungu linga lake,

koma anakhulupirira chuma chake chambiri

nalimbika kuchita zoyipa!”

8Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi

wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;

ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu

kwa nthawi za nthawi.

9Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;

chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera

pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.