詩篇 4 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

詩篇 4:1-8

4

1ああ神よ。

あなたは私を、御目にかなった完全な者だと

言ってくださいました。

私が苦しんでいるとき、

いつも気にかけてくださいました。

今また、私はあなたを呼び求めます。

どうか答えてください。

私をあわれみ、私の祈りを聞いてください。

2主は問われます。

「人の子らよ、こんな空しい偶像を拝んで、

いつまでわたしの栄光をはずかしめるのか。

偶像が神であるはずなどないのに。」

3人の子らよ、よく心に留めておきなさい。

主は救われた人々を、ご自分のためにえり分けました。

だから、私の声に耳を傾けて、

答えてくださるのです。

4恐れかしこんで、主の前に立ちなさい。

主に対して罪を犯してはいけません。

寝床で、静かに思い巡らしなさい。

5主に信頼し、主に喜ばれる供え物をささげなさい。

6神が助けるはずはないと、だれもが言っています。

ああ主よ、御顔の光で私たちを照らし出し、

彼らが誤っていることを実証してください。

7あなたから頂いた喜びは、

刈り入れ時に人々が穀物の山を眺めて喜ぶよりも、

はるかにまさっています。

8私は安心して横になり、眠りにつきます。

たとえひとりぼっちでも、

ああ主よ、あなたはすべての危険から

守ってくださるのです。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 4:1-8

Salimo 4

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide.

1Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu,

Inu Mulungu wa chilungamo changa.

Pumulitseni ku zowawa zanga;

chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.

2Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi?

Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza?

Sela.

3Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika;

Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.

4Kwiyani koma musachimwe;

pamene muli pa mabedi anu,

santhulani mitima yanu ndi kukhala chete.

Sela

5Perekani nsembe zolungama

ndipo dalirani Yehova.

6Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?”

Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.

7Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu

kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.

8Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere,

pakuti Inu nokha, Inu Yehova,

mumandisamalira bwino.