詩篇 111 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

詩篇 111:1-10

111

1-2ハレルヤ。

私がどれほど主に感謝しているか、

人々に知ってほしいと思います。

感謝を忘れない人たちよ、

さあいっしょに、主のなさった数々の奇跡を

思い巡らしましょう。

3この奇跡こそ、神の栄誉と威厳、

そして永遠の恵みを物語るものです。

4だれが、主のあわれみと恵みを簡単に忘れるでしょう。

5主はご自分に信頼を寄せる人に食物を与え、

決して約束を破棄なさいません。

6神はご自分の民を大きな力で支え、

多くの民族が住んでいた、

イスラエルの地をお与えになりました。

7神のなさることはみな正しく、

そのおきてはどれ一つ取っても誤りがありません。

8神のおきては真理と恵みで成り立っていて、

永遠に続きます。

9主に身の代金を払っていただいた民は、

今や自由に神の前に出入りできるのです。

10人はどうすれば知恵をみがけるでしょうか。

それには、主を信じて従うことです。

神のおきてを守ってこそ、賢くなれるのです。

神を永遠にほめたたえましょう。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 111:1-10

Salimo 111

1Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse

mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;

onse amene amakondwera nazo amazilingalira.

3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.

5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;

amakumbukira pangano lake kwamuyaya.

6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,

kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.

7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;

malangizo ake onse ndi odalirika.

8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,

ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.

9Iyeyo amawombola anthu ake;

anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya

dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;

onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.

Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.