ヨブ 記 18 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

ヨブ 記 18:1-21

18

ビルダデのことば

1シュアハ人ビルダデの二度目の返答。

2「気でもおかしくなったのか。

助言してほしいのなら、

少しは筋の通ったことを言うことだ。

3それではまるで、

私たちが、愚かで物言わぬ獣みたいではないか。

4あなたが怒って着物を裂いただけで、

地震が起こったり、

岩が動いて移ったりするとでも思っているのか。

5物事がうまくいかないとしたら、

それはあなたが罪深かったからだ。

炎が消えて当然だ。

6悪の居座る家には暗闇がつきものなのだから。

7罪深い悪者は肩で風を切って歩くが、

急に足もとが危うくなり、

全身の力が抜けていくのがわかる。

8-9彼は落とし穴に落ち、

待ち伏せしていた追いはぎの餌食になる。

10どこを通っても、罠がしかけられている。

11敵が、すぐあとをつけているのだから、

彼が怖がるのもむりはない。

12飢えのために消耗しきった彼を、

災難が待ちかまえている。

13病気が皮膚をむしばみ、死が彼をむさぼり食う。

14日ごろ頼りにしていた富にもそっぽを向かれ、

恐怖の王のもとへ引き立てられる。

15家も、燃える硫黄の集中攻撃を浴びて姿をかき消す。

16彼は根元から枯れ、枝は一本残らず切り取られる。

17彼の記憶は地上から一掃され、

彼を覚えている者は一人もいなくなる。

18彼は光の国から闇の国へと追いやられ、

この世から立ち退くよう命じられる。

19子も孫も親類縁者もいなくなる。

20老人も若者も、彼の運命を知っておびえる。

21これが、神を信じない罪人の行き着く先だ。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 18:1-21

Mawu a Bilidadi

1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

2“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi?

Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.

3Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe

ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?

4Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako,

kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo?

Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?

5“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa;

malawi a moto wake sakuwalanso.

6Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima;

nyale ya pambali pake yazima.

7Mayendedwe ake amgugu azilala;

fundo zake zomwe zamugwetsa.

8Mapazi ake amulowetsa mu ukonde

ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.

9Msampha wamkola mwendo;

khwekhwe lamugwiritsitsa.

10Amutchera msampha pansi mobisika;

atchera diwa pa njira yake.

11Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse,

zikutsatira mayendedwe ake onse.

12Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala,

tsoka likumudikira.

13Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse;

miyendo yake, manja ake, zonse zawola.

14Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira,

ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.

15Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo;

awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.

16Mizu yake ikuwuma pansi

ndipo nthambi zake zikufota

17Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi;

sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.

18Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima,

ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.

19Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake,

kulibe wotsala kumene iye ankakhala.

20Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake;

anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.

21Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa;

amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”