Zefaniya 3 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 3:1-20

Tsogolo la Yerusalemu

1Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,

owukira ndi odetsedwa!

2Sumvera aliyense,

sulandira chidzudzulo.

Sumadalira Yehova,

suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.

3Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,

olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,

zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.

4Aneneri ake ndi odzikuza;

anthu achinyengo.

Ansembe ake amadetsa malo opatulika

ndipo amaphwanya lamulo.

5Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;

Iye salakwa.

Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,

ndipo tsiku lililonse salephera,

komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.

6“Ndachotseratu mitundu ya anthu;

ndagwetsa malinga awo.

Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,

popanda aliyense wodutsa.

Mizinda yawo yawonongedwa;

palibe aliyense adzatsalemo.

7Ndinati,

‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa

ndi kumvera kudzudzula kwanga!’

Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,

kapena kuwalanganso.

Koma iwo anali okonzeka

kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.

8Choncho mundidikire,” akutero Yehova,

“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.

Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,

kusonkhanitsa maufumu

ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;

mkwiyo wanga wonse woopsa.

Dziko lonse lidzatenthedwa

ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

9“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse

kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova

ndi kumutumikira Iye pamodzi.

10Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi

anthu anga ondipembedza, omwazikana,

adzandibweretsera zopereka.

11Tsiku limenelo simudzachita manyazi

chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,

popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu

amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.

Simudzakhalanso odzikuza

mʼphiri langa lopatulika.

12Koma ndidzasiya pakati panu

anthu ofatsa ndi odzichepetsa,

amene amadalira dzina la Yehova.

13Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;

sadzayankhulanso zonama,

ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.

Adzadya ndi kugona

ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;

fuwula mokweza, iwe Israeli!

Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!

15Yehova wachotsa chilango chako,

wabweza mdani wako.

Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;

sudzaopanso chilichonse.

16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,

“Usaope, iwe Ziyoni;

usafowoke.

17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,

ali ndi mphamvu yopulumutsa.

Adzakondwera kwambiri mwa iwe,

adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,

adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18“Ndidzakuchotserani zowawa

za pa zikondwerero zoyikika;

nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.

19Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi

onse amene anakuponderezani;

ndidzapulumutsa olumala

ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.

Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu

mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.

20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;

pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.

Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu

pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi

pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu

inu mukuona,”

akutero Yehova.

Nova Versão Internacional

Sofonias 3:1-20

O Futuro de Jerusalém

1Ai da cidade rebelde,

impura e opressora!

2Não ouve ninguém,

e não aceita correção.

Não confia no Senhor,

não se aproxima do seu Deus.

3No meio dela os seus líderes

são leões que rugem.

Seus juízes são lobos vespertinos

que nada deixam para a manhã seguinte.

4Seus profetas são irresponsáveis,

são homens traiçoeiros.

Seus sacerdotes profanam o santuário

e fazem violência à lei.

5No meio dela está o Senhor,

que é justo e jamais comete injustiça.

A cada manhã ele ministra a sua justiça,

e a cada novo dia ele não falha,

mas o injusto não se envergonha da sua injustiça.

6“Eliminei nações;

suas fortificações estão devastadas.

Deixei desertas as suas ruas.

Suas cidades estão destruídas;

ninguém foi deixado; ninguém!

7Eu disse à cidade:

Com certeza você me temerá e aceitará correção!

Pois, então, a sua habitação não seria eliminada,

nem cairiam sobre ela todos os meus castigos.

Mas eles ainda estavam ávidos

por fazer todo tipo de maldade.

8Por isso, esperem por mim”,

declara o Senhor,

“no dia em que eu me levantar para testemunhar.

Decidi ajuntar as nações, reunir os reinos

e derramar a minha ira sobre eles,

toda a minha impetuosa indignação.

O mundo inteiro será consumido

pelo fogo da minha zelosa ira.

9“Então purificarei os lábios dos povos,

para que todos eles invoquem o nome do Senhor

e o sirvam de comum acordo.

10Desde além dos rios da Etiópia

os meus adoradores, o meu povo disperso,

me trarão ofertas.

11Naquele dia, vocês não serão envergonhados

pelos seus atos de rebelião,

porque retirarei desta cidade

os que se regozijam em seu orgulho.

Nunca mais vocês serão altivos

no meu santo monte.

12Mas deixarei no meio da cidade

os mansos e humildes,

que se refugiarão no nome do Senhor.

13O remanescente de Israel não cometerá injustiças;

eles não mentirão,

nem se achará engano em suas bocas.

Eles se alimentarão e descansarão,

sem que ninguém os amedronte.”

14Cante, ó cidade3.14 Hebraico: filha. de Sião;

exulte, ó Israel!

Alegre-se, regozije-se de todo o coração,

ó cidade de Jerusalém!

15O Senhor anulou a sentença contra você,

ele fez retroceder os seus inimigos.

O Senhor, o Rei de Israel, está em seu meio;

nunca mais você temerá perigo algum.

16Naquele dia, dirão a Jerusalém:

“Não tema, ó Sião;

não deixe suas mãos enfraquecerem.

17O Senhor, o seu Deus, está em seu meio,

poderoso para salvar.

Ele se regozijará em você;

com o seu amor a renovará3.17 Ou a tranquilizará,

ele se regozijará em você

com brados de alegria”.

18“Eu ajuntarei os que choram pelas festas fixas,

os que se afastaram de vocês,

para que isso não mais pese como vergonha para vocês.

19Nessa época, agirei contra todos os que oprimiram vocês;

salvarei os aleijados e ajuntarei os dispersos.

Darei a eles louvor e honra em todas as terras

onde foram envergonhados.

20Naquele tempo, eu ajuntarei vocês;

naquele tempo, os trarei para casa.

Eu darei a vocês honra e louvor

entre todos os povos da terra,

quando eu restaurar a sua sorte3.20 Ou eu os trouxer de volta

diante dos seus próprios olhos”,

diz o Senhor.