Zefaniya 2 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 2:1-15

1Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,

inu mtundu wochititsa manyazi,

2isanafike nthawi yachiweruzo,

nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,

usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,

tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.

3Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,

inu amene mumachita zimene amakulamulani.

Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;

mwina mudzatetezedwa

pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.

Za Afilisti

4Gaza adzasiyidwa

ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.

Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu

ndipo Ekroni adzazulidwa.

5Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,

inu mtundu wa Akereti;

mawu a Yehova akutsutsa

iwe Kanaani, dziko la Afilisti.

“Ndidzakuwononga

ndipo palibe amene adzatsale.”

6Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,

lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.

7Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;

adzapezako msipu.

Nthawi ya madzulo adzagona

mʼnyumba za Asikeloni.

Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;

adzabwezeretsa mtendere wawo.

Za Mowabu ndi Amoni

8“Ndamva kunyoza kwa Mowabu

ndi chipongwe cha Amoni,

amene ananyoza anthu anga

ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.

9Choncho, pali Ine Wamoyo,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,

“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,

Amoni adzasanduka ngati Gomora;

malo a zomeramera ndi maenje a mchere,

dziko la bwinja mpaka muyaya.

Anthu anga otsala adzawafunkha;

opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”

10Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,

chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.

11Yehova adzawachititsa mantha kwambiri

pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.

Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,

uliwonse ku dziko la kwawo.

Za Kusi

12“Inunso anthu a ku Kusi,

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Za Asiriya

13Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto

ndi kuwononga Asiriya,

kusiya Ninive atawonongekeratu

ndi owuma ngati chipululu.

14Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,

pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.

Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu

adzakhala pa nsanamira zake.

Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,

mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,

nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.

15Umenewu ndiye mzinda wosasamala

umene kale unali wotetezedwa.

Unkanena kuti mu mtima mwake,

“Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”

Taonani lero wasanduka bwinja,

kokhala nyama zakutchire!

Onse owudutsa akuwunyoza

ndi kupukusa mitu yawo.

Nova Versão Internacional

Sofonias 2:1-15

1Reúna-se e ajunte-se,

nação sem pudor,

2antes que chegue o tempo determinado

e aquele dia passe como a palha,

antes que venha sobre vocês a ira impetuosa do Senhor,

antes que o dia da ira do Senhor os alcance.

3Busquem o Senhor, todos vocês, os humildes da terra,

vocês que fazem o que ele ordena.

Busquem a justiça, busquem a humildade;

talvez vocês tenham abrigo no dia da ira do Senhor.

O Castigo da Filístia

4Gaza será abandonada,

e Ascalom ficará arruinada.

Ao meio-dia Asdode será banida,

e Ecrom será desarraigada.

5Ai de vocês que vivem junto ao mar,

nação dos queretitas;

a palavra do Senhor está contra você,

ó Canaã, terra dos filisteus.

“Eu a destruirei,

e não sobrará ninguém.”

6Essa terra junto ao mar,

onde habitam os queretitas,

será morada de pastores

e curral de ovelhas.

7Pertencerá ao remanescente da tribo de Judá.

Ali encontrarão pastagem;

e, ao entardecer, eles se deitarão

nas casas de Ascalom.

O Senhor, o seu Deus, cuidará deles,

e lhes restaurará a sorte2.7 Ou trará de volta seus cativos.

O Castigo de Moabe e de Amom

8“Ouvi os insultos de Moabe

e as zombarias dos amonitas,

que insultaram o meu povo

e fizeram ameaças contra o seu território.

9Por isso, juro pela minha vida”,

declara o Senhor dos Exércitos,

o Deus de Israel,

“Moabe se tornará como Sodoma

e os amonitas como Gomorra:

um lugar tomado por ervas daninhas e poços de sal,

uma desolação perpétua.

O remanescente do meu povo os saqueará;

os sobreviventes da minha nação herdarão a terra deles.”

10É isso que eles receberão

como recompensa pelo seu orgulho,

por insultarem e ridicularizarem

o povo do Senhor dos Exércitos.

11O Senhor será terrível contra eles

quando destruir todos os deuses da terra.

As nações de todo o mundo o adorarão,

cada uma em sua própria terra.

O Castigo da Etiópia

12“Vocês também, ó etíopes,2.12 Hebraico: cuxitas

serão mortos pela minha espada.”

O Castigo da Assíria

13Ele estenderá a mão contra o norte

e destruirá a Assíria,

deixando Nínive totalmente em ruínas,

tão seca como o deserto.

14No meio dela se deitarão rebanhos

e todo tipo de animais selvagens.

Até a coruja-do-deserto e o mocho

se empoleirarão no topo de suas colunas.

Seus gritos ecoarão pelas janelas.

Haverá entulho nas entradas,

e as vigas de cedro ficarão expostas.

15Essa é a cidade que exultava,

vivendo despreocupada,

e dizia para si mesma:

“Eu, e mais ninguém!”

Que ruínas sobraram!

Uma toca de animais selvagens!

Todos os que passam por ela zombam

e sacodem os punhos.