1Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,
inu mtundu wochititsa manyazi,
2isanafike nthawi yachiweruzo,
nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,
usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,
tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
3Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,
inu amene mumachita zimene amakulamulani.
Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;
mwina mudzatetezedwa
pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.
Za Afilisti
4Gaza adzasiyidwa
ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.
Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu
ndipo Ekroni adzazulidwa.
5Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,
inu mtundu wa Akereti;
mawu a Yehova akutsutsa
iwe Kanaani, dziko la Afilisti.
“Ndidzakuwononga
ndipo palibe amene adzatsale.”
6Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,
lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
7Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;
adzapezako msipu.
Nthawi ya madzulo adzagona
mʼnyumba za Asikeloni.
Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;
adzabwezeretsa mtendere wawo.
Za Mowabu ndi Amoni
8“Ndamva kunyoza kwa Mowabu
ndi chipongwe cha Amoni,
amene ananyoza anthu anga
ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
9Choncho, pali Ine Wamoyo,”
akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,
Amoni adzasanduka ngati Gomora;
malo a zomeramera ndi maenje a mchere,
dziko la bwinja mpaka muyaya.
Anthu anga otsala adzawafunkha;
opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”
10Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,
chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
11Yehova adzawachititsa mantha kwambiri
pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.
Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,
uliwonse ku dziko la kwawo.
Za Kusi
12“Inunso anthu a ku Kusi,
mudzaphedwa ndi lupanga.”
Za Asiriya
13Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto
ndi kuwononga Asiriya,
kusiya Ninive atawonongekeratu
ndi owuma ngati chipululu.
14Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,
pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.
Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu
adzakhala pa nsanamira zake.
Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,
mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,
nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
15Umenewu ndiye mzinda wosasamala
umene kale unali wotetezedwa.
Unkanena kuti mu mtima mwake,
“Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”
Taonani lero wasanduka bwinja,
kokhala nyama zakutchire!
Onse owudutsa akuwunyoza
ndi kupukusa mitu yawo.
1Reúna-se e ajunte-se,
nação sem pudor,
2antes que chegue o tempo determinado
e aquele dia passe como a palha,
antes que venha sobre vocês a ira impetuosa do Senhor,
antes que o dia da ira do Senhor os alcance.
3Busquem o Senhor, todos vocês, os humildes da terra,
vocês que fazem o que ele ordena.
Busquem a justiça, busquem a humildade;
talvez vocês tenham abrigo no dia da ira do Senhor.
O Castigo da Filístia
4Gaza será abandonada,
e Ascalom ficará arruinada.
Ao meio-dia Asdode será banida,
e Ecrom será desarraigada.
5Ai de vocês que vivem junto ao mar,
nação dos queretitas;
a palavra do Senhor está contra você,
ó Canaã, terra dos filisteus.
“Eu a destruirei,
e não sobrará ninguém.”
6Essa terra junto ao mar,
onde habitam os queretitas,
será morada de pastores
e curral de ovelhas.
7Pertencerá ao remanescente da tribo de Judá.
Ali encontrarão pastagem;
e, ao entardecer, eles se deitarão
nas casas de Ascalom.
O Senhor, o seu Deus, cuidará deles,
e lhes restaurará a sorte2.7 Ou trará de volta seus cativos.
O Castigo de Moabe e de Amom
8“Ouvi os insultos de Moabe
e as zombarias dos amonitas,
que insultaram o meu povo
e fizeram ameaças contra o seu território.
9Por isso, juro pela minha vida”,
declara o Senhor dos Exércitos,
o Deus de Israel,
“Moabe se tornará como Sodoma
e os amonitas como Gomorra:
um lugar tomado por ervas daninhas e poços de sal,
uma desolação perpétua.
O remanescente do meu povo os saqueará;
os sobreviventes da minha nação herdarão a terra deles.”
10É isso que eles receberão
como recompensa pelo seu orgulho,
por insultarem e ridicularizarem
o povo do Senhor dos Exércitos.
11O Senhor será terrível contra eles
quando destruir todos os deuses da terra.
As nações de todo o mundo o adorarão,
cada uma em sua própria terra.
O Castigo da Etiópia
12“Vocês também, ó etíopes,2.12 Hebraico: cuxitas
serão mortos pela minha espada.”
O Castigo da Assíria
13Ele estenderá a mão contra o norte
e destruirá a Assíria,
deixando Nínive totalmente em ruínas,
tão seca como o deserto.
14No meio dela se deitarão rebanhos
e todo tipo de animais selvagens.
Até a coruja-do-deserto e o mocho
se empoleirarão no topo de suas colunas.
Seus gritos ecoarão pelas janelas.
Haverá entulho nas entradas,
e as vigas de cedro ficarão expostas.
15Essa é a cidade que exultava,
vivendo despreocupada,
e dizia para si mesma:
“Eu, e mais ninguém!”
Que ruínas sobraram!
Uma toca de animais selvagens!
Todos os que passam por ela zombam
e sacodem os punhos.