Zefaniya 3 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 3:1-20

Tsogolo la Yerusalemu

1Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,

owukira ndi odetsedwa!

2Sumvera aliyense,

sulandira chidzudzulo.

Sumadalira Yehova,

suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.

3Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,

olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,

zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.

4Aneneri ake ndi odzikuza;

anthu achinyengo.

Ansembe ake amadetsa malo opatulika

ndipo amaphwanya lamulo.

5Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;

Iye salakwa.

Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,

ndipo tsiku lililonse salephera,

komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.

6“Ndachotseratu mitundu ya anthu;

ndagwetsa malinga awo.

Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,

popanda aliyense wodutsa.

Mizinda yawo yawonongedwa;

palibe aliyense adzatsalemo.

7Ndinati,

‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa

ndi kumvera kudzudzula kwanga!’

Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,

kapena kuwalanganso.

Koma iwo anali okonzeka

kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.

8Choncho mundidikire,” akutero Yehova,

“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.

Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,

kusonkhanitsa maufumu

ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;

mkwiyo wanga wonse woopsa.

Dziko lonse lidzatenthedwa

ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

9“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse

kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova

ndi kumutumikira Iye pamodzi.

10Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi

anthu anga ondipembedza, omwazikana,

adzandibweretsera zopereka.

11Tsiku limenelo simudzachita manyazi

chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,

popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu

amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.

Simudzakhalanso odzikuza

mʼphiri langa lopatulika.

12Koma ndidzasiya pakati panu

anthu ofatsa ndi odzichepetsa,

amene amadalira dzina la Yehova.

13Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;

sadzayankhulanso zonama,

ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.

Adzadya ndi kugona

ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;

fuwula mokweza, iwe Israeli!

Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!

15Yehova wachotsa chilango chako,

wabweza mdani wako.

Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;

sudzaopanso chilichonse.

16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,

“Usaope, iwe Ziyoni;

usafowoke.

17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,

ali ndi mphamvu yopulumutsa.

Adzakondwera kwambiri mwa iwe,

adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,

adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18“Ndidzakuchotserani zowawa

za pa zikondwerero zoyikika;

nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.

19Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi

onse amene anakuponderezani;

ndidzapulumutsa olumala

ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.

Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu

mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.

20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;

pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.

Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu

pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi

pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu

inu mukuona,”

akutero Yehova.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Sefania 3:1-20

Hatima Ya Yerusalemu

13:1 Yer 6:6; Kum 21:18; Eze 23:30Ole mji wa wadhalimu,

waasi na waliotiwa unajisi!

23:2 Yer 5:3; 7:28; 22:21; Kum 1:32; Law 26:33; Za 78:23Hautii mtu yeyote,

haukubali maonyo.

Haumtumaini Bwana,

haukaribii karibu na Mungu wake.

33:3 Za 22:13; Mwa 49:27; Mik 3:3Maafisa wake ni simba wangurumao,

watawala wake ni mbwa mwitu wa jioni,

ambao hawabakizi chochote

kwa ajili ya asubuhi.

43:4 Za 25:3; Isa 48:8; Yer 3:20; 9:4; 23:11; Mal 2:10; Eze 22:26Manabii wake ni wenye kiburi,

ni wadanganyifu.

Makuhani wake hunajisi patakatifu

na kuihalifu sheria.

53:5 Ezr 9:15; Kum 32:4; Za 5:3; 99:3, 4; Mao 3:23; Yer 3:3; Eze 18:25Bwana aliye ndani yake ni mwenye haki,

hafanyi kosa.

Asubuhi kwa asubuhi hutoa haki yake,

kila kukipambazuka huitimiza,

bali mtu dhalimu hana aibu.

63:6 Law 26:31“Nimeyafutilia mbali mataifa,

ngome zao zimebomolewa.

Nimeziacha barabara ukiwa,

hakuna anayepita humo.

Miji yao imeharibiwa;

hakuna mmoja atakayeachwa:

hakuna hata mmoja.

73:7 Yer 7:28; Mwa 6:12; Hos 9:9Niliuambia huo mji,

‘Hakika utaniogopa na kukubali maonyo!’

Ndipo makao yake hayatafutiliwa mbali,

wala adhabu zangu zote hazitakuja juu yake.

Lakini walikuwa bado na shauku

kutenda kwa upotovu katika yote waliyofanya.”

83:8 Za 27:14; 79:6; Yoe 3:2; 3:11; Isa 2:3; Mit 20:22; Ufu 16:1; Yer 10:25; Mao 4:11; Sef 1:18Bwana anasema,

“Kwa hiyo ningojee mimi,

siku nitakayosimama kuteka nyara.

Nimeamua kukusanya mataifa,

kukusanya falme

na kumimina ghadhabu yangu juu yao,

hasira yangu kali yote.

Dunia yote itateketezwa

kwa moto wa wivu wa hasira yangu.

93:9 Sef 2:11; Mwa 4:26; Isa 19:18“Ndipo nitatakasa midomo ya mataifa,

kwamba wote waweze kuliitia jina la Bwana

na kumtumikia kwa pamoja.

103:10 Mwa 10:6; Za 68:31; Mal 1:11; Isa 60:7; Mdo 8:27; 2Nya 32:23Kutoka ngʼambo ya mito ya Kushi

watu wangu wanaoniabudu,

watu wangu waliotawanyika,

wataniletea sadaka.

113:11 Isa 29:22; Yoe 2:26-27; Mwa 50:15; Kut 15:17; Za 59:12; Mt 3:9; Law 26:19Siku hiyo hutaaibishwa

kwa ajili ya makosa yote ulionitendea,

kwa sababu nitawaondoa kutoka mji huu

wale wote wanaoshangilia

katika kiburi chao.

Kamwe hutajivuna tena

katika kilima changu kitakatifu.

123:12 Isa 14:32; Mt 5:3; Lk 6:20; Isa 57:15; Yer 29:12; Nah 1:7Lakini nitakuachia ndani yako

wapole na wanyenyekevu,

ambao wanatumaini jina la Bwana.

133:13 Isa 4:3; 10:21; Za 119:3; Yer 33:16; Ufu 14:5; Ay 16:17; Eze 34:25-28Mabaki ya Israeli hayatafanya kosa;

hawatasema uongo,

wala udanganyifu hautakuwa

katika vinywa vyao.

Watakula na kulala

wala hakuna yeyote

atakayewaogopesha.”

143:14 Za 9:14; 14:7; Zek 2:10; Isa 12:6; 51:11Imba, ee Binti Sayuni;

paza sauti, ee Israeli!

Furahi na kushangilia kwa moyo wako wote,

ee Binti Yerusalemu!

153:15 Yn 1:49; Eze 37:26-28; 48:35; Ufu 21:3; Isa 54:14; Zek 9:9Bwana amekuondolea adhabu yako,

amewarudisha nyuma adui zako.

Bwana, Mfalme wa Israeli, yu pamoja nawe;

kamwe hutaogopa tena madhara yoyote.

163:16 2Fal 19:26; Ebr 12:12; Ay 4:3; Isa 35:3-4Katika siku hiyo watauambia Yerusalemu,

“Usiogope, ee Sayuni;

usiiache mikono yako ilegee.

173:17 Isa 40:1; 62:4; 63:1; Yoe 2:21; Kum 28:63; Hos 14:4Bwana Mungu wako yu pamoja nawe,

yeye ni mwenye nguvu kuokoa.

Atakufurahia kwa furaha kubwa,

atakutuliza kwa pendo lake,

atakufurahia kwa kuimba.”

183:18 Mao 2:6“Huzuni katika sikukuu zilizoamriwa

nitaziondoa kwenu;

hizo ni mzigo na fedheha kwenu.

193:19 Isa 14:2; 60:18; Eze 34:16; Mik 4:6Wakati huo nitawashughulikia

wote waliokudhulumu;

nitaokoa vilema na kukusanya

wale ambao wametawanywa.

Nitawapa sifa na heshima

katika kila nchi ambayo waliaibishwa.

203:20 Yer 29:14; Eze 37:12; Za 22:27; Isa 56:5; 60:18; 66:22; Kum 26:19Wakati huo nitawakusanya;

wakati huo nitawaleta nyumbani.

Nitawapa sifa na heshima

miongoni mwa mataifa yote ya dunia

wakati nitakapowarudishia mateka yenu

mbele ya macho yenu hasa,”

asema Bwana.