Zefaniya 3 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 3:1-20

Tsogolo la Yerusalemu

1Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,

owukira ndi odetsedwa!

2Sumvera aliyense,

sulandira chidzudzulo.

Sumadalira Yehova,

suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.

3Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,

olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,

zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.

4Aneneri ake ndi odzikuza;

anthu achinyengo.

Ansembe ake amadetsa malo opatulika

ndipo amaphwanya lamulo.

5Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;

Iye salakwa.

Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,

ndipo tsiku lililonse salephera,

komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.

6“Ndachotseratu mitundu ya anthu;

ndagwetsa malinga awo.

Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,

popanda aliyense wodutsa.

Mizinda yawo yawonongedwa;

palibe aliyense adzatsalemo.

7Ndinati,

‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa

ndi kumvera kudzudzula kwanga!’

Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,

kapena kuwalanganso.

Koma iwo anali okonzeka

kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.

8Choncho mundidikire,” akutero Yehova,

“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.

Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,

kusonkhanitsa maufumu

ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;

mkwiyo wanga wonse woopsa.

Dziko lonse lidzatenthedwa

ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

9“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse

kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova

ndi kumutumikira Iye pamodzi.

10Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi

anthu anga ondipembedza, omwazikana,

adzandibweretsera zopereka.

11Tsiku limenelo simudzachita manyazi

chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,

popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu

amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.

Simudzakhalanso odzikuza

mʼphiri langa lopatulika.

12Koma ndidzasiya pakati panu

anthu ofatsa ndi odzichepetsa,

amene amadalira dzina la Yehova.

13Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;

sadzayankhulanso zonama,

ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.

Adzadya ndi kugona

ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;

fuwula mokweza, iwe Israeli!

Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!

15Yehova wachotsa chilango chako,

wabweza mdani wako.

Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;

sudzaopanso chilichonse.

16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,

“Usaope, iwe Ziyoni;

usafowoke.

17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,

ali ndi mphamvu yopulumutsa.

Adzakondwera kwambiri mwa iwe,

adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,

adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18“Ndidzakuchotserani zowawa

za pa zikondwerero zoyikika;

nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.

19Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi

onse amene anakuponderezani;

ndidzapulumutsa olumala

ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.

Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu

mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.

20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;

pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.

Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu

pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi

pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu

inu mukuona,”

akutero Yehova.

Japanese Contemporary Bible

ゼパニヤ書 3:1-20

3

1罪と汚れに満ちたエルサレム、

暴力と犯罪の町は災いだ。

2おごり高ぶって、神の声にさえ耳を貸そうとしない。

だれもこの町と話ができない。

あらゆる懲らしめを拒んでいるからだ。

主に信頼せず、神を求めようとしない。

3エルサレムの指導者たちは、

獲物を求めてほえるライオンのようだ。

手に入れることができるなら、

どんなものでもねらっている。

裁判官たちは日暮れの飢えた狼のようだ。

明け方には、獲物の痕跡を残さない。

4エルサレムの預言者たちは

自分の利得を求める偽り者だ。

祭司たちは律法に背いて、神殿を汚している。

5しかし、主はそんな町の中にいても不正を行わない。

日に日に神の正義が明らかになる。

ところが、だれも注意を払わない。

悪者たちは恥知らずだ。

6「わたしは多くの国を切り捨て、

その全領域を荒廃させた。

通りは荒れはてて静まり返り、町々は、

何が起こったかを思い出す者は

一人も残らないまま見捨てられた。

7わたしは思った。

『今こそ、彼らはわたしの言うことを聞くだろう。

確かにわたしの警告に耳を傾けるから、

二度と打つ必要はない』と。

ところが、そうではなかった。

どんなに罰しても、夜明けから夕暮れまで、

夕暮れから夜明けまで、悪を行っている。」

8それでも、主はこうお語りになる。

「もう少しの我慢だ。

悪に染まったこの国々を告発するために

わたしが立ち上がる時が、すぐにくる。

地上の国々を一つに集め、

最も激しい怒りと憤りを下すと決めている。

全地は、わたしのねたみの炎で焼き尽くされる。

イスラエルの残りの者の回復

9その時、戻って来るわたしの民の語ることばを

純粋なヘブル語に変え、

全員が共に主を礼拝できるようにする。

10散らされたわたしの民で

エチオピヤの川の向こうのスーダンに住んでいる者も、

ささげ物を携えて来て、

もう一度彼らの神になってくれるよう、わたしに願う。

11その時あなたは、

もうわたしに反逆しないので、恥じ入る必要はない。

あなたの中から、

高ぶっている横柄な人々を取り除く。

わたしの聖なる山に、

おごり高ぶる者は一人もいなくなる。

12残された者は貧しく謙遜な人々で、主の名に信頼する。

13罪を犯さず、偽りを言わず、欺くこともない。

静かで平和な生活を送り、安らかに眠りにつく。

だれにも脅やかされることがない。」

14シオンの娘よ、歌え。イスラエルよ、叫べ。

エルサレムの娘よ、心から喜び楽しめ。

15神はさばきの手を引っ込め、

あなたの敵の軍を追い散らすからだ。

イスラエルの王である主ご自身が、

あなたのうちに住む。

ついにあなたの苦しみは終わる。

もう恐れる必要はない。

16その日、エルサレムに告げ知らされる。

「元気を出せ。恐れるな。

17-18あなたの神、主が、

あなたのうちに住むために到着したからだ。

この方は力ある救い主で、勝利をお与えになる。

あなたのことをことのほか喜ぶ。

あなたを愛し、責めることはなさらない。」

聞こえてくるのは、

喜びにあふれた聖歌隊の歌声だろうか。

いや、神が、あなたがたのことを喜び、

歌っているのだ。

「わたしは傷ついた者を集め、あなたの恥を取り去ろう。

19また、あなたを虐げた者をきびしく扱おう。

頼る相手のいない弱い者を救い、

追い払われた者を集めよう。

捕囚としてあざけられ、

辱めを受けたわたしの民に誉れを与えよう。

20その時、わたしはあなたがたを呼び集め、連れ戻そう。

そして、全地のあらゆる国民の間で抜きん出た、

りっぱな名を授けよう。

あなたがたの目の前で、あなたがたを元どおり繁栄させる時、

彼らはあなたがたを称賛する。」

このように主が言う。