Zefaniya 2 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 2:1-15

1Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,

inu mtundu wochititsa manyazi,

2isanafike nthawi yachiweruzo,

nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,

usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,

tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.

3Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,

inu amene mumachita zimene amakulamulani.

Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;

mwina mudzatetezedwa

pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.

Za Afilisti

4Gaza adzasiyidwa

ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.

Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu

ndipo Ekroni adzazulidwa.

5Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,

inu mtundu wa Akereti;

mawu a Yehova akutsutsa

iwe Kanaani, dziko la Afilisti.

“Ndidzakuwononga

ndipo palibe amene adzatsale.”

6Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,

lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.

7Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;

adzapezako msipu.

Nthawi ya madzulo adzagona

mʼnyumba za Asikeloni.

Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;

adzabwezeretsa mtendere wawo.

Za Mowabu ndi Amoni

8“Ndamva kunyoza kwa Mowabu

ndi chipongwe cha Amoni,

amene ananyoza anthu anga

ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.

9Choncho, pali Ine Wamoyo,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,

“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,

Amoni adzasanduka ngati Gomora;

malo a zomeramera ndi maenje a mchere,

dziko la bwinja mpaka muyaya.

Anthu anga otsala adzawafunkha;

opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”

10Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,

chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.

11Yehova adzawachititsa mantha kwambiri

pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.

Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,

uliwonse ku dziko la kwawo.

Za Kusi

12“Inunso anthu a ku Kusi,

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Za Asiriya

13Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto

ndi kuwononga Asiriya,

kusiya Ninive atawonongekeratu

ndi owuma ngati chipululu.

14Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,

pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.

Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu

adzakhala pa nsanamira zake.

Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,

mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,

nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.

15Umenewu ndiye mzinda wosasamala

umene kale unali wotetezedwa.

Unkanena kuti mu mtima mwake,

“Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”

Taonani lero wasanduka bwinja,

kokhala nyama zakutchire!

Onse owudutsa akuwunyoza

ndi kupukusa mitu yawo.

La Bible du Semeur

Sophonie 2:1-15

L’appel à la conversion

1Rassemblez-vous, ╵regroupez-vous2.1 Autre traduction : Réfléchissez, rentrez en vous-mêmes.,

ô vous, gens sans vergogne,

2avant que le décret ╵soit publié,

que le jour passe ╵comme la bale au vent !

N’attendez pas ╵que se fasse sentir sur vous ╵l’ardeur de la colère ╵de l’Eternel,

que vous atteigne

le jour de la colère ╵de l’Eternel.

3Tournez-vous donc vers l’Eternel, ╵vous tous les humbles du pays,

vous qui faites ce qui est droit,

cherchez à accomplir ╵ce qui est juste. ╵Efforcez-vous d’être humbles ;

peut-être serez-vous ╵mis à l’abri

au jour de la colère ╵de l’Eternel.

Malheur aux Philistins

4Gaza sera abandonnée,

Ashkelôn sera dévastée,

les habitants d’Ashdod ╵seront chassés au loin ╵à l’heure de midi.

Eqrôn sera déracinée.

5Malheur aux habitants ╵des côtes de la mer,

au peuple venu de la Crète2.5 Les Philistins. !

Car contre vous se fait entendre ╵la parole de l’Eternel :

« Malheur à Canaan, ╵pays des Philistins !

Je te dévasterai ╵et je te viderai ╵de tous tes habitants. »

6La région de la mer ╵servira de pacages,

de citernes2.6 Texte incertain. pour les bergers

et de parcs à moutons.

7Ce district va échoir au reste ╵du peuple de Juda.

Ils y mèneront paître leurs troupeaux2.7 Autre traduction : ils y trouveront leur pâture..

Le soir, ils se reposeront ╵dans les maisons à Ashkelôn,

car l’Eternel, leur Dieu, ╵interviendra pour eux

et changera leur sort2.7 Autre traduction : et ramènera ceux d’entre eux qui auront été emmenés en captivité..

Malheur aux faux frères

8J’ai entendu ╵les propos insultants ╵des Moabites,

et les outrages ╵des Ammonites2.8 Moab et Ammon: peuplades installées à l’est du Jourdain et de la mer Morte, qui faisaient partie, avec les Edomites, des ennemis traditionnels d’Israël.

qui insultaient mon peuple

et qui s’agrandissaient ╵aux dépens de son territoire.

9Aussi vrai que je vis,

déclare l’Eternel, ╵le Seigneur des armées célestes, ╵Dieu d’Israël :

Moab sera comme Sodome,

les Ammonites ╵seront comme Gomorrhe2.9 Voir Gn 19.24-25.,

leur pays deviendra ╵un lieu couvert d’orties,

une mine de sel,

et une terre dévastée ╵à perpétuité.

Le reste de mon peuple ╵les pillera,

oui, ce qui restera de ma nation ╵en prendra possession.

10Cela leur adviendra ╵pour prix de leur orgueil,

car ils ont insulté le peuple ╵de l’Eternel, ╵le Seigneur des armées célestes,

et se sont agrandis ╵à ses dépens.

11Avec eux, l’Eternel ╵se montrera terrible,

car il anéantit ╵tous les dieux de la terre ;

alors tous les peuples, ╵jusques aux plus lointains, ╵se prosterneront devant lui,

chacun dans sa contrée.

Malheur aux Ethiopiens

12Vous aussi, Ethiopiens2.12 De 715 à 663 av. J.-C., l’Egypte avait été gouvernée par une dynastie éthiopienne.,

vous serez transpercés ╵par mon épée.

Malheur à Ninive l’orgueilleuse

13L’Eternel étendra ╵la main contre le nord,

il fera périr l’Assyrie

et il dévastera Ninive

pour en faire un désert aride.

14Au milieu de la ville ╵se reposeront des troupeaux,

des animaux de toute espèce,

le hibou et le hérisson

y passeront la nuit ╵parmi ses chapiteaux.

On entendra ╵hululer aux fenêtres :

dès le seuil des maisons, ╵ce ne sera que ruines,

et les poutres de cèdres ╵seront à nu.

15La voilà donc, ╵cette cité joyeuse,

installée en toute sécurité,

et qui se dit :

« C’est moi, et rien que moi ! »

Comment est-elle devenue ╵une terre ainsi désolée,

un gîte pour les bêtes ?

Quiconque passera ╵dans sa proximité

se moquera d’elle en sifflant ╵et en faisant des gestes de la main.