Yoweli 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 3:1-21

Kuweruzidwa kwa Mitundu ya Anthu

1“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo,

nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,

2ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse

ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati.

Kumeneko ndidzawaweruza

chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli,

pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu

ndikugawa dziko langa.

3Anagawana anthu anga pochita maere

ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere;

anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo

kuti iwo amwe.

4“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu. 5Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano. 6Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.

7“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu. 8Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.

9Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:

Konzekerani nkhondo!

Dzutsani ankhondo amphamvu!

Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.

10Sulani makasu anu kuti akhale malupanga

ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.

Munthu wofowoka anene kuti,

“Ndine wamphamvu!”

11Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,

ndipo musonkhane kumeneko.

Tumizani ankhondo anu Yehova!

12“Mitundu ya anthu idzuke;

ipite ku Chigwa cha Yehosafati,

pakuti kumeneko Ine ndidzakhala

ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.

13Tengani chikwakwa chodulira tirigu,

pakuti mbewu zakhwima.

Bwerani dzapondeni mphesa,

pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza

ndipo mitsuko ikusefukira;

kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”

14Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,

mʼchigwa cha chiweruzo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira

mʼchigwa cha chiweruzo.

15Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,

ndipo nyenyezi sizidzawalanso.

16Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni

ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;

dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.

Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,

linga la anthu a ku Israeli.

Madalitso a Anthu a Mulungu

17“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,

ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.

Yerusalemu adzakhala wopatulika;

alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,

ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;

mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.

Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova

ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.

19Koma Igupto adzasanduka bwinja,

Edomu adzasanduka chipululu,

chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda

mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.

20Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya

ndi Yerusalemu ku mibadomibado.

21Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke

ndidzakhululuka.”

Yehova amakhala mu Ziyoni!

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約珥書 3:1-21

上帝要審判萬國

1「到那日,在我復興猶大耶路撒冷的時候, 2我要聚集萬國,帶他們下到約沙法3·2 約沙法」意思是「耶和華審判」。谷,在那裡審判他們,因為他們把我的子民,就是我的產業以色列,分散到各國,並瓜分我的土地。 3他們抽籤分了我的子民,將男童換妓女,賣女童買酒喝。

4泰爾西頓非利士境內所有的人啊,你們為什麼這樣對我?你們要報復我嗎?如果你們是報復我,我必速速使你們遭報應。 5你們奪去我的金銀,搶走我的珍寶,拿去放在你們的廟中, 6並把猶大耶路撒冷的居民賣給希臘人,使他們遠離家鄉。 7然而,他們被賣到哪裡,我要從哪裡把他們帶回來,並要使你們得到報應, 8我要把你們的兒女賣給猶大人,猶大人必把他們賣給遠方的示巴人。這是耶和華說的。」

9你們去向萬國宣告:

「要召集勇士,徵調軍隊,

前去打仗!

10要將犁頭打成刀劍,

把鐮刀鑄成矛頭,

軟弱的人也要做勇士!

11四圍的列國啊,

你們快快聚集到那裡吧!」

耶和華啊,

求你差遣大能的勇士降臨。

12「萬國都要起來,

上到約沙法谷受審判,

因為我要坐在那裡審判他們。

13開鐮吧,因為莊稼熟了;

踩踏吧,因為榨酒池的葡萄滿了。

他們惡貫滿盈,如酒池滿溢。」

14千千萬萬的人聚集在審判谷,

因為耶和華的日子要臨到那裡。

15日月昏暗,

星辰無光。

16耶和華從錫安發出怒吼,

耶路撒冷發出雷聲,

天地為之震動。

但耶和華卻是祂子民的避難所,

以色列人的堡壘。

17「這樣,你們就知道我是你們的上帝耶和華,

我住在錫安——我的聖山上。

耶路撒冷必成為聖地,

外族人必不再侵犯它。

18「到那日,群山要滴下甜酒,

丘陵要流出乳汁。

猶大的溪澗碧水常流,

必有清泉從耶和華的殿中流出,

澆灌什亭谷。

19埃及必一片荒涼,

以東必成為不毛之地,

因為他們曾殘暴地對待猶大人,

猶大濫殺無辜。

20猶大必人口興盛,

耶路撒冷必存到萬代。

21我必追討3·21 追討」希伯來文是「洗淨」。尚未追討的血債,

因為耶和華住在錫安。」