Yohane 9 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 9:1-41

Yesu Achiritsa Munthu Wosaona Chibadwire

1Iye akuyendabe, anaona munthu wosaona chibadwire. 2Ophunzira ake anamufunsa Iye kuti, “Rabi anachimwa ndani, munthuyu kapena makolo ake, kuti iye abadwe wosaona?”

3Yesu anayankha kuti, “Sikuti iyeyu anachimwa kapena makolo ake, koma izi zinachitika kuti Mulungu aonetse ntchito zake mwa iyeyu. 4Ife tiyenera kugwira ntchito za Iye amene anandituma kukanali masana. Usiku ukubwera, pamene wina aliyense sadzagwira ntchito. 5Pamene Ine ndili mʼdziko lapansi, Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi.”

6Atanena izi, Iye anathira malovu pansi ndi kukanda dothi, napaka matopewo mʼmaso a munthuyo. 7Yesu anamuwuza iye kuti, “Pita kasambe mʼdziwe la Siloamu” (mawu awa akutanthauza Wotumidwa). Choncho munthuyo anapita ndi kukasamba ndipo anabwerako akupenya.

8Anzake ndi iwo amene anamuona iye poyamba akupempha anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene amapemphapempha uja?” 9Ena ananena kuti anali yemweyo.

Ena anati, “Ayi, sakuoneka ngati yemweyo.”

Koma iye mwini ananenetsa kuti, “Munthuyo ndine.”

10Iwo anafunsitsa kuti, “Kodi nanga maso ako anatsekuka bwanji?”

11Iye anayankha kuti, “Munthu wina wotchedwa Yesu anakanda dothi ndi kupaka mʼmaso anga. Iye anandiwuza kuti ndipite ku Siloamu ndi kukasamba. Choncho ndinapita kukasamba, ndipo ndikuona.”

12Iwo anamufunsa iye kuti, “Ali kuti munthu ameneyu?”

Iye anati, “Ine sindikudziwa.”

Afarisi Afufuza za Kuchiritsidwa Kwake

13Iwo anabwera naye munthu amene poyamba anali wosaona kwa Afarisi. 14Tsono linali la Sabata tsiku limene Yesu anakanda dothi ndi kutsekula maso a munthuyu. 15Choncho Afarisi anamufunsanso iye momwe analandirira kuona kwake. Munthuyo anayankha kuti, “Iye anapaka matope mʼmaso anga, ndipo ine ndinakasamba, ndipo ndikuona.”

16Ena a Afarisi anati, “Munthu uyu siwochokera kwa Mulungu, pakuti sasunga Sabata.”

Koma enanso anafunsa kuti, “Kodi munthu wochimwa angachite bwanji zizindikiro zodabwitsa ngati izi?” Choncho iwo anagawanika.

17Pomaliza iwo anatembenukiranso kwa munthu amene anali wosaona uja nati, “Kodi iwe unena chiyani za Iye poti ndi maso ako amene watsekula?”

Munthuyo anayankha kuti, “Iye ndi mneneri.”

18Ayuda sanakhulupirirebe kuti iye anali wosaona ndi kuti anayamba kuona kufikira atayitana makolo ake. 19Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu ndi mwana wanu? Kodi iyeyu ndi amene mukunena kuti anabadwa wosaona? Nanga zikutheka bwanji kuti akuona?”

20Makolo anayankha kuti, “Ife tikudziwa kuti ndi mwana wathu, ndipo tikudziwa kuti anabadwa wosaona. 21Koma sitidziwa zimene zachitika kuti tsopano azipenya. Amenenso wamupenyetsa sitikumudziwa. Mufunseni ndi wamkulu; iye adziyankhira yekha.” 22Makolo ake ananena izi chifukwa amaopa Ayuda, popeza Ayuda anatsimikiza kale kuti aliyense amene adzamuvomereza Yesu kuti anali Khristu adzatulutsidwa mʼsunagoge. 23Ichi ndi chifukwa chake makolo ake anati, “Mufunseni iye ndi wamkulu.”

24Iwo anamuyitanitsa kachiwiri munthu amene anali wosaonayo. Iwo anati, “Lemekeza Mulungu. Ife tikudziwa kuti munthu uyu ndi wochimwa.”

25Iye anayankha kuti, “Zakuti Iye ndi wochimwa kapena ayi, ine sindikudziwa. Ine ndikudziwa chinthu chimodzi. Ndinali wosaona koma tsopano ndikuona!”

26Kenaka anamufunsa kuti, “Kodi Iye anachita chiyani kwa iwe? Iye anatsekula motani maso ako?”

27Iye anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kale ndipo inu simunamvetsetse. Chifukwa chiyani mukufuna mumvenso? Mukufuna kuti inu mukhale ophunzira akenso?”

28Pamenepo anamunyoza ndipo anati, “Iwe ndiye ophunzira wa munthuyu! Ife ndife ophunzira a Mose! 29Ife tikudziwa kuti Mulungu anayankhula kwa Mose, koma za munthu uyu, ife sitikudziwa ngakhale kumene akuchokera.”

30Munthuyo anayankha kuti, “Tsopano izi ndi zodabwitsa! Inu simukudziwa kumene akuchokera, komabe iye watsekula maso anga. 31Ife tikudziwa kuti Mulungu samvera wochimwa. Iye amamvera munthu woopa Mulungu amene amachita chifuniro chake. 32Palibe amene anamvapo za kutsekula maso a munthu wobadwa wosaona. 33Ngati munthu uyu akanakhala wosachokera kwa Mulungu, palibe chimene Iye akanachita.”

34Pamenepo anayankha kuti, “Iwe unabadwa mu uchimo kotheratu; bwanji ukuyesa kutiphunzitsa ife!” Ndipo anamutulutsa kunja.

Kusaona kwa Uzimu

35Yesu anamva kuti anamutulutsa kunja ndipo pamene anamupeza anati, “Kodi ukukhulupirira Mwana wa Munthu?”

36Munthuyo anafunsa kuti, “Kodi, Ambuye, ameneyo ndi ndani? Ndiwuzeni kuti ndimukhulupirire Iye?”

37Yesu anati, “Iwe wamuona tsopano. Zoonadi ndiye amene akuyankhula nawe.”

38Pamenepo munthuyo anati, “Ambuye, ndikukhulupirira,” ndipo anamulambira Iye.

39Yesu anati, “Ndinabwera pansi pano kudzaweruza kuti osaona aone ndi openya asaone.”

40Afarisi ena amene anali pafupi naye anamva akunena izi ndipo anafunsa kuti, “Chiyani? Kodi ndife osaonanso?”

41Yesu anati, “Mukanakhala osaona, simukanachimwa; koma tsopano popeza mukuti mumaona, ndinu ochimwabe.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иохан 9:1-41

Исцеление слепого

1Однажды, проходя мимо, Исо увидел человека, слепого от рождения. 2Его ученики спросили у Него:

– Учитель, почему этот человек родился слепым? Кто согрешил: он сам или его родители?

3– Нет, это не из-за его греха или греха его родителей, – ответил Исо, – это произошло для того, чтобы на нём были явлены дела Всевышнего. 4Пока ещё день не кончился, мы должны совершать дела Того, Кто послал Меня. Наступает ночь, и тогда уже никто не сможет ничего делать. 5Пока Я в мире, Я – свет миру.

6Сказав это, Исо плюнул на землю, смешал слюну с землёй и помазал ею глаза слепому.

7– А теперь пойди и умойся в пруду Силоам, – сказал Он слепому (Силоам значит: «Посланный»).

Слепой пошёл, умылся и вернулся зрячим. 8Соседи его и те, кто раньше видели его просящим милостыню, спрашивали:

– Разве это не он сидел и просил милостыню?

9Одни говорили:

– Да, это он.

Другие говорили:

– Нет, он только похож на него.

Исцелённый же утверждал:

– Это я.

10– Как же ты прозрел? – спрашивали они.

11Он ответил:

– Человек, Которого зовут Исо, смешал грязь и помазал мои глаза, потом Он сказал мне пойти в Силоам и умыться. Я пошёл, умылся и стал видеть.

12– Где Этот Человек? – спрашивали они его.

– Я не знаю, – отвечал исцелённый.

Религиозные вожди допрашивают исцелённого

13Человека, который раньше был слепым, привели к блюстителям Закона, 14потому что Исо смешал грязь и открыл ему глаза в субботу. 15Блюстители Закона тоже спросили его, как он обрёл зрение.

– Он помазал мои глаза грязью, – ответил исцелённый, – я умылся и теперь вижу.

16Некоторые блюстители Закона стали говорить:

– Человек Этот не от Всевышнего, потому что Он делает то, что запрещается делать в субботу.

Другие же спрашивали:

– Как грешник может творить такие знамения?

Мнения разделились. 17Тогда они опять стали расспрашивать слепого:

– Что ты сам можешь сказать о Нём? Это ведь твои глаза Он открыл.

Человек ответил:

– Он пророк.

18Предводители иудеев всё ещё не верили, что он был слеп и что обрёл зрение, и поэтому позвали его родителей.

19– Это ваш сын? – спросили они. – Это о нём вы говорите, что он родился слепым? Как же он может сейчас видеть?

20– Мы знаем, что это наш сын, – ответили родители, – и мы знаем, что он родился слепым. 21А как он сейчас может видеть и кто открыл его глаза, мы не знаем. Спросите его сами. Он уже совершеннолетний и может сам ответить за себя.

22Родители так ответили из боязни перед предводителями иудеев, так как те уже вынесли решение о том, что кто признает Исо Масехом, тот будет отлучён от общества. 23Поэтому родители и сказали: «Он уже совершеннолетний, спросите его самого».

24Они во второй раз вызвали человека, который был слепым.

– Воздай славу Всевышнему9:24 Эти слова были формулой судебной клятвы, обязывавшей говорить правду (см. Иеш. 7:19)., – сказали они, – мы знаем, что Этот Человек грешник.

25Исцелённый ответил:

– Грешник Он или нет, я не знаю. Я знаю одно, что я был слеп, а сейчас вижу!

26Они спросили:

– Что Он с тобой сделал? Как Он открыл твои глаза?

27Он ответил:

– Я уже говорил вам, а вы не слушали. Зачем вы хотите ещё раз это услышать? Вы тоже хотите стать Его учениками?

28Они стали оскорблять его и сказали:

– Сам ты Его ученик! Мы ученики пророка Мусо! 29Мы знаем, что с Мусо говорил Всевышний, а об Этом Человеке мы даже не знаем, откуда Он.

30Исцелённый ответил:

– Вот это-то и странно! Вы не знаете, откуда Он, а Он открыл мне глаза. 31Мы знаем, что Всевышний грешников не слушает. Он слушает только тех, кто чтит Его и поступает по Его воле. 32Ведь испокон веков никто не слышал, чтобы у рождённого слепым открылись глаза9:32 Прозрение слепых часто рассматривалось пророками, особенно Исаией, как знак времён Масеха (см. Ис. 29:18; 35:5; 42:7, 18).. 33И если бы Этот Человек не был от Всевышнего, то Он не смог бы сделать ничего такого.

34Они на это ответили:

– Ты был рождён в грехах, как ты смеешь нас учить!

И они выгнали его вон9:34 Или: «отлучили его (от общества иудеев)», также в ст. 35..

О духовной слепоте

35Исо, услышав о том, что блюстители Закона выгнали его вон, нашёл его и спросил:

– Ты веришь в Ниспосланного как Человек?

36– А кто Он, Господин? – спросил исцелённый. – Скажи мне, чтобы я в Него поверил.

37Исо сказал:

– Ты сейчас Его видишь, Он говорит с тобой.

38Тогда человек ответил:

– Повелитель, я верю, – и поклонился Исо.

39Исо сказал:

– Я пришёл в этот мир для суда, чтобы слепые видели, а те, кто видят, стали слепыми.

40Блюстители Закона, которые были с Ним, слышали это и спросили:

– Что? Мы, значит, тоже слепы?

41Исо сказал:

– Если бы вы были слепы, то греха не было бы на вас, но так как вы заявляете, что видите, то грех ваш на вас остаётся.