Yohane 8 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 8:1-59

1Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi. 2Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa. 3Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo 4anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo. 5Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?” 6Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye.

Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake. 7Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.” 8Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.

9Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo. 10Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”

11Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.”

“Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”

Za Umboni wa Yesu

12Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”

13Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”

14Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita. 15Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense. 16Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma. 17Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka. 18Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”

19Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?”

Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.” 20Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.

Mkangano Woti Yesu Ndani

21Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”

22Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’ ”

23Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino. 24Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”

25Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?”

Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi, 26ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”

27Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake. 28Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa. 29Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.” 30Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.

Ana a Abrahamu

31Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga. 32Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”

33Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’ ”

34Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo. 35Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. 36Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu. 37Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu. 38Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”

39Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.”

Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita. 40Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi. 41Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.”

Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”

Ana a Mdierekezi

42Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha. 43Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga. 44Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza. 45Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine! 46Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira? 47Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”

Zomwe Yesu Ananena za lye Mwini

48Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”

49Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza. 50Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza. 51Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.”

52Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ 53Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”

54Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine. 55Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake. 56Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”

57Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”

58Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!” 59Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иохан 8:1-59

1А Исо пошёл на Оливковую гору.

Прощение женщины, уличённой в супружеской измене

2Рано утром Он опять был в храме. Вокруг Него собралось много людей, и Он сел и стал их учить. 3Учители Таврота и блюстители Закона привели женщину, уличённую в супружеской измене. Они поставили её перед народом 4и сказали Исо:

– Учитель, мы поймали эту женщину на месте преступления, она изменила мужу! 5Мусо повелевает в Тавроте побивать таких камнями8:5 См. Втор. 22:22-24.. А Ты что скажешь?

6Они спросили это, чтобы найти повод уловить Исо в чём-либо и обвинить Его8:6 Если бы Исо осудил женщину, то Он пошёл бы против римских законов, запрещавших иудеям самим применять смертную казнь (см. 18:31), если бы отпустил её – вступил бы в противоречие с законами Таврота (см. Лев. 20:10).. Исо склонился и писал пальцем на земле. 7Они упрямо продолжали Его спрашивать. Тогда Исо выпрямился и сказал:

– Кто из вас без греха, пусть первым бросит в неё камень.

8И Он опять, склонившись, продолжал писать на земле. 9Тогда они начали по одному уходить, начиная с самых старших. В конце концов остались только Исо и женщина. 10Исо выпрямился и спросил:

– Женщина, где твои обвинители? Разве никто не осудил тебя?

11– Никто, Господин, – ответила она.

– И Я тебя не осуждаю, – сказал Исо. – Иди и больше не греши.

Исо Масех – свет миру

12Когда Исо вновь заговорил с народом, Он сказал:

– Я свет миру8:12 Свет, так же как и вода, был символом праздника Шалашей. Согласно древнему источнику во дворе храма зажигались большие, в 23 м высотой, золотые светильники, перед которыми танцевали верующие с факелами в руках.. Тот, кто идёт за Мной, не будет ходить во тьме, но будет иметь свет жизни.

13Блюстители Закона тогда сказали Ему:

– Но ведь Ты Сам свидетельствуешь о Себе, значит, Твоё свидетельство недействительно.

14Исо ответил:

– Даже если Я и Сам свидетельствую о Себе, Моё свидетельство истинно, потому что Я знаю, откуда Я пришёл и куда Я иду. Вы же не имеете никакого понятия ни о том, откуда Я пришёл, ни о том, куда Я иду. 15Вы судите по человеческим меркам, Я же не сужу никого. 16Но если Я и сужу, Мой суд справедлив, потому что Я не один, со Мной Отец, Который послал Меня. 17В вашем же Законе написано, что когда свидетельствуют двое, то их свидетельство имеет силу8:17 См. Втор. 19:15.. 18О Себе свидетельствую Я Сам и Мой Отец, Который послал Меня.

19Они тогда спросили:

– Где же Твой Отец?

Исо ответил:

– Вы не знаете ни Меня, ни Моего Отца. Если бы вы знали Меня, вы бы знали и Моего Отца.

20Он сказал это, когда учил в храме, там, где собирали пожертвования. Никто, однако, не схватил Его, потому что Его время ещё не настало.

Исо Масех пришёл свыше

21Исо сказал им ещё раз:

– Я ухожу, и вы будете искать Меня, и умрёте во грехе вашем. Туда, куда Я иду, вы не сможете прийти.

22Предводители иудеев стали тогда спрашивать:

– Он что, собирается покончить с Собой? Может, это Он имеет в виду, когда говорит: «Туда, куда Я иду, вы не сможете прийти»?

23Исо продолжал:

– Вы земные, а Я пришёл с небес. Вы принадлежите этому миру, а Я этому миру не принадлежу. 24Поэтому Я сказал вам, что вы умрёте в ваших грехах. Если вы не поверите, что Я Тот, за Кого Себя выдаю8:24 Букв.: «Я есть». См. сноску на 8:58. Так же в 8:28., вы действительно умрёте в ваших грехах.

25– Кто же Ты такой? – спросили они.

– Я вам уже давно говорю, кто Я такой, – ответил Исо. – 26Я мог бы обвинить вас во многом, но Тот, Кто послал Меня, говорит истину, и то, что Я слышал от Него, Я говорю миру.

27Они не поняли, что Он говорил им о Небесном Отце. 28Тогда Исо сказал:

– Когда вы вознесёте8:28 См. сноску на 3:14. Ниспосланного как Человек, тогда и узнаете, что Я Тот, за Кого Себя выдаю, и что от Себя Я не делаю ничего, а говорю то, чему Отец научил Меня. 29Пославший Меня всегда со Мной, Он Меня одного не оставляет, потому что Я делаю то, что угодно Ему.

30Когда Он это говорил, многие поверили в Него.

Дети Всевышнего и дети дьявола

31Исо сказал иудеям, поверившим в Него:

– Если вы будете верны Моему учению, то вы действительно Мои ученики. 32Вы тогда узнаете истину, и истина сделает вас свободными.

33Они ответили:

– Мы потомки Иброхима и никогда не были никому рабами. Как это мы можем «стать свободными»?

34Исо ответил:

– Говорю вам истину, каждый, кто грешит, – раб греха. 35Раб не может надеяться на постоянное место в доме, сын же остаётся в нём навсегда. 36Поэтому если Сын вас освободит, вы будете действительно свободными. 37Я знаю, что вы потомки Иброхима, но вы готовы убить Меня, потому что Моё слово не находит в вас отклика. 38Я говорю вам о том, что Я видел у Моего Отца, а вы делаете то, что вы услышали от вашего отца.

39– Наш отец – Иброхим, – ответили они.

– Если бы вы были детьми Иброхима, – ответил Исо, – вы бы делали дела Иброхима, 40но вы стремитесь убить Меня, Человека, говорящего вам истину, – истину, которую Я слышал от Всевышнего. Иброхим так не делал. 41Вы делаете то, что делал ваш отец.

– Мы не какие-нибудь незаконнорождённые, – говорили они, – у нас один Отец – Сам Всевышний.

42Исо сказал им:

– Если бы Всевышний был вашим Отцом, то вы любили бы Меня, потому что Я пришёл от Всевышнего, и вот Я здесь. Я пришёл не Сам от Себя, Меня послал Он. 43Почему вы не понимаете того, о чём Я вам говорю? Да потому, что вы не можете даже слышать слова Моего. 44Вы принадлежите вашему отцу, дьяволу, и хотите исполнить желания вашего отца. Он от начала был человекоубийцей и не устоял в истине, потому что в нём нет никакой истины. Когда он лжёт, то делает то, что ему свойственно, потому что он лжец и отец лжи. 45Но Я говорю вам истину, и поэтому вы Мне не верите! 46Может ли кто-либо из вас уличить Меня во грехе? Если же Я говорю истину, то почему вы Мне не верите? 47Тот, кто принадлежит Всевышнему, слышит, что говорит Всевышний. Вы не слышите Меня потому, что вы не принадлежите Всевышнему.

Исо Масех говорит о Своём вечном существовании

48Бывшие там иудеи стали говорить Исо:

– Ну разве мы не правы, когда говорим, что Ты сомарянин8:48 Назвать иудея сомарянином означало оскорбить его (см. сноски на 4:7, 9)., и притом одержим демоном!

49– Я не одержим, – ответил Исо, – Я чту Моего Отца, а вы бесчестите Меня. 50Я не ищу славы Себе, но есть Тот, Кто ищет её для Меня, пусть Он и судит. 51Говорю вам истину: кто соблюдает слово Моё, тот никогда не увидит смерти8:51 Имеется в виду духовная смерть..

52Тогда иудеи закричали:

– Теперь мы точно знаем, что Ты одержим демоном! Иброхим умер, и все другие пророки умерли, а Ты говоришь, что кто исполняет Твоё слово, тот никогда не умрёт. 53Неужели Ты больше нашего отца Иброхима, который умер? И другие пророки тоже умерли. А кем Ты Себя считаешь?

54Исо ответил:

– Если Я славлю Самого Себя, то слава эта ничего не значит. Меня прославляет Мой Отец, Которого вы называете своим Богом, 55хотя вы Его и не знаете. Но Я Его знаю, и если бы Я сказал, что не знаю Его, то был бы таким же лжецом, как и вы. Но Я знаю Его и исполняю Его слово. 56Ваш отец Иброхим радовался при мысли, что увидит Мой день, и он его увидел и был счастлив.

57– Да Тебе нет и пятидесяти лет, – говорили Ему иудеи, – и Ты видел Иброхима?

58Исо сказал:

– Говорю вам истину, ещё до того, как Иброхим родился, Я ЕСТЬ!8:58 Часто в Писании, когда Всевышний говорил о Себе, Он употреблял это же самое выражение (см., напр., Исх. 3:14; Втор. 32:39; Ис. 41:4; 43:10-13 и сноски на эти стихи). Таким ответом Исо недвусмысленно даёт понять, что Он и есть Всевышний.

59Тогда они схватили камни, чтобы бросить в Него, но Исо скрылся и вышел из храма8:59 Намёк Исо на то, что Он Всевышний, был расценён Его оппонентами как кощунство, за которое следовало побивать камнями (см. Лев. 24:16)..