Yohane 8 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 8:1-59

1Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi. 2Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa. 3Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo 4anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo. 5Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?” 6Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye.

Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake. 7Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.” 8Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.

9Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo. 10Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”

11Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.”

“Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”

Za Umboni wa Yesu

12Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”

13Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”

14Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita. 15Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense. 16Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma. 17Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka. 18Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”

19Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?”

Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.” 20Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.

Mkangano Woti Yesu Ndani

21Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”

22Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’ ”

23Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino. 24Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”

25Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?”

Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi, 26ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”

27Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake. 28Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa. 29Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.” 30Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.

Ana a Abrahamu

31Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga. 32Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”

33Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’ ”

34Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo. 35Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. 36Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu. 37Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu. 38Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”

39Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.”

Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita. 40Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi. 41Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.”

Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”

Ana a Mdierekezi

42Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha. 43Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga. 44Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza. 45Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine! 46Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira? 47Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”

Zomwe Yesu Ananena za lye Mwini

48Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”

49Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza. 50Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza. 51Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.”

52Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ 53Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”

54Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine. 55Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake. 56Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”

57Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”

58Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!” 59Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.

Knijga O Kristu

Ivan 8:1-59

Preljubnica

1Isus se vrati na Maslinsku goru, 2no rano sljedećeg jutra opet dođe u Hram. Mnoštvo se ubrzo okupi oko njega, a on sjedne i počne ih poučavati. 3Dok je govorio, židovski poglavari i farizeji dovedu mu neku ženu uhvaćenu u preljubu. Postave ju ispred radoznaloga mnoštva.

4“Učitelju,” rekoše Isusu, “ova je žena zatečena u sâmome činu preljuba. 5Mojsijev nam zakon kaže da bismo ju trebali kamenovati. Što ti na to kažeš?”

6Htjeli su ga navesti da kaže nešto zbog čega bi ga mogli optužiti, ali Isus se samo sagnuo i počeo pisati prstom po prašini. 7Kako su i dalje zahtijevali da im odgovori, on se uspravi i reče im: “Pa dobro, kamenujte ju—ali neka prvi baci kamen na nju onaj od vas koji još nikada nije zgriješio!” 8Zatim se ponovno sagne i nastavi pisati po tlu.

9A vjerski se poglavari krišom raziđu jedan po jedan, počevši od najstarijega. Isus ostane ispred mnoštva sam sa ženom. 10Opet se uspravi i reče joj: “Gdje su tvoji tužitelji, ženo? Zar te nijedan nije osudio?”

11“Nijedan, Gospodine”, odgovori žena.

A Isus joj reče: “Ni ja te ne osuđujem. Idi i ne griješi više!”

Isus, svjetlo svijeta

12Isus ponovno reče narodu: “Ja sam svjetlo svijeta. Tko me slijedi, neće se spoticati u tami, već će imati svjetlo koje vodi u život.”

13Farizeji mu odgovore: “Ti svjedočiš sam o sebi i zato što govoriš nije istina!”

14Isus reče: “Govorim istinu, iako svjedočim sam o sebi, jer znam odakle sam došao i kamo idem. A vi to ne znate. 15Vi o meni sudite prema ljudskim mjerilima, ali ja nikoga ne osuđujem. 16A i kad bih sudio, bio bi to potpuno pravedan sud jer nisam sâm—uza me je Otac koji me poslao. 17Vaš Zakon kaže da svjedočanstvo dvojice, ako je istovjetno, valja prihvatiti kao istinito.8:17 Vidjeti: Ponovljeni zakon 19:15. 18Evo, ja svjedočim za sebe, a moj je Otac koji me je poslao drugi svjedok.”

19“Gdje ti je Otac?” upitaju ga. Isus im odgovori: “Ne znate tko sam ja, pa ne znate ni tko mi je Otac. Kad biste mene poznavali, znali biste i njega.” 20Isus je sve to rekao u riznici dok je poučavao u Hramu. Pa ipak, nisu ga uhitili jer još nije došlo njegovo vrijeme.

Upozorenje nevjernicima

21Poslije im Isus ponovno reče: “Ja odlazim, a vi ćete me tražiti i umrijet ćete u svojem grijehu. Kamo ja idem, vi ne možete doći.”

22Židovi se nato stanu pitati: “Da se možda ne kani ubiti? Na što je mislio kad je rekao: ‘Kamo ja idem, vi ne možete doći’?”

23On im tada reče: “Vi ste odozdol, a ja sam odozgor. Vi ste od ovoga svijeta, a ja nisam. 24Eto, zato sam rekao da ćete umrijeti u svojim grijesima. Jer ne povjerujete li da sam onaj koji kažem da jesam, umrijet ćete u svojim grijesima.”

25“Reci nam tko si”, tražili su. On odgovori: “Ja sam onaj koji vam od početka i tvrdim da jesam.8:25 Ili: Zašto vam uopće i govorim? 26Imao bih mnogo toga za vas kazati i osuditi vas za mnogošto, ali neću jer govorim samo ono što mi kaže onaj koji me poslao, a on je Istiniti.” 27Oni, međutim, nisu razumjeli da im govori o Ocu.

28Stoga Isus reče: “Kad podignete Sina Čovječjega na križ, shvatit ćete da sam ja taj i da vam nisam govorio vlastite misli, nego samo ono što me je Otac naučio. 29Onaj koji me je poslao sa mnom je. Ne ostavlja me samoga zato što uvijek činim ono što je njemu ugodno.”

30Mnogi koji su ga čuli da to govori povjeruju u njega.

Isus i Abraham

31Tada Isus reče Židovima koji su mu povjerovali: “Uistinu ste moji učenici ako živite onako kako vam kažem. 32Upoznat ćete istinu, a istina će vas osloboditi.”

33“Ali mi smo Abrahamovi potomci”, kazaše oni. “Nikad nismo nikome robovali. Kako to misliš—‘oslobodit će vas’?”

34Isus im odgovori: “Svi ste vi robovi grijeha. 35Rob nema stalnog mjesta u obitelji, ali sin joj zauvijek pripada. 36Ako vas, dakle, Sin oslobodi, zaista ćete biti slobodni. 37Znam da ste Abrahamovi potomci, ali ipak me neki od vas žele ubiti jer moja riječ ne nalazi odjeka u vašim srcima. 38Govorim vam ono što sam vidio kad sam bio kod Oca. Ali vi ipak slijedite savjet svojega oca.”

39“Naš je otac Abraham”, odgovore oni. “Da vam je Abraham otac,” reče im Isus, “slijedili biste njegov dobar primjer.8:39 U nekim rukopisima: Ako ste djeca Abrahamova, slijedite njegov primjer. 40Umjesto toga, pokušavate me ubiti—samo zato što sam vam govorio istinu koju sam čuo od Boga. Takvo što Abraham nikad nije učinio! 41Ne; kad tako postupate, slušate svojega pravog oca.” “Nismo mi rođeni iz preljuba—naš pravi otac je sâm Bog”, odgovore mu.

42Isus im reče: “Kad bi bilo tako, voljeli biste i mene jer sam od Boga izišao i došao k vama. Nisam sâm došao, nego me je on poslao. 43Zašto ne možete shvatiti što vam govorim? Zato što niste kadri slušati moju riječ. 44Jer vam je otac đavao, pa volite činiti zlo koje on čini. On je od početka ubojica i mrzi istinu, jer u njemu nema ni trunka istine. Kad laže, govori što je njegovo jer je lažac i otac laži. 45Zato meni ne vjerujete kad vam govorim istinu. 46Koji mi od vas može dokazati i jedan jedini grijeh? Ako vam govorim istinu, zašto mi ne vjerujete? 47Komu je Otac Bog, rado sluša Božje riječi. Vi ih ne slušate zato što niste njegova djeca.”

48“Nismo li mi dobro rekli da si Samarijanac i da si opsjednut zloduhom?”

49Isus reče: “Nisam ja opsjednut zloduhom, već poštujem svojeg Oca, a vi me prezirete. 50Ionako ne tražim da sebe proslavim. Bog tako želi i On je sudac. 51Zaista vam kažem, tko sluša moje riječi, nikada neće vidjeti smrti.”

52“Sad znamo da te opsjeo zloduh”, rekoše mu židovski vođe. “Abraham je umro kao i proroci, a ti pak tvrdiš da onaj koji sluša tvoje riječi neće vidjeti smrti! 53Zar si ti veći od našeg oca Abrahama, koji je umro? I od proroka, koji su pomrli? Pa kime se ti praviš?”

54Isus im tada reče: “Hvalim li sâm sebe, to ništa ne vrijedi—no mene proslavlja moj Otac. Za njega vi tvrdite da je vaš Bog, 55a uopće ga ne poznajete. Ali ja ga poznajem. Kad bih rekao da ga ne poznajem, bio bih lažac kao i vi. No istina je da ga poznajem i da slušam njegove riječi. 56Vaš se otac Abraham radovao mojemu dolasku. Vidio ga je i jako se razveselio.”

57Židovski poglavari rekoše: “Nemaš još ni pedeset godina, a kažeš da si vidio Abrahama!”8:57 U nekim rukopisima: Kako možeš reći da te Abraham vidio?

58Isus im odvrati: “Zaista vam kažem, Ja jesam,8:58 Ja jesam ime je kojim je Bog sebe nazvao u Starome zavjetu. još prije nego što je Abraham i rođen.”8:58 U grčkome: …prije nego je Abraham postao, Ja jesam.

59Nato židovski poglavari pograbe kamenje da ga ubiju, ali Isus kradomice iziđe iz Hrama.