Yohane 14 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 14:1-31

Yesu Atonthoza Ophunzira Ake

1“Mtima wanu usavutike. Khulupirirani Mulungu; khulupirirani Inenso. 2Mʼnyumba mwa Atate anga muli zipinda zambiri. Kukanakhala kuti mulibemo ndikanakuwuzani. Ine ndikupita kumeneko kukakukonzerani malo. 3Ndipo ndikapita kukakukonzerani malo, ndidzabweranso kudzakutengani, kuti kumene kuli Ineko, inunso mukakhale komweko. 4Inu mukudziwa njira ya kumene Ine ndikupita.”

Yesu Njira ya kwa Atate

5Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye ife sitikudziwa kumene Inu mukupita, nanga tingadziwe bwanji njirayo?”

6Yesu anayankha kuti, “Ine ndine njira, choonadi ndi moyo. Palibe munthu angafike kwa Atate popanda kudzera mwa Ine. 7Mukanandidziwadi Ine, mukanadziwanso Atate anga. Kuyambira tsopano, mukuwadziwa ndipo mwawaona.”

8Filipo anati, “Ambuye, tionetseni Atatewo ndipo ife tikhutitsidwa.”

9Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe Filipo, ndakhala pakati panu nthawi yonseyi ndipo iwe sukundidziwabe? Aliyense amene waona Ine, waonanso Atate. Tsono ukunena bwanji kuti, ‘Tionetseni Atate?’ 10Kodi sukukhulupirira kuti Ine ndili mwa Atate, ndipo Atate ali mwa Ine? Mawu amene Ine ndiyankhula kwa inu si mawu anga okha koma ndi mawu Atate wokhala mwa Ine, amene akugwira ntchito yake. 11Khulupirirani Ine pamene ndi kuti Ine ndili mwa Atate ndipo Atate ali mwa Ine. Koma ngati si chomwecho, khulupiriranitu Ine chifukwa cha ntchito zanga zodabwitsa. 12Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene akhulupirira Ine adzachita zimene Ine ndakhala ndikuchita. Iye adzachita ngakhale zinthu zazikulu kuposa zimenezi, chifukwa ndikupita kwa Atate. 13Ndipo Ine ndidzachita chilichonse chimene inu mudzapempha mʼdzina langa kuti Atate alemekezedwe mwa Mwana. 14Ngati mudzapempha kanthu kalikonse mʼdzina langa, Ine ndidzachita.

Lonjezo la Mzimu Woyera

15“Ngati mundikonda Ine, sungani malamulo anga. 16Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina kuti izikhala nanu nthawi zonse. 17Nkhosweyo ndiye Mzimu wachoonadi. Dziko lapansi silingalandire Nkhosweyi chifukwa samuona kapena kumudziwa. Koma inu mumamudziwa pakuti amakhala nanu ndipo adzakhala mwa inu. 18Ine sindikusiyani nokha kuti mukhale ana amasiye. Ine ndidzabweranso kwa inu. 19Patsala nthawi yochepa dziko lapansi silidzandionanso koma inu mudzandiona. Popeza kuti Ine ndili ndi moyo, inunso mudzakhala ndi moyo. 20Tsiku limenelo inu mudzazindikira kuti Ine ndili mwa Atate, ndipo inu muli mwa Ine, ndipo Ine ndili mwa inu. 21Iye amene amadziwa malamulo anga ndi kuwasunga ndiye amene amandikonda. Wokonda Ine adzakondedwa ndi Atate wanga ndipo Inenso ndidzamukonda ndikudzionetsa ndekha kwa iye.”

22Kenaka Yudasi (osati Yudasi Isikarioti) anati, “Koma Ambuye, nʼchifukwa chiyani mukufuna kudzionetsa nokha kwa ife, osati ku dziko lapansi?”

23Yesu anamuyankha kuti, “Ngati wina aliyense andikonda Ine, adzasunga mawu anga. Atate wanga adzamukonda, ndipo Ife tidzabwera ndi kukhala naye. 24Iye amene sandikonda Ine sasunga mawu anga. Mawu awa amene mukumva si anga ndi a Atate amene anandituma Ine.

25“Ndayankhula zonsezi ndikanali nanu. 26Koma Nkhosweyo, Mzimu Woyera, amene Atate adzamutumiza mʼdzina langa adzakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo adzakukumbutsani zonse zimene ndinakuwuzani. 27Ine ndikukusiyirani mtendere. Ndikukupatsani mtendere wanga. Ine sindikukupatsani monga dziko lapansi limaperekera. Mtima wanu usavutike ndipo musachite mantha.

28“Inu munamva Ine ndikunena kuti, ‘Ine ndikupita ndipo ndidzabweranso kwa inu.’ Mukanandikonda, mukanasangalala kuti Ine ndikupita kwa Atate, pakuti Atate ndi wamkulu kuposa Ine. 29Ine ndakuwuzani tsopano zisanachitike, kuti zikadzachitika mudzakhulupirire. 30Ine sindiyankhulanso nanu zambiri nthawi yayitali popeza wolamulira dziko lapansi akubwera. Iye alibe mphamvu pa Ine, 31koma kuti dziko lapansi lizindikire kuti Ine ndimakonda Atate ndi kuti ndimachita zokhazokha zimene Atate wandilamulira Ine.

“Nyamukani; tizipita.”

Священное Писание

Иохан 14:1-31

Иса Масих – путь к Небесному Отцу

1– Пусть ничто не тревожит ваши сердца. Верьте во Всевышнего и верьте в Меня. 2В доме Моего Отца много комнат, и если бы это было не так, то разве Я сказал бы вам: «Я иду приготовить место для вас»?14:2 Или: «В доме Моего Отца много комнат, и Я иду приготовить место для вас. Но если бы это было не так, то Я сказал бы вам». 3И если сейчас Я пойду и приготовлю вам место, то после вернусь и возьму вас к Себе, чтобы и вы были там, где Я. 4Вы знаете путь туда, куда Я иду.

5Фома сказал Ему:

– Повелитель, мы не знаем, куда Ты идёшь, как же мы можем знать туда путь?

6Иса ответил:

– Я – путь, истина и жизнь. Никто не приходит к Отцу, как только через Меня. 7Если бы вы действительно знали Меня, вы бы знали и Моего Отца. И сейчас вы знаете Его и видели Его.

8Филипп сказал:

– Повелитель, покажи нам Отца, и этого нам будет достаточно.

9Иса ответил:

– Неужели ты не знаешь Меня, Филипп? Ведь Я уже столько времени среди вас! Кто видел Меня, тот видел и Отца. Как ты можешь говорить: «Покажи нам Отца»? 10Неужели вы не верите, что Я в Отце и Отец во Мне? Слова, которые Я вам говорю, не Мои слова. Это Отец, Который живёт во Мне, совершает Свою работу. 11Верьте Мне, когда Я говорю, что Я в Отце и Отец во Мне, или верьте, по крайней мере, по Моим делам. 12Говорю вам истину, кто верит в Меня, тот сможет делать то, что Я делаю. Он сможет сделать ещё больше, потому что Я возвращаюсь к Отцу. 13Я сделаю всё, чего бы вы ни попросили во имя Моё, чтобы Отец был прославлен через Сына. 14Чего ни попросите во имя Моё, Я то сделаю.

Иса Масих обещает Святого Духа

15– Если вы любите Меня, то будете исполнять Мои повеления. 16Я попрошу Отца, и Он даст вам другого Заступника14:16 Здесь Иса определённо говорит о Святом Духе, Духе истины (см. 14:17, 26; 15:26)., Который будет с вами всегда, – 17Духа истины. Мир не может принять Его, потому что не видит Его и не знает Его. Но вы знаете Его, потому что Он живёт с вами и в вас будет. 18Я не оставлю вас сиротами, Я вернусь к вам14:18 Вернее всего, Иса говорил о Своих явлениях ученикам после воскресения (см., напр., 20:19), но, возможно, Он имел в виду сошествие Святого Духа (см. Деян. 2:1-4), через Которого Он и сейчас присутствует среди Своих последователей (см. Рим. 8:9-10).. 19Ещё недолго, и мир Меня больше не увидит, но вы увидите Меня. Я живу, и поэтому вы тоже будете жить. 20В тот день вы узнаете, что Я в Моём Отце, а вы во Мне, и Я в вас. 21Кто хранит Мои повеления и исполняет их, тот и любит Меня. Того, кто любит Меня, полюбит Мой Отец, и Я тоже буду любить его и открою Себя ему.

22Тогда Иуда (не Искариот) сказал:

– Повелитель, но почему Ты хочешь открыть Себя только нам, а не всему миру?

23Иса ответил:

– Кто любит Меня, тот будет соблюдать слово Моё, и того полюбит Мой Отец, к тому Мы придём и будем жить у него. 24Тот, кто Меня не любит, не будет и соблюдать слов Моих. Слово же, которое вы слышите, – не Моё, оно принадлежит пославшему Меня Отцу.

25Всё это Я сказал вам, пока ещё нахожусь с вами. 26Заступник же, Святой Дух, Которого Отец пошлёт вам во имя Моё, научит вас всему и напомнит вам всё, о чём Я вам говорил. 27Я оставляю вам мир. Мой мир Я даю вам. Я даю вам не так, как даёт этот грешный мир. Пусть ничто не тревожит ваше сердце. Не бойтесь! 28Вы слышали, что Я сказал вам: «Я ухожу от вас, но Я опять возвращусь к вам». Если бы вы любили Меня, то радовались бы тому, что Я иду к Отцу, потому что Отец больше Меня. 29Говорю вам обо всём заранее, чтобы, когда это произойдёт, вы поверили Мне. 30Больше Я уже не буду говорить вам, потому что приближается сатана, князь этого греховного мира. У него нет власти надо Мной, 31но мир должен узнать, что Я люблю Отца и что Я делаю то, что Отец Мне повелел.

Вставайте, пойдём отсюда.