Yohane 10 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 10:1-42

Mʼbusa Wabwino ndi Nkhosa Zake

1“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani inu Afarisi, kuti munthu amene salowera pa khomo mʼkhola la nkhosa, koma amalowera pena pake ndi wakuba ndi wachifwamba. 2Munthu amene amalowera pa khomo ndi mʼbusa wankhosazo. 3Mlonda amamutsekulira khomo, ndipo nkhosa zimamvera mawu ake. Iye amaziyitana mayina nkhosa zakezo, nazitulutsa. 4Akazitulutsa nkhosa zake zonse, iye amazitsogolera, ndipo nkhosa zakezo zimamutsata chifukwa zimadziwa mawu ake. 5Koma nkhosazo sizidzatsatira mlendo. Izo zidzamuthawa chifukwa sizizindikira mawu a mlendo.” 6Yesu ananena mawu ophiphiritsawa, koma Afarisi sanazindikire zimene ankawawuza.

7Choncho Yesu anatinso, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Ine ndine khomo la nkhosa. 8Onse amene anadza ndisanabwere Ine ndi akuba ndi achifwamba, ndipo nkhosa sizinawamvere. 9Ine ndine khomo, aliyense amene alowa kudzera mwa Ine adzapulumuka. Iye adzalowa ndi kutuluka ndi kupeza msipu. 10Mbala sibwera chabe koma kuti idzabe, kupha ndi kuwononga. Ine ndabwera kuti iwo akhale ndi moyo, ndi kukhala nawo wochuluka.

11“Ine ndine Mʼbusa wabwino. Mʼbusa wabwino amataya moyo wake chifukwa cha nkhosa zake. 12Wantchito ndi mʼbusa amene nkhosazo si zake. Choncho, pamene aona mmbulu ukubwera, iye amazisiya nkhosazo ndi kuthawa. Ndipo mmbulu umagwira nkhosazo ndikuzibalalitsa. 13Munthuyo amathawa chifukwa ndi wantchito ndipo sasamalira chilichonse cha nkhosazo.

14“Ine ndine mʼbusa wabwino. Ine ndimazidziwa nkhosa zanga ndipo nkhosa zangazo zimandidziwa, 15monga momwe Atate amandidziwa Ine, ndiponso Ine kudziwira Atatewo. Ndimapereka moyo wanga chifukwa cha nkhosa. 16Ine ndili ndi nkhosa zina zimene sizili za gulu ili. Ine ndiyenera kuzibweretsanso. Izonso zidzamvera mawu anga, ndipo zidzakhala gulu limodzi ndi mʼbusa mmodzi. 17Nʼchifukwa chake Atate anga amandikonda, popeza Ine ndikupereka moyo wanga kuti ndiwutengenso. 18Palibe amene angawuchotse mwa Ine, koma ndikuwupereka mwakufuna kwanga. Ine ndili ndi ulamuliro wa kuwupereka ndi ulamuliro wakuwutenganso. Lamulo ili ndinalandira kwa Atate anga.”

19Pa mawu awa Ayuda anagawikananso. 20Ambiri a iwo anati, “Iye ndi wogwidwa ndi ziwanda ndi wamisala. Chifukwa chiyani mukumvera Iye?”

21Koma ena anati, “Awa si mawu a munthu wogwidwa ndi ziwanda. Kodi ziwanda zingathe bwanji kutsekula maso a wosaona?”

Kusakhulupirira kwa Ayuda

22Ku Yerusalemu kunali chikondwerero chokumbukira kupatulidwa kwa Nyumba ya Mulungu. Inali nthawi yozizira, 23ndipo Yesu ankayenda mʼbwalo la Nyumbayo ku malo a Solomoni. 24Ayuda anamuzungulira Iye akunena kuti, “Kodi iwe udzazunguza malingaliro athu mpaka liti? Ngati iwe ndi Khristu, tiwuze momveka.”

25Yesu anayankha kuti, “Ine ndimakuwuzani, koma inu simukhulupirira. Ntchito zimene ndikuchita mʼdzina la Atate anga zikundichitira umboni, 26koma inu simukhulupirira chifukwa simuli a gulu lankhosa zanga. 27Nkhosa zanga zimamva mawu anga, Ine ndimazidziwa, ndipo zimanditsata Ine. 28Ine ndimazipatsa moyo wosatha ndipo sizidzawonongeka. Palibe amene adzazikwatula mʼdzanja langa. 29Atate anga, amene anandipatsa Ine, ndi akulu kuposa onse. Palibe amene angazikwatule mʼdzanja la Atate anga. 30Ine ndi Atate ndife amodzi.”

31Ayuda anatolanso miyala kuti amugende Iye, 32koma Yesu anawawuza kuti, “Ine ndakuonetsani zinthu zambiri zabwino zodabwitsa kuchokera kwa Atate. Nʼchifukwa chiti mwa izi chimene mukundigendera?”

33Ayuda anayankha kuti, “Ife sitikukugenda chifukwa cha izi, koma popeza ukunyoza Mulungu, chifukwa iwe, munthu wamba, ukuti ndiwe Mulungu.”

34Yesu anawayankha kuti, “Kodi sizinalembedwa mʼmalamulo anu kuti, ‘Ine ndanena kuti ndinu milungu?’ 35Ngati anawatcha milungu anthu amene analandira mawu a Mulungu, pajatu Malemba sangasweke, 36nanga bwanji uyu amene Atate anamuyika padera monga wake weniweni ndi kumutuma ku dziko lapansi? Nanga ndi chifukwa chiyani mukundinena Ine kuti ndikuchita chipongwe? Kodi nʼchifukwa choti ndanena kuti, ‘Ine ndine Mwana wa Mulungu?’ 37Musandikhulupirire Ine ngati sindichita ntchito za Atate anga. 38Koma ngati Ine ndikuchita zimenezi, ngakhale kuti simundikhulupirira, khulupirirani ntchito zodabwitsazo, ndipo mudziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndiponso Ine ndili mwa Atate.” 39Iwo anafuna kumugwiranso koma anawapulumuka mʼmanja mwawo.

40Kenaka Yesu anabwereranso kutsidya la mtsinje wa Yorodani kumalo kumene Yohane ankabatiza mʼmasiku akale. Iye anakhala kumeneko 41ndipo anthu ambiri anabwera kwa Iye. Iwo anati, “Ngakhale kuti Yohane sanachite chizindikiro chodabwitsa, zonse zimene Yohane ananena za munthu uyu zinali zoona.” 42Ndipo pamalo amenewo ambiri anakhulupirira Yesu.

Bibelen på hverdagsdansk

Johannesevangeliet 10:1-42

Farisæerne beskrives som tyve og røvere

1Jesus fortsatte med at tale til farisæerne: „Det siger jeg jer: Enhver, som ikke går ind ad døren til fårefolden, men sniger sig ind på anden måde, er en tyv eller røver. 2Fårenes rigtige hyrde kommer altid hen til døren, 3og det er ham, dørvogteren lukker op for. Fårene kender hans stemme. Han kalder sine får ved navn og fører dem ud på græs. 4Når han har lukket alle sine får ud, går han foran dem, og fårene følger ham, fordi de kender hans stemme. 5Men de vil ikke følge efter en fremmed. Tværtimod, de vil flygte fra ham, fordi de ikke kender hans stemme.”

6Jesus brugte det billede på farisæerne, men de forstod ikke, hvad han mente.

7Derfor prøvede han at forklare det nærmere: „Det siger jeg jer: Jeg er døren til fårefolden. 8Fårene har ikke lyttet til de ‚hyrder’, som er kommet før mig, for de er tyve og røvere.

9Jeg er døren. De, der kommer ind i folden gennem mig, skal få det evige liv. De vil gå ud for at finde føde, og de vil komme hjem igen. 10Tyven kommer kun for at stjæle, slagte og ødelægge, men jeg er kommet, for at de skal have liv, ja overflod af liv.”

Den gode hyrde ofrer sit liv for fårene

11Jesus fortsatte: „Jeg er den gode hyrde. Den gode hyrde vover sit liv for at redde fårene. 12-13Men en, som er ansat til at vogte får, og altså ikke er fårenes ejer, han er ligeglad med, hvordan det går med fårene, for han tænker kun på at hytte sit eget skind. Når han ser ulven nærme sig, lader han fårene i stikken og flygter. Så går ulven til angreb og spreder fårene for alle vinde.

14Jeg er den gode hyrde. Jeg kender mine får, og de kender mig, 15ligesom Faderen kender mig, og jeg kender ham. Og jeg vil ofre mit liv for at redde fårene.

16Jeg har andre får, som ikke hører til i denne fold. Dem skal jeg også være hyrde for, og de vil adlyde mig. Alle fårene skal samles, så der bliver én hjord og én hyrde.

17-18Faderen elsker mig, fordi jeg adlyder den befaling, han har givet mig: at jeg skal ofre mit liv og siden få det igen. Ingen kan tage mit liv, men jeg ofrer det af egen fri vilje. Jeg har autoritet til at ofre mit liv, og jeg har autoritet til at tage det tilbage.”

19Disse ord førte igen til uenighed blandt de jødiske ledere. 20Mange sagde: „Han er besat, han er gal! Hvorfor hører I på ham?” 21Andre sagde: „Sådan taler en besat ikke. Kan onde ånder give blinde deres syn igen?”

De jødiske ledere forkaster Jesus som Messias

22-23Det blev vinter, og Jesus var igen på besøg i Jerusalem, denne gang under Hanukka10,22-23 Tempelindvielsesfesten. festen. Han gik omkring i den del af templet, som kaldes Salomons søjlegang. 24De jødiske ledere omringede ham og spurgte: „Hvor længe vil du holde os hen i uvished? Er du Messias, så sig det ligeud!”

25Jesus svarede: „Det har jeg allerede gjort, men I ville ikke tro mig. De undere, jeg gør i min Fars navn, er bevis nok. 26Men I tror mig ikke, fordi I ikke hører til blandt mine får. 27Mine får adlyder min stemme. Jeg kender dem, og de følger mig. 28Jeg giver dem evigt liv, og de skal aldrig gå fortabt. Ingen kan rive dem ud af min hånd. 29Min Far, som har givet mig dem, har større magt end nogen anden, og ingen kan rive dem ud af min Fars hånd. 30Jeg og Faderen, vi er ét.”

31Da begyndte de igen at samle sten op for at slå ham ihjel. 32Men han sagde: „Jeg har udført mange gode gerninger, som min Far har bedt mig om at gøre. Hvilken af dem er det, I vil stene mig for?”

33„Du skal ikke stenes for nogen god gerning,” svarede de. „Men du skal dø, fordi du håner Gud. Du er kun et menneske, men du gør dig til ét med Gud!”

34„Står der ikke i Skriften: ‚Jeg har kaldt jer guder’?10,34 Citat fra Sl. 82,6. I denne salme bruges ordet „guder” om de ledere og dommere, der var indsat af Gud til at udføre hans vilje.” spurgte Jesus. 35„Hvis altså Skriften, som ikke kan annulleres, kalder de mennesker ‚guder’, som Gud havde indsat til at gøre hans vilje, 36hvordan kan I så anklage mig, som Faderen har indsat og sendt til verden, og sige, at jeg håner Gud, fordi jeg siger, at jeg er Guds Søn? 37Hvis det ikke var min Fars gerninger, jeg gjorde, så skulle I ikke tro mig. 38Men når jeg nu gør hans gerninger, så tro i det mindste for gerningernes skyld, så I må kunne forstå og komme til den erkendelse, at Faderen er i mig og jeg er i ham.”

39De forsøgte derefter at fange ham, men han slap fra dem.

Mange almindelige mennesker kommer til tro på Jesus som Messias

40Jesus tog nu igen over til området øst for Jordanfloden, til det sted, hvor Johannes tidligere havde døbt. Der opholdt han sig et godt stykke tid, 41og mange mennesker flokkedes om ham. De sagde til hinanden: „Johannes udførte ganske vist ingen undere, men alt, hvad han sagde om denne mand, var sandt.” 42Og mange af dem kom til tro på Jesus.