Yohane 9 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 9:1-41

Yesu Achiritsa Munthu Wosaona Chibadwire

1Iye akuyendabe, anaona munthu wosaona chibadwire. 2Ophunzira ake anamufunsa Iye kuti, “Rabi anachimwa ndani, munthuyu kapena makolo ake, kuti iye abadwe wosaona?”

3Yesu anayankha kuti, “Sikuti iyeyu anachimwa kapena makolo ake, koma izi zinachitika kuti Mulungu aonetse ntchito zake mwa iyeyu. 4Ife tiyenera kugwira ntchito za Iye amene anandituma kukanali masana. Usiku ukubwera, pamene wina aliyense sadzagwira ntchito. 5Pamene Ine ndili mʼdziko lapansi, Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi.”

6Atanena izi, Iye anathira malovu pansi ndi kukanda dothi, napaka matopewo mʼmaso a munthuyo. 7Yesu anamuwuza iye kuti, “Pita kasambe mʼdziwe la Siloamu” (mawu awa akutanthauza Wotumidwa). Choncho munthuyo anapita ndi kukasamba ndipo anabwerako akupenya.

8Anzake ndi iwo amene anamuona iye poyamba akupempha anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene amapemphapempha uja?” 9Ena ananena kuti anali yemweyo.

Ena anati, “Ayi, sakuoneka ngati yemweyo.”

Koma iye mwini ananenetsa kuti, “Munthuyo ndine.”

10Iwo anafunsitsa kuti, “Kodi nanga maso ako anatsekuka bwanji?”

11Iye anayankha kuti, “Munthu wina wotchedwa Yesu anakanda dothi ndi kupaka mʼmaso anga. Iye anandiwuza kuti ndipite ku Siloamu ndi kukasamba. Choncho ndinapita kukasamba, ndipo ndikuona.”

12Iwo anamufunsa iye kuti, “Ali kuti munthu ameneyu?”

Iye anati, “Ine sindikudziwa.”

Afarisi Afufuza za Kuchiritsidwa Kwake

13Iwo anabwera naye munthu amene poyamba anali wosaona kwa Afarisi. 14Tsono linali la Sabata tsiku limene Yesu anakanda dothi ndi kutsekula maso a munthuyu. 15Choncho Afarisi anamufunsanso iye momwe analandirira kuona kwake. Munthuyo anayankha kuti, “Iye anapaka matope mʼmaso anga, ndipo ine ndinakasamba, ndipo ndikuona.”

16Ena a Afarisi anati, “Munthu uyu siwochokera kwa Mulungu, pakuti sasunga Sabata.”

Koma enanso anafunsa kuti, “Kodi munthu wochimwa angachite bwanji zizindikiro zodabwitsa ngati izi?” Choncho iwo anagawanika.

17Pomaliza iwo anatembenukiranso kwa munthu amene anali wosaona uja nati, “Kodi iwe unena chiyani za Iye poti ndi maso ako amene watsekula?”

Munthuyo anayankha kuti, “Iye ndi mneneri.”

18Ayuda sanakhulupirirebe kuti iye anali wosaona ndi kuti anayamba kuona kufikira atayitana makolo ake. 19Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu ndi mwana wanu? Kodi iyeyu ndi amene mukunena kuti anabadwa wosaona? Nanga zikutheka bwanji kuti akuona?”

20Makolo anayankha kuti, “Ife tikudziwa kuti ndi mwana wathu, ndipo tikudziwa kuti anabadwa wosaona. 21Koma sitidziwa zimene zachitika kuti tsopano azipenya. Amenenso wamupenyetsa sitikumudziwa. Mufunseni ndi wamkulu; iye adziyankhira yekha.” 22Makolo ake ananena izi chifukwa amaopa Ayuda, popeza Ayuda anatsimikiza kale kuti aliyense amene adzamuvomereza Yesu kuti anali Khristu adzatulutsidwa mʼsunagoge. 23Ichi ndi chifukwa chake makolo ake anati, “Mufunseni iye ndi wamkulu.”

24Iwo anamuyitanitsa kachiwiri munthu amene anali wosaonayo. Iwo anati, “Lemekeza Mulungu. Ife tikudziwa kuti munthu uyu ndi wochimwa.”

25Iye anayankha kuti, “Zakuti Iye ndi wochimwa kapena ayi, ine sindikudziwa. Ine ndikudziwa chinthu chimodzi. Ndinali wosaona koma tsopano ndikuona!”

26Kenaka anamufunsa kuti, “Kodi Iye anachita chiyani kwa iwe? Iye anatsekula motani maso ako?”

27Iye anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kale ndipo inu simunamvetsetse. Chifukwa chiyani mukufuna mumvenso? Mukufuna kuti inu mukhale ophunzira akenso?”

28Pamenepo anamunyoza ndipo anati, “Iwe ndiye ophunzira wa munthuyu! Ife ndife ophunzira a Mose! 29Ife tikudziwa kuti Mulungu anayankhula kwa Mose, koma za munthu uyu, ife sitikudziwa ngakhale kumene akuchokera.”

30Munthuyo anayankha kuti, “Tsopano izi ndi zodabwitsa! Inu simukudziwa kumene akuchokera, komabe iye watsekula maso anga. 31Ife tikudziwa kuti Mulungu samvera wochimwa. Iye amamvera munthu woopa Mulungu amene amachita chifuniro chake. 32Palibe amene anamvapo za kutsekula maso a munthu wobadwa wosaona. 33Ngati munthu uyu akanakhala wosachokera kwa Mulungu, palibe chimene Iye akanachita.”

34Pamenepo anayankha kuti, “Iwe unabadwa mu uchimo kotheratu; bwanji ukuyesa kutiphunzitsa ife!” Ndipo anamutulutsa kunja.

Kusaona kwa Uzimu

35Yesu anamva kuti anamutulutsa kunja ndipo pamene anamupeza anati, “Kodi ukukhulupirira Mwana wa Munthu?”

36Munthuyo anafunsa kuti, “Kodi, Ambuye, ameneyo ndi ndani? Ndiwuzeni kuti ndimukhulupirire Iye?”

37Yesu anati, “Iwe wamuona tsopano. Zoonadi ndiye amene akuyankhula nawe.”

38Pamenepo munthuyo anati, “Ambuye, ndikukhulupirira,” ndipo anamulambira Iye.

39Yesu anati, “Ndinabwera pansi pano kudzaweruza kuti osaona aone ndi openya asaone.”

40Afarisi ena amene anali pafupi naye anamva akunena izi ndipo anafunsa kuti, “Chiyani? Kodi ndife osaonanso?”

41Yesu anati, “Mukanakhala osaona, simukanachimwa; koma tsopano popeza mukuti mumaona, ndinu ochimwabe.”

Bibelen på hverdagsdansk

Johannesevangeliet 9:1-41

Jesus helbreder en blindfødt mand

1Da Jesus og disciplene senere gik omkring i byen, traf de en mand, som havde været blind fra fødslen. 2„Mester, hvorfor er den mand født blind?” spurgte disciplene. „Er det på grund af hans egne synder eller hans forældres?”

3„Ingen af delene,” svarede Jesus. „Men det, der er sket med ham, vil føre til, at Guds kraft bliver synliggjort. 4Så længe det endnu er ‚dag’, må jeg9,4 Nogle håndskrifter siger „vi”. gøre de gerninger, som Gud har lagt til rette for mig. Der kommer en ‚nat’, hvor ingen kan arbejde. 5Mens jeg er i verden, er jeg verdens Lys.”

6Derefter spyttede Jesus på jorden, lavede mudder af spyttet, smurte det på den blinde mands øjne 7og sagde til ham: „Gå hen og vask dig i den dam, der kaldes Shiloa.” (Shiloa betyder „udsendt”). Manden gik så hen og vaskede sig, og da han kom tilbage, kunne han se.

8Hans naboer og andre, der kendte ham som den blinde tigger, sagde: „Er det ikke ham, der sad og tiggede?” 9„Jo, det må være ham,” mente nogle. Andre sagde: „Nej, det må være en, der ligner ham.”

„Det er mig!” sagde manden.

10„Hvordan er du kommet til at se?” spurgte folk.

11„En mand ved navn Jesus lavede noget mudder og smurte det på mine øjne,” svarede han. „Og så sagde han, at jeg skulle gå hen og vaske det af i Shiloa-dammen. Da jeg havde gjort det, kunne jeg se.”

12„Hvor er den mand henne nu?” spurgte folk.

„Det ved jeg ikke,” svarede han.

Forhøret hos farisæerne

13Så tog de manden, som havde været blind, med hen til farisæerne. 14Da helbredelsen var foregået på en sabbat, 15forhørte farisæerne ham om, hvordan han var kommet til at se. Han forklarede, hvordan Jesus havde smurt mudder på hans øjne og bedt ham vaske det af. Da han havde gjort det, kunne han se.

16„Den mand er ikke sendt af Gud,” sagde nogle af farisæerne, „han overholder jo ikke sabbatten.” Men andre sagde: „Hvordan skulle en synder kunne gøre sådan et mirakel?” De var meget uenige om, hvad de skulle mene om Jesus.

17Derfor spurgte de manden, der havde været blind: „Hvad mener du om ham? Det er jo dig, han har helbredt.”

„Han er en profet!” var svaret.

18De jødiske ledere nægtede nu at tro på, at manden havde været blind. Derfor blev hans forældre tilkaldt og krydsforhørt: 19„Er den mand her jeres søn, som I påstår er født blind? Hvordan kan det så være, at han kan se nu?”

20„Ja, det er vores søn. Og det er rigtigt, at han er født blind. 21Men hvordan det er gået til, at han nu kan se, eller hvem der er årsag til det, det kan vi ikke sige noget om. Spørg ham selv! Han er gammel nok til selv at svare.” 22-23De svarede på den måde, fordi de var bange for de jødiske ledere, som havde vedtaget, at hvis nogen sagde, at Jesus var Messias, skulle de udelukkes fra synagogen.

24For anden gang tilkaldte farisæerne manden, der havde været blind, og sagde til ham: „Giv Gud æren! Vi ved jo, at han, der helbredte dig, er et syndigt menneske.”

25„Om han er en synder, det ved jeg ikke,” svarede manden, „men én ting ved jeg: Før var jeg blind, og nu kan jeg se!”

26„Jamen, hvordan gjorde han det?” spurgte de. „Hvordan fik han dig til at se?”

27„Det har jeg jo lige fortalt jer!” udbrød manden. „I hørte måske ikke efter? Hvorfor vil I ellers høre det igen? I vil da ikke være hans disciple, vel?”

28Så skældte de ham ud: „Du kan selv være hans discipel! Vi er disciple af Moses. 29Vi ved, at Gud talte til Moses, men vi ved ikke, hvem den her mand er.”

30„Det var da mærkeligt,” svarede manden. „Han helbreder en blind, og I aner ikke, hvem han er. 31Mon Gud ville bønhøre ham, hvis han var et syndigt menneske? Nej, Gud bønhører dem, der viser ham ære og gør hans vilje. 32Har man nogensinde før hørt, at en blindfødt er blevet helbredt, så han kunne se? 33Hvis den mand ikke kom fra Gud, kunne han ikke have gjort det.”

34„Vil du nu til at belære os?” råbte de. „Du, som har været en synder hele dit liv!” Så jog de ham ud.9,34 Eller: „smed ham ud.” Måske betyder det, at han blev smidt ud af synagogens fællesskab.

Farisæernes blindhed

35Da Jesus hørte, hvordan manden var blevet smidt ud, opsøgte han ham og spurgte: „Tror du på Menneskesønnen?” 36„Mester, sig mig, hvem han er, så jeg kan tro på ham,” svarede manden. 37„Du har allerede set ham,” sagde Jesus. „For det er mig, der er Menneskesønnen.” 38„Herre, jeg tror!” svarede han og faldt på knæ foran Jesus.

39Da sagde Jesus: „Denne verden vil blive dømt, nu da jeg er kommet. De blinde bliver seende, men de seende bliver blinde.” 40Da nogle af de farisæere, som fulgte med Jesus, hørte det, sagde de: „Vil du måske påstå, at vi også er blinde?” 41Jesus svarede: „Havde I været blinde, ville I have været uden skyld. Men så længe I påstår, at I kan se, er I skyldige!”