Yobu 9 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 9:1-35

Mawu a Yobu

1Ndipo Yobu anayankha kuti,

2“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona.

Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?

3Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye,

Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.

4Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka.

Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?

5Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa,

ndipo amawagubuduza ali wokwiya.

6Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake

ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.

7Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala;

Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.

8Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba

ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.

9Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana,

nsangwe ndi kumpotosimpita.

10Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,

zodabwitsa zimene sizingawerengeke.

11Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona;

akadutsa, sindingathe kumuzindikira.

12Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa?

Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’

13Mulungu sabweza mkwiyo wake;

ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.

14“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji?

Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?

15Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe;

ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.

16Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera,

sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.

17Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho,

ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.

18Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso

koma akanandichulukitsira zowawa.

19Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi!

Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?

20Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa;

ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.

21“Ngakhale ine ndili wosalakwa,

sindidziyenereza ndekha;

moyo wanga ndimawupeputsa.

22Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti,

‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’

23Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi,

Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.

24Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa

Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo.

Ngati si Iyeyo, nanga ndani?

25“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro;

masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.

26Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja,

ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.

27Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga,

ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’

28ndikuopabe mavuto anga onse,

popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.

29Popeza ndapezeka kale wolakwa

ndivutikirenji popanda phindu?

30Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri

ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,

31mutha kundiponyabe pa dzala,

kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.

32“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha,

sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.

33Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu,

kuti atibweretse ife tonse pamodzi,

34munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine

kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!

35Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo,

koma monga zililimu, sindingathe.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 9:1-35

约伯的回应

1约伯回答说:

2“不错,我知道你所言不虚,

但人怎能在上帝面前算为义人?

3人若想与祂辩驳,

千次也不能胜一次。

4祂充满智慧,能力无比,

谁能抗拒祂还可平安无恙?

5祂可猝然挪动群山,

在怒气中把山翻倒。

6祂震动大地,使其挪位,

以致地的支柱摇撼。

7祂一声令下,

太阳便不再升起,

众星也不再发光。

8祂独自铺展穹苍,

步行在海浪之上。

9祂创造了北斗星、参星、昴星及南天的星座。

10祂行的奇事不可测度,

奇迹不可胜数。

11祂经过我身旁,我却看不见;

祂从旁边掠过,我也无法察觉。

12祂若夺取,谁能阻挡?

谁敢问祂,‘你做什么?’

13上帝不会忍怒不发,

海怪9:13 海怪”希伯来文是“拉哈伯”,下同26:12的帮手必屈膝在祂脚前。

14“因此,我怎敢与祂辩驳?

怎敢措辞与祂理论?

15我纵然无辜,也无法申诉,

只能乞求我的审判者施恩。

16即使我呼唤祂的时候,祂回应我,

我仍不相信祂会垂听我的声音。

17祂用暴风摧毁我,

无故地使我饱受创伤。

18祂不肯让我喘息,

祂使我尝尽苦头。

19若论力量,祂甚强大;

若上公堂,谁敢传祂?

20即使我清白无辜,我的口也会认罪;

即使我纯全无过,祂也会判我有罪。

21我虽纯全无过,也已毫不在乎,

我厌恶我的生命。

22因为,我认为都是一样,

纯全无过的人和恶人都会被祂毁灭。

23灾祸突然夺走人命时,

祂嘲笑无辜者的遭遇。

24大地落入恶人手中,

蒙敝审判官眼睛的不是祂是谁?

25“我的年日比信差还快,

匆匆而过,不见幸福。

26我的岁月疾驰如快船,

快如急降抓食的老鹰。

27即使我说要忘掉怨恨,

抛开愁容,强颜欢笑,

28诸多的患难仍使我惧怕,

我知道祂9:28 ”希伯来文是“你”,下同31节。不承认我无辜。

29既然我被定为有罪,

又何必徒然挣扎?

30即使我用雪水净身,

用碱水洗手,

31祂仍会把我扔进污坑,

连我的衣服也嫌弃我。

32祂并非我的同类,

我无法与祂争辩,一起对薄公堂。

33我俩中间没有仲裁者,

无人为我们断定是非9:33 为我们断定是非”希伯来文是“把手按在我们身上”。

34若能拿开祂责打我的刑杖,

使我不再受祂的惊吓,

35我就会放胆发言,不必对祂心存恐惧,

但现在我却不能这样9:35 但现在我却不能这样”或译“因为我知道自己的清白”。