Yobu 8 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 8:1-22

Mawu a Bilidadi

1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

2“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti?

Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.

3Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama?

Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?

4Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu,

Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.

5Koma utayangʼana kwa Mulungu,

ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,

6ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima

ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako

ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.

7Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa

koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.

8“Funsa kwa anthu amvulazakale

ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira

9pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse,

ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.

10Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera?

Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?

11Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho?

Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?

12Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula;

zimawuma msangamsanga kuposa bango.

13Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu;

ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.

14Kulimba mtima kwake kumafowoka;

zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.

15Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka;

amawugwiritsitsa koma sulimba.

16Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa,

nthambi zake zimatambalala pa munda wake;

17mizu yake imayanga pa mulu wa miyala

ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.

18Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo,

pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’

19Ndithudi chomeracho chimafota,

ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.

20“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa

kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.

21Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete

ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.

22Adani ako adzachita manyazi,

ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 8:1-22

比勒达发言

1书亚比勒达回答约伯说:

2“你要这样絮叨到何时?

你的话犹如阵阵狂风。

3上帝岂会歪曲正义?

全能者岂会颠倒是非?

4如果你的儿女得罪了祂,

祂会给他们应有的惩罚。

5但你若寻求上帝,

向全能者恳求;

6你若纯洁、正直,

祂必起身相助,

恢复你应有的家园。

7你起初虽然卑微,

日后必兴旺发达。

8“你要请教先辈,

探究祖先的经验。

9因为我们就像昨天才出生,一无所知,

我们在世的日子如同掠影。

10先辈必给你教诲和指点,

向你道出明智之言。

11“蒲草无泥岂可长高?

芦苇无水岂可茂盛?

12它们还在生长、尚未割下,

已比百草先枯萎。

13忘记上帝的人,结局也是如此;

不信上帝的人,盼望终必破灭。

14他所仰仗的虚若游丝,

他所倚靠的诚如蛛网。

15他倚靠它,它却支撑不住;

他抓紧它,它却支离破碎。

16他像阳光下生机勃勃的植物,

枝条爬满了园囿,

17根茎盘绕石堆,

深深扎入石缝。

18一旦他被连根拔起,

原处必否认见过他。

19他的生命就这样消逝8:19 他的生命就这样消逝”或译“这就是他一生的乐趣”。

地上会兴起其他人。

20“上帝决不会抛弃纯全的人,

也不会扶持邪恶的人。

21祂要使你笑口常开,

欢声不断。

22憎恨你的人必抱愧蒙羞,

恶人的帐篷必不复存在。”