Yobu 8 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 8:1-22

Mawu a Bilidadi

1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

2“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti?

Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.

3Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama?

Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?

4Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu,

Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.

5Koma utayangʼana kwa Mulungu,

ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,

6ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima

ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako

ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.

7Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa

koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.

8“Funsa kwa anthu amvulazakale

ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira

9pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse,

ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.

10Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera?

Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?

11Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho?

Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?

12Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula;

zimawuma msangamsanga kuposa bango.

13Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu;

ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.

14Kulimba mtima kwake kumafowoka;

zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.

15Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka;

amawugwiritsitsa koma sulimba.

16Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa,

nthambi zake zimatambalala pa munda wake;

17mizu yake imayanga pa mulu wa miyala

ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.

18Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo,

pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’

19Ndithudi chomeracho chimafota,

ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.

20“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa

kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.

21Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete

ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.

22Adani ako adzachita manyazi,

ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

New Russian Translation

Иов 8:1-22

Первая речь Билдада

Совет Билдада молиться Богу

1Тогда ответил Билдад из Шуаха:

2– Долго ли будешь ты так говорить?

Твои слова – буйный ветер!

3Разве Бог извращает суд?

Извращает ли Всемогущий правду?

4Если твои дети согрешили против Него,

Он отдал их во власть их греха.

5Но если ты воззовешь к Богу

и помолишься Всемогущему,

6если ты чист и праведен,

то и ныне поднимется Он для тебя

и вернет тебя на должное место.

7Прежнее тебе покажется ничтожным,

настолько велико будет твое будущее.

Жизнь нечестивых и праведников

8Спроси прежнее поколение,

рассмотри, что узнали их предки,

9ведь мы лишь вчерашние и ничего не знаем,

наши дни на земле – лишь тень.

10Неужели они не научат тебя, не наставят

и слов своей мудрости не изрекут?

11Растет ли папирус, где нет болот?

Поднимается ли тростник без влаги?

12Пока в цвету они и еще не срезаны,

но засыхают быстрее всех трав.

13Таков удел всех, кто забыл Бога,

и умирает надежда безбожников.

14Их упование непрочно,

их безопасность – паучья сеть.

15Обопрутся на сеть свою – она не выдержит,

схватятся – не удержит.

16Расцветают они под солнцем,

простирая ветви над садом;

17груду камней оплетая корнями,

пробиваются они меж камней8:17 Смысл этого места в еврейском тексте неясен..

18А когда их исторгнут с прежнего места,

само место от них отречется:

«Я никогда вас не видело».

19Вот вся радость их жизни!8:19 Или: «Посмотри, жизнь нечестивого испарится».

А из земли прорастут другие.

20Итак не отвергнет Бог беспорочного

и не поддержит руки злодея.

21Он наполнит еще смехом твои уста

и ликованием – губы твои.

22Враги твои облекутся в стыд,

и шатров нечестивых не станет.