Yobu 9 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 9:1-35

Mawu a Yobu

1Ndipo Yobu anayankha kuti,

2“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona.

Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?

3Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye,

Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.

4Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka.

Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?

5Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa,

ndipo amawagubuduza ali wokwiya.

6Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake

ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.

7Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala;

Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.

8Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba

ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.

9Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana,

nsangwe ndi kumpotosimpita.

10Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,

zodabwitsa zimene sizingawerengeke.

11Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona;

akadutsa, sindingathe kumuzindikira.

12Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa?

Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’

13Mulungu sabweza mkwiyo wake;

ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.

14“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji?

Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?

15Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe;

ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.

16Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera,

sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.

17Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho,

ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.

18Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso

koma akanandichulukitsira zowawa.

19Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi!

Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?

20Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa;

ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.

21“Ngakhale ine ndili wosalakwa,

sindidziyenereza ndekha;

moyo wanga ndimawupeputsa.

22Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti,

‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’

23Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi,

Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.

24Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa

Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo.

Ngati si Iyeyo, nanga ndani?

25“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro;

masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.

26Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja,

ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.

27Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga,

ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’

28ndikuopabe mavuto anga onse,

popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.

29Popeza ndapezeka kale wolakwa

ndivutikirenji popanda phindu?

30Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri

ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,

31mutha kundiponyabe pa dzala,

kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.

32“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha,

sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.

33Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu,

kuti atibweretse ife tonse pamodzi,

34munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine

kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!

35Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo,

koma monga zililimu, sindingathe.

New Russian Translation

Иов 9:1-35

Ответ Иова

Иов не в силах противостоять Богу

1Тогда Иов ответил:

2– Воистину, знаю, что это так.

Но будет ли смертный перед Богом прав?

3Если бы он захотел с Ним спорить,

не смог бы ответить ни на один из тысячи вопросов.

4Великий мудростью, крепкий силой –

кто с Ним спорил и остался цел?

5Он передвигает горы без ведома людей

и в Своем гневе рушит их.

6Он колеблет землю и сдвигает с места,

и основания ее дрожат.

7Он солнцу велит, и оно не светит;

печатью Он заключает звезды.

8Он один простирает небеса

и попирает волны морские.

9Он сотворил Большую Медведицу и Орион,

Плеяды и южные созвездия.

10Творит Он великое и непостижимое,

бессчетные чудеса.

11Вот, Он пройдет передо мной, а я Его не увижу,

пронесется мимо, а я Его не замечу.

12Вот, Он схватит, и кто Его остановит?

Кто скажет Ему: «Что ты делаешь?»

13Бог не станет удерживать Свой гнев;

Помощники Раава9:13 Раав – мистическое морское чудовище, символизирующее силы зла и разрушения. перед Ним падут.

14Как же мне спорить с Ним?

Где найти слова, чтобы Ему возразить?

15Пусть я и невиновен, я не смог бы ответить;

я бы мог лишь молить судью моего о милости.

16Если бы звал я, и Он ответил, –

не поверю, что Он выслушал бы меня.

17Тот, Кто налетает на меня, словно вихрь,

умножает мне раны безвинно;

18не дает мне дух перевести

и насыщает меня бедой.

19Если в силе дело, то Он могуч!

А если в правосудии, то кто приведет Его на суд?

20Пусть я невиновен – мои уста осудят меня;

если даже я безупречен, они вынесут мне приговор.

21Я безвинен, но мне уже все равно;

я презираю свою жизнь.

22Да, все одно, поэтому и говорю:

«Он губит и безвинного и нечестивого».

23Когда внезапно разит беда,

Он смеется отчаянию невинных.

24Когда страна в руках у нечестивых,

Он ослепляет ее судей.

Если не Он, то кто же?

Полное признание Иова в своей немощи

25Бегут мои дни быстрее гонца;

они улетают, не видя блага;

26ускользают прочь, как быстрые папирусные лодки,

как орлы, что падают на добычу.

27И даже если скажу: «Я позабуду жалобы,

изменю свой мрачный вид и улыбнусь»,

28я все равно боюсь своих страданий:

так как я знаю, что Ты не признаешь меня невинным.

29А раз я уже обвинен,

то зачем мне бороться впустую?

30Даже если вымоюсь снеговой водой9:30 Или: «с мылом».,

руки отмою щелоком,

31то и тогда Ты погрузишь меня в грязь,

что даже моя одежда мной побрезгует.

32Он не смертный, как я, чтобы мне ответить Ему,

чтобы сойтись нам в суде на тяжбу.

33Нет посредника между нами9:33 Или: «О если бы был между нами посредник».,

кто положил бы руку на нас обоих9:33 То есть «кто мог бы нас справедливо рассудить».,

34нет того, кто отвел бы Его жезл от меня,

чтобы Его ужас не терзал меня больше.

35Тогда я говорил бы, не страшась Его,

потому что сам по себе я не такой.