Yobu 41 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 41:1-34

1“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba

kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?

2Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake,

kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?

3Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo?

Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?

4Kodi idzachita nawe mgwirizano

kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?

5Kodi udzasewera nayo ngati mbalame,

kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?

6Kodi anthu adzayitsatsa malonda?

Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?

7Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga,

kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?

8Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo,

ndipo iweyo sudzabwereranso.

9Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza;

kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.

10Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa.

Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?

11Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere?

Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.

12“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho,

za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.

13Ndani angasende chikopa chake?

Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?

14Ndani angatsekule kukamwa kwake,

pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?

15Kumsana kwake kuli mizere ya mamba

onga zishango zolumikizanalumikizana;

16Mambawo ndi olukanalukana

kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.

17Ndi olumikizanalumikizana;

ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.

18Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali;

maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.

19Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo

mumathetheka mbaliwali zamoto.

20Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi

ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.

21Mpweya wake umayatsa makala,

ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.

22Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake;

aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.

23Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo

ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.

24Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala,

ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.

25Ngʼonayo ikangovuwuka,

ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.

26Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu,

ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.

27Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe

ndi mkuwa ngati chikuni chowola.

28Muvi sungathe kuyithawitsa,

miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.

29Zibonga zimakhala ngati ziputu;

imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.

30Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo

imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.

31Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali,

imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.

32Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee,

kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.

33Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho,

nʼcholengedwa chopanda mantha.

34Chimanyoza nyama zina zonse;

icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

Bibelen på hverdagsdansk

Jobs Bog 41:1-26

1Det er håbløst at forsøge at fange den.

Synet af den er nok til, at modet forsvinder.

2Når ingen tør kæmpe mod dette mægtige dyr,

hvem tør da kæmpe imod mig?

3Hvem tør sige, at jeg skylder dem noget?

Alt i hele verden tilhører mig.

4Lad mig beskrive Livjatans krop.

Den er velformet med enorme lemmer og vældig styrke.

5Hvem kan flå huden af den

eller trænge ind under dens panser?

6Hvem kan åbne munden på den,

så man ser de frygtindgydende tænder?

7Ryggen er dækket af rækker af plader,

der beskytter den fuldstændigt som skjolde.

8Pladerne sidder så tæt,

at intet kan trænge ind imellem dem.

9De overlapper hinanden,

og det er umuligt at skille dem ad.

10Når den fnyser, er det som lysglimt,

øjnene gløder som en solopgang.

11Flammer står ud af munden på den,

et fyrværkeri af gnister.

12Damp kommer ud ad dens næsebor

som fra en kedel med kogende vand.

13Dens ånde får kul til at gløde,

fra gabet spruder den ild.

14Halsmusklerne er utroligt stærke,

den skaber rædsel overalt, hvor den kommer.

15Dens bug er hård og fast,

den kan modstå ethvert angreb.

16Dens hjerte er hårdt som sten,

urokkeligt som en møllesten.

17Går den til angreb, gyser de stærkeste helte,

de løber rædselsslagne deres vej.

18Det er nytteløst at kæmpe imod den med sværd,

hverken spyd, pil eller lanse kan bruges.

19Den bøjer jernstænger, som var det strå,

bronze splintrer den som råddent træ.

20Pile kan ikke jage den på flugt,

og sten preller af som ingenting.

21Stridskøller har ingen virkning,

og kastespyd ler den blot ad.

22Dens bug er dækket af skarpe skæl,

som sætter dybe spor i jorden.

23Flodvandet pisker den i kog,

det bobler som i en gryde.

24Kølvandet er som en glinsende sti,

en stribe af sølvhvidt skum.

25Der findes ingen skabning på jorden,

der er så frygtløs som den.

26Den har intet at være bange for,

den er det stolteste dyr på jorden.”