1“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso
ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,
kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse
ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.
Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.
Pamene wabangula,
palibe chimene amalephera kuchita.
5Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa
Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’
ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.
Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8Zirombo zimakabisala
ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,
kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi
ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,
amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12Mulungu amayendetsa mitamboyo
mozungulirazungulira dziko lonse lapansi
kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,
kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14“Abambo Yobu, tamvani izi;
imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo
ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,
ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta
pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo
limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;
sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?
Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,
ndi kunyezimira mlengalenga,
kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;
Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;
pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,
kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
Guds uendelige storhed
1Det får mit hjerte til at banke voldsomt,
det hopper næsten helt op i halsen.
2Hør efter, når Gud taler fra stormvejret,
når hans tordenrøst ruller hen over os.
3Lynene glimter hen over himlen
og rækker helt til jordens ende.
4Derefter kommer tordenskraldet,
hans majestætiske, tordnende røst.
Han sparer ikke på lynene,
når han lader sin røst høre.
5Guds storslåede stemme høres i bulderet,
han gør store og ufattelige ting.
6Han befaler sneen at falde på jorden
og sender regnskyl i tykke tove.
7Folk må standse op midt i deres arbejde
og anerkende Guds vældige magt.
8Dyrene søger i skjul,
de bliver i deres huler.
9Den bidende blæst lukkes ud fra sit hus
og kommer med kulde fra nord.
10Gud ånder på vandet,
så overfladen fryser til is.
11Han fylder skyerne med vand,
og fra dem udspringer hans lyn.
12Skyerne farer frem og tilbage,
de bevæger sig efter hans vilje.
De udfører hans befalinger
ud over den vide jord,
13hvad enten lynet kommer for at straffe,
eller regnen kommer for at velsigne.
14Tænk dig om et øjeblik, Job,
læg mærke til Guds forunderlige gerninger.
15Ved du, hvordan han styrer naturens kræfter,
hvordan han får lynene til at glimte fra skyerne?
16Forstår du, hvordan skyerne kan svæve i luften?
Det er den Almægtiges underværker.
17Du, som lider under den brændende sol,
når søndenvinden bringer en hedebølge,
18var det dig, der hjalp ham udspænde himlens bue,
så den skinner som et spejl af blankt metal?
19Job, hvad med at dele noget af din visdom med Gud,
for vi andre ved jo ingenting!
20Tør du sige til Gud, at du vil fortælle ham noget?
Risikerer du ikke at dø ved at træde frem for ham?
21Når vinden har blæst skyerne væk,
og solen kommer frem i al sin skarphed,
kan intet menneske holde ud at se på dens strålende lys.
22Mod nord kan man se et gyldent skær,
men Guds herlighed er langt mere strålende.
23Vi kan ikke mødes på lige fod med den almægtige Gud,
for hans magt er uendelig.
Hans godhed er uden grænser,
og han kan umuligt være uretfærdig.
24Derfor har mennesker ærefrygt for ham,
men de selvretfærdige kan Gud ikke hjælpe.”