Yobu 34 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 34:1-37

1Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,

2“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru;

tcherani khutu inu anthu ophunzira.

3Pakuti khutu limayesa mawu

monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.

4Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera;

tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.

5“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa,

koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.

6Ngakhale ndine wolungama mtima,

akundiyesa wabodza;

ngakhale ndine wosachimwa,

mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’

7Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani,

amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?

8Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa;

amayanjana ndi anthu oyipa mtima.

9Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu

poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’

10“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu.

Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe,

Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.

11Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake;

Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.

12Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa,

kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.

13Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani?

Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?

14Mulungu akanakhala ndi maganizo

oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,

15zamoyo zonse zikanawonongekeratu

ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.

16“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi;

mvetserani zimene ndikunena.

17Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira?

Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?

18Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’

ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’

19Iye sakondera akalonga

ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka,

pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?

20Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku;

anthu amachita mantha ndipo amamwalira;

munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.

21“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu;

amaona mayendedwe ake onse.

22Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani

kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.

23Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu,

kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.

24Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu

ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.

25Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo

amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.

26Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo,

pamalo pamene aliyense akuwaona;

27Chifukwa anasiya kumutsata

ndipo sasamaliranso njira zake zonse.

28Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake,

kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.

29Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa?

Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe?

Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,

30kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza,

kuti asatchere anthu misampha.

31“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti,

‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,

32ndiphunzitseni zimene sindikuziona

ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’

33Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira,

pamene inu mukukana kulapa?

Chisankho nʼchanu, osati changa;

tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.

34“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana,

anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,

35‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru;

mawu ake ndi opanda fundo.’

36Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto

chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!

37Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira;

amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu,

ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

La Bible du Semeur

Job 34:1-37

Dieu est toujours juste

1Elihou reprit la parole et dit :

2O vous qui êtes sages, ╵écoutez mes paroles,

vous qui avez la connaissance ╵prêtez votre attention !

3Car l’oreille discerne ╵la valeur des paroles,

comme le palais juge ╵du goût des aliments.

4Choisissons donc pour nous le droit

et reconnaissons entre nous ╵ce qui est bien.

5Voici ce qu’a prétendu Job : ╵« Je suis dans mon bon droit34.5 Voir 10.15 ; 13.18.,

mais Dieu me refuse justice34.5 Voir 19.7 ; 27.2..

6Alors que je suis juste ╵je passe pour menteur34.6 Voir 10.17 ; 16.8..

Des flèches m’ont percé ╵me causant des plaies incurables ╵sans que j’aie commis de péché34.6 Voir 6.4 ; 16.13.. »

7Quel homme est comme Job,

pour boire l’insolence ╵comme on boirait de l’eau ?

8Il fait cause commune ╵avec les malfaiteurs

et marche en compagnie ╵de ceux qui sont méchants.

9N’a-t-il pas dit lui-même : ╵« L’homme ne gagne rien

à vouloir plaire à Dieu34.9 Voir 9.22-24 ; 21.7-34. » ?

10Aussi, écoutez-moi, ╵vous qui êtes sensés :

il est inconcevable ╵que Dieu fasse le mal,

et que le Tout-Puissant ╵pratique l’injustice,

11car il rend à chaque homme ╵selon ce qu’il a fait,

et il traite chacun ╵selon son attitude.

12Oh, non en vérité, ╵Dieu n’agit jamais mal,

jamais le Tout-Puissant ╵ne fausse la justice.

13Qui donc lui a confié ╵la charge de la terre

ou qui lui a remis ╵le soin du monde entier ?

14S’il portait sur lui-même ╵toute son attention,

s’il ramenait à lui ╵son Esprit et son souffle,

15toutes les créatures ╵expireraient ensemble ;

l’homme retournerait ╵aussi à la poussière.

16Si tu as du bon sens, ╵écoute donc ceci,

et sois bien attentif ╵à mes paroles.

17Un ennemi du droit ╵pourrait-il gouverner ?

Oses-tu condamner ╵le Juste, le Puissant ?

18Celui qui dit aux rois : ╵« Tu n’es qu’un scélérat »,

et qui traite les grands ╵de criminels,

19ne favorise pas les princes,

ni ne privilégie ╵le riche par rapport au pauvre.

Ils sont tous, en effet, ╵l’ouvrage de ses mains.

20En un instant, ils meurent :

au milieu de la nuit, ╵un peuple se révolte, ╵alors ils disparaissent ;

on dépose un tyran ╵sans qu’une main se lève,

21car Dieu observe ╵la conduite de l’homme,

et il a les regards ╵sur tous ses faits et gestes.

22Car il n’y a pour lui ╵aucune obscurité, ╵pas d’épaisses ténèbres

où pourraient se cacher ╵les artisans du mal.

23Oui, Dieu n’a pas besoin ╵d’épier longtemps un homme

pour le faire assigner ╵devant lui en justice.

24Sans une longue enquête, ╵il brise les tyrans

et met d’autres gens à leur place.

25Car il connaît leurs œuvres.

Aussi, en pleine nuit34.25 C’est-à-dire à l’improviste (voir v. 20)., ╵soudain, il les renverse, ╵les voilà écrasés.

26Comme des criminels,

il les frappe en public.

27Ils lui tournaient le dos

et ignoraient ╵toutes ses directives.

28Car ils ont fait monter vers lui ╵le cri des pauvres

et il a entendu ╵les cris des opprimés.

29S’il garde le silence34.29 Autre traduction : s’il donne le repos., ╵qui le condamnera ?

Et s’il cache sa face, ╵qui pourra le voir malgré tout ?

Pourtant, pour les nations et pour les hommes,

30Dieu fait en sorte d’empêcher ╵que règne un souverain impie

et qu’on tende des pièges au peuple.

31Cet homme va-t-il dire à Dieu :

« J’ai eu mon châtiment, ╵je ne me rendrai plus coupable.

32Ce que je ne vois pas, ╵toi, enseigne-le-moi.

Si j’ai commis des injustices, ╵je ne le ferai plus » ?

33Pour rétribuer un tel homme, ╵Dieu devrait-il consulter ton avis, ╵toi qui critiques ?

Si toi tu choisis de penser ainsi, ╵pour ma part, ce n’est pas mon cas34.33 Hébreu peu clair. Plus litt. : c’est toi qui choisis, pas moi. On peut comprendre de trois manières : 1. Elihou dit à Job : « C’est toi qui penses ainsi, mais ce n’est pas mon cas ». 2. Elihou dit à Job : « C’est à toi de choisir (de changer d’attitude), pas à moi ». 3. Elihou place ces paroles dans la bouche de Dieu : « Dieu devrait-il te dire : “c’est à toi de décider, pas à moi” ? ».

Allez, dis donc ce que tu sais !

34Les hommes de bon sens ╵aussi bien que les sages ╵qui m’auront entendu

conviendront avec moi :

35Job parle sans savoir

et ses paroles ╵manquent d’intelligence.

36Que son épreuve ╵aille jusqu’à son terme

puisqu’il répond ╵à la manière des injustes.

37Car il ajoute à son péché

et abonde en révolte parmi nous34.37 Autre traduction : Car, en plus de sa faute, voilà qu’il se révolte, il sème le doute parmi nous. ;

et puis il multiplie ╵ses propos contre Dieu.