Yobu 31 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 31:1-40

1“Ndinachita pangano ndi maso anga

kuti sindidzapenya namwali momusirira.

2Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani?

Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?

3Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa,

tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?

4Kodi Mulungu saona zochita zanga,

ndi kudziwa mayendedwe anga?

5“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso,

kapena kufulumira kukachita zachinyengo,

6Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama

ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,

7ngati mayendedwe anga asempha njira,

ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona,

kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.

8Pamenepo ena adye zimene ndinadzala,

ndipo zomera zanga zizulidwe.

9“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi,

ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,

10pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya,

ndipo amuna ena azigona naye.

11Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi,

tchimo loyenera kulangidwa nalo.

12Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko;

ukanapsereza zokolola zanga.

13“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi,

pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,

14ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa?

Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?

15Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo?

Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?

16“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba,

kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,

17ngati chakudya changa ndinadya ndekha,

wosagawirako mwana wamasiye,

18chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake,

ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,

19ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa,

kapena munthu wosauka alibe chofunda,

20ndipo ngati iyeyo sananditamandepo

chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,

21ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye,

poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,

22pamenepo phewa langa lipokonyeke,

mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.

23Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu,

ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.

24“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma

kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’

25ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri,

zinthu zimene manja anga anazipeza,

26ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala,

kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,

27ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo

nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,

28pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo,

chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.

29“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga,

kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,

30ine sindinachimwe ndi pakamwa panga

potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,

31ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti,

‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’

32Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse,

pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,

33ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena,

kubisa kulakwa mu mtima mwanga

34chifukwa choopa gulu la anthu,

ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko

kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.

35“Aa, pakanakhala wina wondimva!

Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe;

mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.

36Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa,

ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.

37Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita;

ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.

38“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine

ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,

39ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama

kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,

40pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu

ndi udzu mʼmalo mwa barele.”

Mawu a Yobu athera pano.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 31:1-40

约伯最后的申辩

1“我跟自己的眼睛立了约,

决不贪看女色。

2天上的上帝所定的是什么?

高天的全能者赐下什么产业?

3岂不是降灾难给不义之人,

降祸患给作恶的人?

4上帝岂不鉴察我走的路,

数算我的脚步?

5我何曾与虚假同行,

疾步追随诡诈?

6愿上帝把我放在公义的天平上称量,

让祂知道我的清白。

7倘若我的脚偏离正路,

贪图眼目之欲,

或手上粘着罪污,

8愿我种的庄稼被别人享用,

我田中的出产被连根拔起。

9我的心若迷恋女人,

在邻居的门口窥探,

10愿我妻子为别人推磨,

愿别人与她同房。

11因为这是大恶,

是当受审判的罪,

12是烧向灭亡的火焰,

会吞噬我所有家业。

13我的仆婢告我,

我也会讲公道,

14否则上帝追究,我怎么办?

祂审问我,我如何回答?

15祂创造了我,岂不也创造了他们?

岂不是同一位使我们在母腹中成胎?

16我何曾拒绝穷人的请求,

或使寡妇眼露失望之情,

17或独吞我的食物,

不与孤儿同享?

18我自幼就如父亲般抚养孤儿,

我自出母胎就照顾寡妇。

19倘若我见有人冻得要死,

或有穷人衣不蔽体,

20却没有把我的羊毛给他们御寒,

以致他们向我道谢;

21倘若我仗着在城门口有势力,

就动手欺负孤儿,

22情愿我的肩膀从肩胛脱落,

我的手臂从手肘折断。

23因为我惧怕上帝降灾祸,

我无法承担祂的威严。

24“我若仰仗金子,

依靠纯金,

25因财富充裕、

或家产丰足而欢喜;

26我若见太阳发光,

明月在天上移动,

27就暗自心生迷恋,

向它们吻手示敬,

28就是犯了当受审判的罪恶,

因为这等于我背弃了天上的上帝。

29“我何曾因敌人遭殃而欢喜,

因他们遇祸而快乐?

30我从未咒诅他们丧命,

以致我的口犯罪。

31住在我帐篷中的人,

谁没饱餐我的肉食呢?

32我的家门向路人敞开,

从未有旅客露宿街头。

33我何曾像亚当一样遮掩我的过犯,

将罪恶藏在怀中,

34因惧怕群众,

被族人藐视,

就默不作声、不敢出门?

35“但愿有人听我申诉!

看啊,我在这里画押,愿全能者回答我!

愿我的控诉者写好状词!

36我会把状词披在肩上,

如冠冕一般戴在头上。

37我会像王者一样到祂面前,

向祂交代我的一切所为。

38“若我的田地向我喊冤,

条条犁沟一同哭诉;

39若我白吃地的出产,

或使地的主人丧命,

40愿地长出蒺藜而非麦子,

长出杂草而非大麦。”

约伯的话说完了。